< От Иоанна святое благовествование 9 >

1 И мимоидый виде человека слепа от рождества.
Iye akuyendabe, anaona munthu wosaona chibadwire.
2 И вопросиша Его ученицы Его, глаголюще: Равви, кто согреши, сей ли, или родителя его, яко слеп родися?
Ophunzira ake anamufunsa Iye kuti, “Rabi anachimwa ndani, munthuyu kapena makolo ake, kuti iye abadwe wosaona?”
3 Отвеща Иисус: ни сей согреши, ни родителя его, но да явятся дела Божия на нем:
Yesu anayankha kuti, “Sikuti iyeyu anachimwa kapena makolo ake, koma izi zinachitika kuti Mulungu aonetse ntchito zake mwa iyeyu.
4 мне подобает делати дела Пославшаго Мя, дондеже день есть: приидет нощь, егда никтоже может делати:
Ife tiyenera kugwira ntchito za Iye amene anandituma kukanali masana. Usiku ukubwera, pamene wina aliyense sadzagwira ntchito.
5 егда в мире есмь, свет есмь миру.
Pamene Ine ndili mʼdziko lapansi, Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi.”
6 Сия рек, плюну на землю, и сотвори брение от плюновения, и помаза очи брением слепому,
Atanena izi, Iye anathira malovu pansi ndi kukanda dothi, napaka matopewo mʼmaso a munthuyo.
7 и рече ему: иди, умыйся в купели Силоамсте, еже сказается послан. Иде убо и умыся, и прииде видя.
Yesu anamuwuza iye kuti, “Pita kasambe mʼdziwe la Siloamu” (mawu awa akutanthauza Wotumidwa). Choncho munthuyo anapita ndi kukasamba ndipo anabwerako akupenya.
8 Соседи же и иже бяху видели его прежде, яко слеп бе, глаголаху: не сей ли есть седяй и просяй?
Anzake ndi iwo amene anamuona iye poyamba akupempha anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene amapemphapempha uja?”
9 Овии глаголаху, яко сей есть: инии же (глаголаху), яко подобен ему есть. Он (же) глаголаше, яко аз есмь.
Ena ananena kuti anali yemweyo. Ena anati, “Ayi, sakuoneka ngati yemweyo.” Koma iye mwini ananenetsa kuti, “Munthuyo ndine.”
10 Глаголаху же ему: како ти отверзостеся очи?
Iwo anafunsitsa kuti, “Kodi nanga maso ako anatsekuka bwanji?”
11 Отвеща он и рече: Человек нарицаемый Иисус брение сотвори и помаза очи мои и рече ми: иди в купель Силоамлю и умыйся. Шед же и умывся, прозрех.
Iye anayankha kuti, “Munthu wina wotchedwa Yesu anakanda dothi ndi kupaka mʼmaso anga. Iye anandiwuza kuti ndipite ku Siloamu ndi kukasamba. Choncho ndinapita kukasamba, ndipo ndikuona.”
12 Реша убо ему: кто Той есть? Глагола: не вем.
Iwo anamufunsa iye kuti, “Ali kuti munthu ameneyu?” Iye anati, “Ine sindikudziwa.”
13 Ведоша (же) его к фарисеом, иже бе иногда слеп.
Iwo anabwera naye munthu amene poyamba anali wosaona kwa Afarisi.
14 Бе же суббота, егда сотвори брение Иисус и отверзе ему очи.
Tsono linali la Sabata tsiku limene Yesu anakanda dothi ndi kutsekula maso a munthuyu.
15 Паки же вопрошаху его и фарисее, како прозре. Он же рече им: брение положи мне на очи, и умыхся, и вижу.
Choncho Afarisi anamufunsanso iye momwe analandirira kuona kwake. Munthuyo anayankha kuti, “Iye anapaka matope mʼmaso anga, ndipo ine ndinakasamba, ndipo ndikuona.”
16 Глаголаху убо от фарисей нецыи: несть Сей от Бога Человек, яко субботу не хранит. Овии глаголаху: како может человек грешен сицева знамения творити? И распря бе в них.
Ena a Afarisi anati, “Munthu uyu siwochokera kwa Mulungu, pakuti sasunga Sabata.” Koma enanso anafunsa kuti, “Kodi munthu wochimwa angachite bwanji zizindikiro zodabwitsa ngati izi?” Choncho iwo anagawanika.
17 Глаголаху (убо) слепцу паки: ты что глаголеши о Нем, яко отверзе очи твои? Он же рече, яко пророк есть.
Pomaliza iwo anatembenukiranso kwa munthu amene anali wosaona uja nati, “Kodi iwe unena chiyani za Iye poti ndi maso ako amene watsekula?” Munthuyo anayankha kuti, “Iye ndi mneneri.”
18 Не яша убо веры Иудее о нем, яко слеп бе и прозре, дондеже возгласиша родителя того прозревшаго
Ayuda sanakhulupirirebe kuti iye anali wosaona ndi kuti anayamba kuona kufikira atayitana makolo ake.
19 и вопросиша я, глаголюще: сей ли есть сын ваю, егоже вы глаголете, яко слеп родися? Како убо ныне видит?
Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu ndi mwana wanu? Kodi iyeyu ndi amene mukunena kuti anabadwa wosaona? Nanga zikutheka bwanji kuti akuona?”
20 Отвещаста (же) им родителя его и реста: вемы, яко сей есть сын наю и яко слеп родися:
Makolo anayankha kuti, “Ife tikudziwa kuti ndi mwana wathu, ndipo tikudziwa kuti anabadwa wosaona.
