Aionian Verses
И сви синови његови и све кћери његове устадоше око њега тешећи га, али се он не даде утешити, него говораше: С тугом ћу у гроб лећи за сином својим. Па и његов отац плакаше за њим. (Sheol )
Ngakhale kuti ana ake onse aamuna ndi aakazi anasonkhana kudzamutonthoza, iye anakana kutonthozedwa. Iye anati, “Ayi. Ndidzalira mpaka ndidzapite kwa mwana wanga ku manda.” Choncho Israeli anapitirirabe kulira mwana wake. (Sheol )
А он рече: Неће ићи син мој с вама, јер је брат његов умро и он оста сам, па ако би га задесило како зло на путу на који ћете ићи, свалили би сте ме стара с тугом у гроб. (Sheol )
Koma Yakobo anati, “Mwana wanga sapita nanu kumeneko; mkulu wake anamwalira ndipo watsala yekha. Ngati choyipa chitamuchitikira pa ulendo mukupitawu, ndiye kuti ndi mmene ndakalambiramu inu mudzandipha ndi chisoni chotere.” (Sheol )
Ако и овог одведете од мене и задеси га како зло, свалићете ме старог у гроб с тугом. (Sheol )
Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol )
Умреће кад види да нема детета, те ће слуге твоје свалити старог слугу твог, а оца свог, с тугом у гроб. (Sheol )
ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol )
Ако ли шта ново учини Господ, и земља отвори уста своја и прождре их са свим што је њихово, и сиђу живи у гроб, тада знајте да су ови људи увредили Господа. (Sheol )
Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol )
И тако сиђоше са свим што имаху живи у гроб, и покри их земља и неста их из збора. (Sheol )
Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol )
Јер се огањ разгорео у гневу мом, и гореће до најдубљег пакла; спалиће земљу и род њен, и попалиће темеље брдима. (Sheol )
Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol )
Господ убија, и оживљује; спушта у гроб, и извлачи. (Sheol )
“Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol )
Болови гробни опколише ме, стегоше ме замке смртне. (Sheol )
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
Учини дакле по мудрости својој, и немој дати да се седа глава његова спусти с миром у гроб. (Sheol )
Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol )
Али му ти немој опростити, јер си мудар човек и знаћеш шта ћеш му учинити, да оправиш седу главу његову с крвљу у гроб. (Sheol )
Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol )
Као што се облак разилази и нестаје га, тако ко сиђе у гроб, неће изаћи, (Sheol )
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol )
То су висине небеске, шта ћеш учинити? Дубље је од пакла, како ћеш познати? (Sheol )
Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol )
О да ме хоћеш у гробу сакрити и склонити ме докле не утоли гнев Твој, и да ми даш рок кад ћеш ме се опоменути! (Sheol )
“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol )
Да бих се надао, гроб ће ми бити кућа; у тами ћу прострети постељу себи. (Sheol )
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol )
У гроб ће сићи, починуће са мном у гробу. (Sheol )
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol )
Проводе у добру дане своје, и за час силазе у гроб. (Sheol )
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol )
Као што суша и врућина граби воде снежне, тако гроб грешнике. (Sheol )
Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol )
Откривен је пакао пред Њим, нити има покривача погибли. (Sheol )
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol )
Јер мртви не спомињу Тебе; у гробу ко ће Те славити? (Sheol )
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol )
Вратиће се у пакао безбожници, сви народи који заборављају Бога; (Sheol )
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol )
Јер нећеш оставити душу моју у паклу, нити ћеш дати да Светац Твој види трулост. (Sheol )
chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol )
