< Левит 14 >

1 И рече Господь к Моисею, глаголя:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 сей закон прокаженному, в оньже день аще очистится, и приведется к жерцу:
“Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
3 и да изыдет жрец вне полка, и узрит жрец, и се, исцеле язва прокажения от прокаженнаго:
Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
4 и повелит жрец, да возмутся очищенному два птичища жива чиста и древо кедрово, и соскана червленица и иссоп:
wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
5 и повелит жрец, да заколют птичище едино в сосуд глинян, над водою живою,
Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
6 и живое птичище да возмет, и древо кедрово и соскану червленицу и иссоп, и да омочит их и птичище живое в крови закланаго птичища над водою живою:
Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
7 и да воскропит на очистившагося от прокажения седмижды, и чист будет: и да отпустит птичище живое на поле:
Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
8 и да исперет очистивыйся ризы своя и да острижет вся власы своя и да измыется водою, и чист будет: и по сих да внидет в полк и да пребудет вне дому своего седмь дний.
“Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
9 И будет в день седмый, обриются вси власы его, глава его и брада и брови, и всяк влас его да обриется: и да измыет ризы своя, и да омыется тело его водою, и чист будет.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
10 И в день осмый да возмет два агнца единолетна непорочна и овцу едину единолетну непорочну, и три десятины муки пшеничны на жертву смешаныя с елеем и меру елеа едину:
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
11 и да поставит жрец очищаяй человека очищаемаго и сия пред Господем, у дверий скинии свидения:
Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
12 и возмет жрец агнца единаго и приведет его преступления ради, и чашу елеа, и отлучит я жрец во отлучение пред Господем:
“Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
13 и заколют агнца на месте идеже закалают всесожжения и яже греха ради, на месте святе: есть бо еже греха ради, якоже и преступления ради есть жерцу: святая святых суть:
Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
14 и возмет жрец от крове яже преступления ради, и возложит жрец на обушие уха очищаемаго деснаго, и на край руки его десныя, и на край ноги его десныя:
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
15 и взем жрец от чаши елеа, возлиет на руку левую свою:
Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
16 и да омочит жрец перст свой десный в елей, иже есть в руце его левей, и да воскропит от елеа перстом седмижды пред Господем:
aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
17 оставшийся же елей, иже в руце его, да возложит жрец на обушие уха очищаемаго деснаго, и на край руки его десныя, и на край ноги его десныя, на место крове яже преступления ради:
Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
18 оставшийся же елей, иже в руце жерца, да возложит жрец на главу очищенному: и помолится о нем жрец пред Господем:
Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
19 и сотворит жрец еже греха ради, и помолится жрец от очищающемся от греха своего: и по сем заколет жрец всесожжение:
“Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
20 и вознесет жрец всесожжение и жертву на олтарь пред Господем, и помолится о нем жрец, и очистится.
ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
21 Аще же убог есть, и рука его не достигнет, да возмет агнца единолетнаго единаго, в оньже преступил на отлучение, яко помолитися о нем, и десятину муки пшеничны смешаны с елеем в жертву, и чашу елеа едину,
“Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
22 и два горличища, или два птенца голубина, елика обрете рука его, и да будет един греха ради, и другий во всесожжение:
Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
23 и да принесет я в день осмый, во еже очистити его, к жерцу, пред двери скинии свидения пред Господа:
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
24 и взем жрец агнца иже преступления ради, и чашу елеа, возложит я возложение пред Господем,
Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
25 и заколет агнца иже преступления ради, и возмет жрец от крове яже преступления ради, и возложит на обушие уха очищаемаго деснаго, и на край руки его десныя, и на край ноги его десныя:
Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
26 и от елеа возлиет жрец на руку свою левую,
Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
27 и воскропит жрец перстом своим десным от елеа, иже в руце его левей, седмижды пред Господем:
ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
28 и возложит жрец от елеа сущаго в руце его на обушие уха очищаемаго деснаго, и на краи руки его десныя, и на край ноги его десныя, на месте крове яже преступления ради:
Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
29 оставшееся же от елеа, еже есть в руце жерца, да возложит на главу очистившемуся: и помолится о нем жрец пред Господем,
Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
30 и сотворит едину от горлиц, или от птенцев голубиных, якоже обрете рука его,
Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
31 едину греха ради, и другую во всесожжение с жертвою: и помолится жрец о очищаемем пред Господем.
imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
32 Сей закон в немже есть язва прокажения, и не обретающему рукою во очищение свое.
“Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
33 И рече Господь к Моисею и Аарону, глаголя:
“Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
34 егда внидете в землю Ханаанску, юже Аз даю вам в притяжание, и дам язву прокажения в домех земли притяжанныя вам:
Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
35 и приидет, егоже дом, и повесть жерцу глаголя: аки язва является в дому моем.
mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
36 И повелит жрец испразднити сосуды дому, прежде неже внити жерцу видети язву, и да не будут нечиста вся яже в дому. По сих же внидет жрец соглядати дом:
Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
37 и узрит жрец язву, и се, язва на стенах дому удолия зеленеющаяся или червленеющаяся, и обличие их худее стен:
Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
38 изшед жрец из дому к дверем дому, и отлучит жрец дом на седмь дний.
wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
39 И возвратится жрец в седмый день, и узрит дом, и се, разсыпася язва по стенам дому:
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
40 и повелит жрец, да изимут камение, на нихже есть язва, и да изнесут е вон из града на место нечисто:
wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
41 и да постружут извнутри дом окрест, и изсыплют персть состроганую вне града на место нечисто:
Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
42 и да возмут камение ино острогано, и вложат я вместо камения: и персть ину да возмут, и помажут дом.
Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
43 Аще же паки найдет язва, и явится в дому но изнесении камения и по острогании дому и по помазании,
“Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
44 и внидет жрец, и узрит аще разсыпася язва в дому, прокажение пребывающее есть в дому, нечист есть:
wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
45 и разорят дом, и древа его и камение его и всю персть дому изнесут вне града, на место нечисто.
Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
46 И входяй в дом вся дни, в няже есть отлучен, нечист будет до вечера:
“Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
47 и спяй в дому да исперет ризы своя и нечист будет до вечера: и ядый в дому да исперет ризы своя и нечист будет до вечера.
Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
48 Аще же пришедый внидет жрец, и увидит: и се, разсыпанием не разсыпася язва в дому но помазании дому, да очистит жрец дом, яко исцеле язва:
“Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
49 и возмет очистити дом, два птичища жива чиста и древо кедрово, и соскану червленицу и иссоп:
Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
50 и да заколет птичище едино в сосуд глинян над водою живою:
Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
51 и возмет древо кедрово и соскание червленое, и иссоп и птичище живое, и да омочит е в кровь птичища закланаго над водою живою, и да окропит ими в дому седмижды:
Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
52 и очистит дом кровию птичищною и водою живою, и птичищем живым и древом кедровым, и иссопом и сосканою червленицею:
Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
53 и да отпустит птичище живое вне града на поле и помолится о доме, и чист будет.
Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
54 Сей закон о всякой язве прокажения и вреда,
Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
55 и прокажения ризы и дому,
nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
56 и струпа, и знамения, и блещащагося,
khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
57 и поведати в оньже день нечисто, и в оньже день очистится: сей закон прокажения.
kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.

< Левит 14 >