21 како же ныне видит, не вемы, или кто отверзе ему очи, мы не вемы: сам возраст имать, самого вопросите, сам о себе да глаголет.
Koma sitidziwa zimene zachitika kuti tsopano azipenya. Amenenso wamupenyetsa sitikumudziwa. Mufunseni ndi wamkulu; iye adziyankhira yekha.”
22 Сия рекоста родителя его, яко боястася Жидов: уже бо бяху сложилися Жидове, да, аще кто Его исповесть Христа, отлучен от сонмища будет:
Makolo ake ananena izi chifukwa amaopa Ayuda, popeza Ayuda anatsimikiza kale kuti aliyense amene adzamuvomereza Yesu kuti anali Khristu adzatulutsidwa mʼsunagoge.
23 сего ради родителя его рекоста, яко возраст имать, самого вопросите.
Ichi ndi chifukwa chake makolo ake anati, “Mufunseni iye ndi wamkulu.”
24 Возгласиша же вторицею человека, иже бе слеп, и реша ему: даждь славу Богу: мы вемы, яко Человек Сей грешен есть.
Iwo anamuyitanitsa kachiwiri munthu amene anali wosaonayo. Iwo anati, “Lemekeza Mulungu. Ife tikudziwa kuti munthu uyu ndi wochimwa.”
25 Отвеща убо он и рече: аще грешен есть, не вем: едино вем, яко слеп бех, ныне же вижу.
Iye anayankha kuti, “Zakuti Iye ndi wochimwa kapena ayi, ine sindikudziwa. Ine ndikudziwa chinthu chimodzi. Ndinali wosaona koma tsopano ndikuona!”
26 Реша же ему паки: что сотвори тебе? Како отверзе очи твои?
Kenaka anamufunsa kuti, “Kodi Iye anachita chiyani kwa iwe? Iye anatsekula motani maso ako?”
27 Отвеща им: рекох вам уже, и не слышасте: что паки хощете слышати? Еда и вы ученицы Его хощете быти?
Iye anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kale ndipo inu simunamvetsetse. Chifukwa chiyani mukufuna mumvenso? Mukufuna kuti inu mukhale ophunzira akenso?”
28 Они же укориша его и реша (ему): ты ученик еси Того: мы же Моисеовы есмы ученицы:
Pamenepo anamunyoza ndipo anati, “Iwe ndiye ophunzira wa munthuyu! Ife ndife ophunzira a Mose!
29 мы вемы, яко Моисеови глагола Бог, Сего же не вемы, откуду есть.
Ife tikudziwa kuti Mulungu anayankhula kwa Mose, koma za munthu uyu, ife sitikudziwa ngakhale kumene akuchokera.”
30 Отвеща человек и рече им: о сем бо дивно есть, яко вы не весте, откуду есть, и отверзе очи мои:
Munthuyo anayankha kuti, “Tsopano izi ndi zodabwitsa! Inu simukudziwa kumene akuchokera, komabe iye watsekula maso anga.
31 вемы же, яко грешники Бог не послушает, но аще кто Богочтец есть и волю Его творит, того послушает:
Ife tikudziwa kuti Mulungu samvera wochimwa. Iye amamvera munthu woopa Mulungu amene amachita chifuniro chake.
32 от века несть слышано, яко кто отверзе очи слепу рождену: (aiōn g165)
Palibe amene anamvapo za kutsekula maso a munthu wobadwa wosaona. (aiōn g165)
33 аще не бы был Сей от Бога, не могл бы творити ничесоже.
Ngati munthu uyu akanakhala wosachokera kwa Mulungu, palibe chimene Iye akanachita.”
34 Отвещаша и реша ему: во гресех ты родился еси весь, и ты ли ны учиши? И изгнаша его вон.
Pamenepo anayankha kuti, “Iwe unabadwa mu uchimo kotheratu; bwanji ukuyesa kutiphunzitsa ife!” Ndipo anamutulutsa kunja.
35 Услыша Иисус, яко изгнаша его вон, и обрет его, рече ему: ты веруеши ли в Сына Божия?
Yesu anamva kuti anamutulutsa kunja ndipo pamene anamupeza anati, “Kodi ukukhulupirira Mwana wa Munthu?”
36 Отвеща он и рече: и кто есть, Господи, да верую в Него?
Munthuyo anafunsa kuti, “Kodi, Ambuye, ameneyo ndi ndani? Ndiwuzeni kuti ndimukhulupirire Iye?”
37 Рече же ему Иисус: и видел еси Его, и Глаголяй с тобою Той есть.
Yesu anati, “Iwe wamuona tsopano. Zoonadi ndiye amene akuyankhula nawe.”
38 Он же рече: верую, Господи. И поклонися Ему.
Pamenepo munthuyo anati, “Ambuye, ndikukhulupirira,” ndipo anamulambira Iye.
39 И рече Иисус: на суд Аз в мир сей приидох, да невидящии видят, и видящии слепи будут.
Yesu anati, “Ndinabwera pansi pano kudzaweruza kuti osaona aone ndi openya asaone.”
40 И слышаша от фарисей сия сущии с Ним и реша Ему: еда и мы слепи есмы?
Afarisi ena amene anali pafupi naye anamva akunena izi ndipo anafunsa kuti, “Chiyani? Kodi ndife osaonanso?”
41 Рече им Иисус: аще бысте слепи были, не бысте имели греха: ныне же глаголете, яко видим, грех убо ваш пребывает.
Yesu anati, “Mukanakhala osaona, simukanachimwa; koma tsopano popeza mukuti mumaona, ndinu ochimwabe.”

< От Иоанна святое благовествование 9 >