Опколише ме болести паклене, стегоше ме замке смртне. (Sheol )
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
Господе! Извео си из пакла душу моју, и оживео си ме да не сиђем у гроб. (Sheol )
Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol )
Господе! Немој ме оставити под срамотом; јер Тебе призивам. Нек се посраме безбожници, нека замукну и падну у пакао. (Sheol )
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol )
Али ће их као овце затворити у пакао, смрт ће им бити пастир; и ујутру ходиће по њима праведници, и облик њихов збрисаће пакао раставивши их с насељем. (Sheol )
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol )
Али ће Бог душу моју избавити из руку паклених; јер ме Он прима. (Sheol )
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol )
Нека их уграби смрт, нека живи сиђу у пакао, јер је злочинство у стану њиховом и у њима. (Sheol )
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol )
Јер је милост Твоја велика нада мном, и извадио си душу моју из пакла најдубљег. (Sheol )
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine; mwandipulumutsa ku malo ozama a manda. (Sheol )
Јер је душа моја пуна јада, и живот се мој примаче паклу. (Sheol )
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol )
Који је човек живео и није смрти видео, и избавио душу своју из руку паклених? (Sheol )
Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa? Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda? (Sela) (Sheol )
Опколише ме болести смртне, и јади паклени задесише ме, наиђох на тугу и муку; (Sheol )
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
Да изађем на небо, Ти си онде. Да сиђем у пакао, онде си. (Sheol )
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol )
Као кад ко сече и теше, тако се разлетеше кости наше до чељусти паклених. (Sheol )
Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol )
Прождрећемо их као гроб живе, и свеколике као оне који силазе у јаму; (Sheol )
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
Ноге јој силазе к смрти, до пакла допиру кораци њени. (Sheol )
Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol )
Кућа је њена пут паклени који води у клети смртне. (Sheol )
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )
А он не зна да су онде мртваци и у дубоком гробу да су званице њене. (Sheol )
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )
Пакао је и погибао пред Господом, а камоли срца синова човечијих. (Sheol )
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol )
Пут к животу иде горе разумноме да се сачува од пакла одоздо. (Sheol )
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol )
Ти га биј прутом, и душу ћеш му избавити из пакла. (Sheol )
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol )
Гроб и пропаст никада се не могу заситити, тако очи човечије никада нису сите. (Sheol )
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
Гроб, материца јалова, земља која не бива сита воде, и огањ, који не говори: Доста. (Sheol )
Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol )
Све што ти дође на руку да чиниш, чини по могућности својој, јер нема рада ни мишљења ни знања ни мудрости у гробу у који идеш. (Sheol )
Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol )
Метни ме као печат на срце своје, као печат на мишицу своју. Јер је љубав јака као смрт, и љубавна сумња тврда као гроб; жар је њен као жар огњен, пламен Божји. (Sheol )
Undiyike pamtima pako ngati chidindo, ngati chidindo cha pa dzanja lako; pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa, nsanje ndiyaliwuma ngati manda. Chikondi chimachita kuti lawilawi ngati malawi a moto wamphamvu. (Sheol )
Зато се раширио гроб и развалио ждрело своје превећ, и сићи ће у њ слава његова и мноштво његово и врева његова и који се веселе у њему. (Sheol )
Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake; mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka; adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko. (Sheol )
Ишти знак од Господа Бога свог, ишти оздо из дубине или озго с висине. (Sheol )
“Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol )
Пакао доле усколеба се тебе ради да те сретне кад дођеш, пробуди ти мртваце и све кнезове земаљске, диже с престола њихових све цареве народне. (Sheol )
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol )
Спусти се у пакао понос твој, звека псалтира твојих; прострти су пода те мољци, а црви су ти покривач. (Sheol )
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol )
А ти се у пакао сврже, у дубину гробну. (Sheol )
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol )
Што рекосте: Ухватисмо веру са смрћу, и уговорисмо с гробом; кад зађе бич као поводањ, неће нас дохватити, јер од лажи начинисмо себи уточиште, и за превару заклонисмо се; (Sheol )
Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol )
И вера ваша са смрћу уништиће се, и уговор ваш с гробом неће остати, а кад зађе бич као поводањ, потлачиће вас. (Sheol )
Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol )
Ја рекох, кад се пресекоше дани моји: Идем к вратима гробним, узе ми се остатак година мојих. (Sheol )
Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol )
Јер неће гроб Тебе славити, неће Те смрт хвалити, и који сиђу у гроб не надају се Твојој истини. (Sheol )
Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol )
Идеш к цару с уљем, с многим мирисима својим; шаљеш посланике своје далеко и понижујеш се до гроба. (Sheol )
Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol )
Овако вели Господ Господ: У који дан сиђе у гроб, учиних жалост, покрих бездану њега ради, и уставих реке њене, и велика вода стаде, и расцвелих за њим Ливан, и сва дрвета пољска повенуше за њим. (Sheol )
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene mkungudzawo unatsikira ku manda, ndinawuza nyanja kuti iwulire maliro pakuwuphimba. Ndinawumitsa mitsinje ndipo madzi ambiri anaphwa. Ndinabweretsa mdima pa Lebanoni chifukwa cha mtengowo ndipo mitengo yonse ya mʼdzikomo inawuma. (Sheol )
Праском падања његовог устресох народе, кад га свалих у гроб с онима који силазе у јаму; и утешише се на најдоњој страни земље сва дрвета едемска, што је најбоље и најлепше на Ливану, сва што се натапаху. (Sheol )
Mitundu ya anthu inagwedezeka pakumva mkokomo wa kugwa kwake, pamene ndinawutsitsira ku manda pamodzi ndi iwo amene anafa. Pamenepo ku dziko la akufa mitengo yonse ya ku Edeni pamodzi ndi ya ku Lebanoni yosankhidwa bwino inasangalatsidwa chifukwa cha zimenezi. (Sheol )
И они сиђоше с њим у гроб к онима што су побијени мачем, и мишица његова, и који сеђаху у хладу његовом међу народима. (Sheol )
Amene ankakhala mu mthunzi wake, amene ankayanjana nawo, iwonso anapita nawo pamodzi ku manda, kukakhala pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga pakati pa mitundu ya anthu. (Sheol )
Говориће му најхрабрији јунаци исред гроба с помоћницима његовим, који сиђоше и леже необрезани, побијени мачем. (Sheol )
Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol )
Али не леже међу јунацима који падоше између необрезаних, који сиђоше у гроб с оружјем својим, и метнуше мачеве под главе своје, и безакоње њихово лежи на костима њиховим, ако и беху јунаци страшни на земљи живих. (Sheol )
Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol )
Од гроба ћу их избавити, од смрти ћу их сачувати; где је, смрти, помор твој, где је, гробе, погибао твоја? Кајање ће бити сакривено од очију мојих. (Sheol )
“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol )
