< Псалми 31 >

1 У Тебе се, Господе, уздам; немој ме оставити под срамотом довека, по правди својој избави ме.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
2 Пригни к мени ухо своје, похитај, помози ми. Буди ми камени град, тврда ограда, где бих се спасао.
Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
3 Јер си Ти камена гора моја и ограда моја, имена свог ради води ме и управљај мном.
Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
4 Извади ме из мреже коју ми тајно заместише; јер си Ти крепост моја.
Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
5 У Твоју руку предајем дух свој; избављао си ме, Господе, Боже истинити!
Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
6 Ненавидим оне који поштују пропадљиве идоле; ја се у Господа уздам.
Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
7 Радоваћу се и веселити се о милости Твојој, кад погледаш на моју муку, познаш тугу душе моје,
Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
8 Не даш ме у руку непријатељу, поставиш ноге моје на пространом месту.
Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
9 Смилуј се на ме, Господе; јер ме је туга, од јада изнеможе око моје, душа моја и срце моје;
Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
10 Ишчиле у жалости живот мој, и године моје у уздисању; ослаби од муке крепост моја, и кости моје сасахнуше.
Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
11 Од мноштва непријатеља својих постадох подсмех и суседима својим, и страшило знанцима својим; који ме виде на улици беже од мене.
Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
12 Заборављен сам као мртав, нема ме у срцима; ја сам као разбијен суд.
Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
13 Јер слушам грдњу од многих, од свуда страх, кад се договарају на ме, мисле ишчупати душу моју.
Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
14 А ја се, Господе, у Тебе уздам и велим: Ти си Бог мој.
Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
15 У Твојој су руци дани моји; отми ме из руку непријатеља мојих, и од оних, који ме гоне.
Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
16 Покажи светло лице своје слузи свом; спаси ме милошћу својом.
Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
17 Господе! Немој ме оставити под срамотом; јер Тебе призивам. Нек се посраме безбожници, нека замукну и падну у пакао. (Sheol h7585)
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol h7585)
18 Нека онеме уста лажљива, која говоре на праведника обесно, охоло и с поругом.
Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
19 Како је много у Тебе добра, које чуваш за оне који Те се боје, и које дајеш онима који се у Те уздају пред синовима човечијим!
Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
20 Сакриваш их под кров лица свог од буна људских; склањаш их под сен од свадљивих језика.
Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
21 Да је благословен Господ, што ми показа дивну милост као да ме уведе у тврд град!
Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
22 Ја рекох у сметњи својој: Одбачен сам од очију Твојих; али Ти чу молитвени глас мој кад Те призвах.
Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
23 Љубите Господа сви свети Његови; Господ држи веру; и увршено враћа онима који поступају охоло.
Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
24 Будите слободни, и нека буде јако срце ваше, сви који се у Господа уздате.
Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

< Псалми 31 >