< Книга Иисуса Навина 17 >

1 И быша пределы племене сынов Манассииных, яко сей первенец Иосифу, Махирови первенцу Манассиину, отцу Галаадову, (сей бо бысть муж храбр) в Галаадитиде и Васанитиде.
Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
2 И быша сыном Манассииным прочым по сонмом их: сыном Ахиезеровым и сыном Елековым и сыном Есриилевым, и сыном Сехемовым и сыном Семираеловым и сыном Оферовым: сии суть сынове Манассиины, сына Иосифова, мужеск пол по племеном своим.
Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
3 И Салпааду сыну Оферову, сына Галаадова, сына Махирова, сына Манассиина, не быша сыны, но токмо дщери: и сия имена дщерем Салпаадовым: Маала и Нуа, и Егла и Мелха и Ферса.
Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
4 И сташа пред Елеазаром жерцем и пред Иисусом сыном Навиным и пред князи, глаголющя: Бог заповеда рукою Моисеовою дати нам наследие посреде братии нашея. И дадеся им наследие повелением Господним, жребий в братии отца их.
Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
5 И паде жребий Манассию поле лавеково кроме земли Галаадовы и Васани, яже есть об ону страну Иордана,
Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
6 понеже дщери сынов Манассииных наследиша жребий посреде братий своих: земля же Галаадова бысть сыном Манассииным прочым.
chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
7 И быша пределы сынов Манассииных от Асир-Махфофа, и данаф, яже есть пред лицем Сихема, и идут пределы на Иамин и на Иасиф ко источнику Фаффоф.
Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
8 Манассию будет земля Фаффоф: и Фаффоф над пределы Манассииными сыном Ефремлим:
(Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
9 и снидут пределы к дебри Кана на юг по дебри Иарим: Теревинф Ефрему посреде града Манассиина. И пределы Манассиины к северу на водотечь, и будет исход его море:
Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
10 от юга Ефрему, и к северу Манассии, и будет море предел им: и ко Асиру совокупятся к северу, и Иссахару от восток.
Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
11 И будет Манассию (предел) между Иссахаром и между Асиром Вефсан и веси их, и Иевлаам и веси его, и живущыя в Доре и веси его, и живущыя в ендоре и веси его, и живущыя в Магедде и веси его, и живущыя в Танахе и веси его, и третия часть Нафефа и веси его.
Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
12 И не возмогоша сынове Манассиины потребити градов сих: и нача Хананей жити в земли сей.
Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
13 И бысть егда укрепишася сынове Израилевы, и сотвориша Хананеов послушных, потреблением же не потребиша их.
Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
14 Противореша же сынове Иосифовы Иисусу, глаголюще: почто наследствовал еси нас жребием единым и ужем единым? Аз же люд мног есмь, и благослови мя Бог (даже доселе).
Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
15 И рече им Иисус: аще люд мног еси, взыди в дубраву и отреби себе тамо место в земли Ферезеа и Рафаима, аще утесняет тя гора Ефремля.
Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
16 И реша сынове Иосифовы: не доволно нам горы Ефремли: и конь преизбранный и железо всему Хананею живущему в земли емек, в Вефсане и в весех ея, и во юдоле Иезраель.
Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
17 И рече Иисус к сыном Иосифовым, Ефрему и Манассию, глаголя: аще люд мног еси и силу велику имаши, не будет ти жребий един:
Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
18 зане дубрава будет тебе, понеже дубрава есть, и отребиши ю, и будет тебе, и концы ея, егда потребиши Хананеа, аще конь преизбранный ему есть: (и сам силен, ) ты бо пресилиши его.
dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”

< Книга Иисуса Навина 17 >