Да се закопају у најдоњи крај земље, оданде ће их узети рука моја; и да изађу на небо, оданде ћу их скинути; (Sheol )
Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol )
И рече: Завапих у невољи својој ка Господу, и услиши ме; из утробе гробне повиках, и Ти чу глас мој. (Sheol )
Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol )
А како вино вара, такав је човек охол, нити остаје у стану; јер раширује дух свој као гроб, и као смрт је, која се не може наситити и збира к себи све народе и скупља к себи сва племена. (Sheol )
Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol )
А ја вам кажем да ће сваки који се гневи на брата свог низашта, бити крив суду; а ако ли ко рече брату свом: Рака! Биће крив скупштини; а ко рече: Будало! Биће крив паклу огњеном. (Geenna )
Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena. (Geenna )
А ако те око твоје десно саблажњава, ископај га и баци од себе: јер ти је боље да погине један од удова твојих неголи све тело твоје да буде бачено у пакао. (Geenna )
Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna )
И ако те десна рука твоја саблажњава, одсеци је и баци од себе: јер ти је боље да погине један од удова твојих неголи све тело твоје да буде бачено у пакао. (Geenna )
Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna )
И не бојте се оних који убијају тело, а душу не могу убити; него се бојте Оног који може и душу и тело погубити у паклу. (Geenna )
Musamaope amene amapha thupi koma sangathe kuchotsa moyo. Koma muziopa Iye amene akhoza kupha mzimu ndi kuwononga thupi mu gehena. (Geenna )
И ти Капернауме! Који си се до небеса подигао до пакла ћеш пропасти: јер да су у Содому била чудеса што су у теби била, остао би до данашњег дана. (Hadēs )
Ndipo iwe Kaperenawo, kodi udzakwezedwa kufika kumwamba? Ayi, udzatsitsidwa mpaka pansi kufika ku Hade. Ngati zodabwitsa zimene zinachitika mwa iwe, zikanachitika mu Sodomu, bwenzi iye alipo kufikira lero. (Hadēs )
И ако ко рече реч на Сина човечијег, опростиће му се; а који рече реч на Духа Светог, неће му се опростити ни на овом свету ни на оном. (aiōn )
Aliyense amene anena mawu otsutsana ndi Mwana wa Munthu adzakhululukidwa koma aliyense wonena motsutsana ndi Mzimu Woyera sadzakhululukidwa mu mʼbado uno kapena umene ukubwerawo. (aiōn )
А посејано у трњу то је који слуша реч, но брига овог света и превара богатства загуше реч, и без рода остане. (aiōn )
Zimene zinafesedwa pakati pa minga, ndi munthu amene amamva mawu koma nkhawa za moyo uno ndi chinyengo cha chuma zimalepheretsa mawuwo kuti abale chipatso. (aiōn )
А непријатељ који га је посејао јесте ђаво; а жетва је последак овог века; а жетеоци су анђели. (aiōn )
Ndipo amene anafesa namsongole ndi Satana. Kukolola ndiko kutha kwa dzikoli ndipo otuta ndi angelo. (aiōn )
Као што се дакле кукољ сабира, и огњем сажиже, тако ће бити на крају овог века. (aiōn )
“Monga momwe namsongole azulidwa ndi kutenthedwa ndi moto, momwemonso kudzakhala pakutha kwa dziko. (aiōn )
Тако ће бити на полетку века: изићи ће анђели и одлучиће зле од праведних. (aiōn )
Umu ndi mmene kudzakhalira pakutha kwa dziko. Angelo adzabwera ndi kulekanitsa oyipa ndi olungama. (aiōn )
А и ја теби кажем: ти си Петар, и на овом камену сазидаћу цркву своју, и врата паклена неће је надвладати. (Hadēs )
Ndipo Ine ndikuwuza iwe kuti ndiwe Petro ndipo pa thanthwe ili Ine ndidzamangapo mpingo wanga ndipo makomo a ku gehena sadzawugonjetsa. (Hadēs )
Ако ли те рука твоја или нога твоја саблажњава, одсеци је и баци од себе: боље ти је ући у живот хром или кљаст, него ли с две руке и две ноге да те баце у огањ вечни. (aiōnios )
Ngati dzanja lako kapena phazi lako likuchimwitsa, lidule ndi kulitaya. Ndi bwino kwa iwe kulowa mʼmoyo wosatha wolumala kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri kapena mapazi awiri ndi kukaponyedwa ku moto wosatha. (aiōnios )
И ако те око твоје саблажњава, извади га и баци од себе: боље ти је с једним оком у живот ући, него с два ока да те баце у пакао огњени. (Geenna )
Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Ndi bwino kwa iwe kuti ukalowe ku moyo wosatha ndi diso limodzi kuposa ndi kukhala ndi maso awiri ndi kukaponyedwa ku moto wa gehena.” (Geenna )
И гле, неко приступивши рече Му: Учитељу благи! Какво ћу добро да учиним да имам живот вечни? (aiōnios )
Taonani mnyamata wina anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Aphunzitsi, ndi chinthu chiti chabwino chimene ndiyenera kuchita kuti ndipeze moyo wosatha?” (aiōnios )
И сваки, који остави куће, или браћу, или сестре, или оца, или матер, или жену, или децу, или земљу, имена мог ради, примиће сто пута онолико, и добиће живот вечни. (aiōnios )
Ndipo aliyense amene wasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena bambo kapena mayi kapena mkazi, kapena ana, kapena minda chifukwa cha Ine adzalandira madalitso ochuluka ndi kulandiranso moyo wosatha. (aiōnios )
И угледавши смокву једну крај пута дође к њој, и не нађе ништа на њој до лишће само, и рече јој: Да никад на теби не буде рода до века. И одмах усахну смоква. (aiōn )
Ataona mtengo wamkuyu mʼmbali mwa msewu, anapitapo koma sanapeze kanthu koma masamba okhaokha. Pamenepo anati kwa mtengowo, “Usadzabalenso chipatso!” Nthawi yomweyo mtengowo unafota. (aiōn )
Тешко вама књижевници и фарисеји, лицемери, што проходите море и земљу да би присвојили једног, и кад га присвојите, чините га сином пакленим, удвоје већим од себе. (Geenna )
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumayenda maulendo ambiri pa mtunda ndi pa nyanja kuti mutembenuze munthu mmodzi, ndipo akatembenuka, mumamusandutsa kukhala mwana wa gehena kawiri kuposa inu. (Geenna )
Змије, породи аспидини! Како ћете побећи од пресуде у огањ паклени? (Geenna )
“Njoka inu! Ana amamba! Mudzachithawa bwanji chilango cha gehena? (Geenna )
А кад сеђаше на гори Маслинској приступише к Њему ученици насамо говорећи: Кажи нам кад ће то бити? И какав је знак Твог доласка и краја века? (aiōn )
Pamene Yesu anakhala pansi pa phiri la Olivi, ophunzira ake anabwera kwa Iye mwamseri nati, “Tiwuzeni, kodi izi zidzachitika liti, ndipo chizindikiro cha kubwera kwanu ndi zizindikiro za kutha kwa dziko zidzakhala chiyani?” (aiōn )
Тада ће рећи и онима што Му стоје с леве стране: Идите од мене проклети у огањ вечни приправљен ђаволу и анђелима његовим. (aiōnios )
“Pamenepo adzanena kwa akumanzere kwake kuti, ‘Chokani kwa Ine, inu otembereredwa, pitani ku moto wosatha wokonzedwera mdierekezi ndi angelo ake. (aiōnios )
И ови ће отићи у муку вечну, а праведници у живот вечни. (aiōnios )
“Amenewa adzapita ku chilango chosatha pamene olungama ku moyo wosatha.” (aiōnios )
Учећи их да све држе што сам вам заповедао; и ево ја сам с вама у све дане до свршетка века. Амин. (aiōn )
ndi kuwaphunzitsa amvere zonse zimene ndinakulamulirani. Ndipo onani, Ine ndidzakhala pamodzi ndi inu kufikira kutha kwa dziko lapansi pano.” (aiōn )
А који похули на Духа Светог нема опроштења вавек, него је крив вечном суду. (aiōn , aiōnios )
koma aliyense amene achitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa pakuti wachita tchimo losatha.” (aiōn , aiōnios )
Али бриге овог света и превара богатства и остале сласти уђу и загуше реч, и без рода остане. (aiōn )
koma nkhawa zamoyo uno, chinyengo cha chuma ndi zokhumba za zinthu zina zimabwera ndi kutchinga mawu, ndipo amawachititsa kukhala osabala chipatso. (aiōn )
И ако те рука твоја саблажњава, одсеци је: боље ти је без руке у живот ући, неголи с обе руке ући у пакао, у огањ вечни, (Geenna )
Ngati dzanja lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo ndi dzanja limodzi kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri ndi kupita ku gehena, kumene moto wake suzima. (Geenna )
И ако те нога твоја саблажњава, одсеци је: боље ти је ући у живот хром, неголи с две ноге да те баце у пакао, у огањ вечни, (Geenna )
Ndipo ngati phazi lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo olumala kusiyana ndi kukhala ndi mapazi awiri ndi kuponyedwa mu gehena. (Geenna )
Ако те и око твоје саблажњава, ископај га: боље ти је с једним оком ући у царство Божје, неголи с два ока да те баце у пакао огњени, (Geenna )
Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi, kusiyana ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa mu gehena, (Geenna )
И кад изађе на пут, притрча неко, и клекнувши на колена пред Њим питаше Га: Учитељу благи! Шта ми треба чинити да добијем живот вечни? (aiōnios )
Yesu atanyamuka, munthu wina anamuthamangira nagwa mogwada pamaso pake. Iye anafunsa kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios )
А да неће примити сад у ово време сто пута онолико кућа, и браће, и сестара, и отаца, и матера, и деце, и земље, у прогоњењу, а на оном свету живот вечни. (aiōn , aiōnios )
adzalephera kulandira 100 (nyumba, abale, alongo, amayi, ana ndi minda, pamodzi ndi mazunzo) mʼbado uno ndi moyo wosatha nthawi ya mʼtsogolo. (aiōn , aiōnios )
И одговарајући Исус рече јој: Да одсад од тебе нико не једе рода довека. И слушаху ученици Његови. (aiōn )
Ndipo Iye anati kwa mtengo, “Palibe amene adzadyenso chipatso kuchokera kwa iwe.” Ndipo ophunzira ake anamva Iye akunena izi. (aiōn )
И цароваће у дому Јаковљевом вавек, и царству Његовом неће бити краја. (aiōn )
ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn )
Као што говори оцима нашим, Аврааму и семену његовом довека. (aiōn )
Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn )
Као што говори устима светих пророка својих од века (aiōn )
(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn )
И мољаху Га да им не заповеди да иду у бездан. (Abyssos )
Ndipo ziwandazo zimamupempha mobwerezabwereza kuti asazitumize ku dzenje la mdima. (Abyssos )
И ти, Капернауме! Који си се до небеса подигао до пакла ћеш пропасти. (Hadēs )
Kodi iwe Kaperenawo, adzakukweza mpaka kumwamba? Ayi, adzakutsitsa mpaka ku Malo a anthu akufa. (Hadēs )
И гле, устаде један законик и кушајући Га рече: Учитељу! Шта ћу чинити да добијем живот вечни? (aiōnios )
Nthawi ina katswiri wa malamulo anayimirira kuti ayese Yesu. Iye anati, “Aphunzitsi, ndichite chiyani kuti ndikhale ndi moyo wosatha?” (aiōnios )
Него ћу вам казати кога да се бојите: бојте се Оног који има власт пошто убије бацити у пакао; да, кажем вам, Оног се бојте. (Geenna )
Koma Ine ndidzakuonetsani amene muyenera kumuopa: Wopani Iye, amene pambuyo pakupha thupi, ali ndi mphamvu yakukuponyani ku gehena. Inde, Ine ndikuwuzani, muopeni Iye. (Geenna )
И похвали господар неверног пристава што мудро учини; јер су синови овог века мудрији од синова видела у свом нараштају. (aiōn )
“Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn )
И ја вама кажем: начините себи пријатеље неправедним богатством, да би вас кад осиромашите примили у вечне куће. (aiōnios )
Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios )
И у паклу кад беше у мукама, подиже очи своје и угледа издалека Авраама и Лазара у наручју његовом, (Hadēs )
Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs )
И запита Га један кнез говорећи: Учитељу благи! Шта да учиним да наследим живот вечни? (aiōnios )
Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios )
Који неће примити више у ово време, и на оном свету живот вечни. (aiōn , aiōnios )
adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn , aiōnios )
И одговарајући Исус рече им: Деца овог света жене се и удају; (aiōn )
Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. (aiōn )
А који се удостоје добити онај свет и васкрсење из мртвих нити ће се женити ни удавати; (aiōn )
Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. (aiōn )
Да ниједан који Га верује не погине, него да има живот вечни: (aiōnios )
kuti aliyense amene akhulupirira Iye akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios )
Јер Богу тако омиле свет да је и Сина свог Јединородног дао, да ниједан који Га верује не погине, него да има живот вечни. (aiōnios )
“Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi, kotero anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike koma akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios )
Ко верује Сина, има живот вечни; а ко не верује Сина, неће видети живот, него гнев Божји остаје на њему. (aiōnios )
Aliyense wokhulupirira Mwanayo ali ndi moyo wosatha, koma iye amene samvera Mwanayo sadzawuona moyo, pakuti mkwiyo wa Mulungu umakhala pa iye.” (aiōnios )
А који пије од воде коју ћу му ја дати неће ожеднети довека; него вода што ћу му ја дати биће у њему извор воде која тече у живот вечни. (aiōn , aiōnios )
koma aliyense amene adzamwa madzi amene Ine ndidzamupatsa sadzamvanso ludzu. Ndithudi, madzi amene ndidzamupatsa adzakhala kasupe wamadzi wotumphukira ku moyo wosatha.” (aiōn , aiōnios )
И који жње прима плату, и сабира род за живот вечни, да се радују заједно и који сеје и који жње; (aiōnios )
Ngakhale tsopano amene akukolola akulandira malipiro ake, ndipo akututa mbewu ku moyo wosatha kuti wofesa ndi wokolola asangalale pamodzi. (aiōnios )
Заиста, заиста вам кажем: Ко моју реч слуша и верује Ономе који је мене послао, има живот вечни, и не долази на суд, него је прешао из смрти у живот. (aiōnios )
“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene amamva mawu anga ndi kukhulupirira Iye amene ananditumiza Ine, ali ndi moyo wosatha ndipo sadzaweruzidwa. Iye wachoka mu imfa ndipo walowa mʼmoyo. (aiōnios )
Прегледајте писма, јер ви мислите да имате у њима живот вечни; и она сведоче за мене. (aiōnios )
Inu mumasanthula malemba chifukwa mumaganiza kuti mʼmalembamo muli moyo wosatha. Awa ndi malemba amene akundichitira umboni. (aiōnios )
Старајте се не за јело које пролази, него за јело које остаје за вечни живот, које ће вам дати Син човечији, јер овог потврди Отац Бог. (aiōnios )
Gwirani ntchito, osati chifukwa cha chakudya chimene chimawonongeka koma chifukwa cha chakudya chimene sichiwonongeka mpaka ku moyo wosatha, chimene Mwana wa Munthu adzakupatsani. Mulungu Atate anamusindikiza chizindikiro chomuvomereza.” (aiōnios )
А ово је воља Оног који ме посла да сваки који види Сина и верује Га има живот вечни; и ја ћу га васкрснути у последњи дан. (aiōnios )
Pakuti chifuniro cha Atate anga ndi chakuti aliyense amene aona Mwanayo namukhulupirira akhale ndi moyo wosatha, ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza.” (aiōnios )
Заиста, заиста вам кажем: који верује мене има живот вечни. (aiōnios )
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Iye amene akhulupirira ali nawo moyo wosatha. (aiōnios )
Ја сам хлеб живи који сиђе с неба; који једе од овог хлеба живеће вавек; и хлеб који ћу ја дати тело је моје, које ћу дати за живот света. (aiōn )
Ine ndine chakudya chamoyo chochokera kumwamba. Ngati munthu adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi zonse. Chakudya chimenechi ndi thupi langa, limene Ine ndidzalipereka kuti anthu pa dziko lapansi akhale ndi moyo.” (aiōn )
Који једе моје тело и пије моју крв има живот вечни, и ја ћу га васкрснути у последњи дан: (aiōnios )
Aliyense amene adya thupi langa ndi kumwa magazi anga ali ndi moyo wosatha ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza. (aiōnios )
Ово је хлеб који сиђе с неба: не као што ваши очеви једоше ману, и помреше; који једе хлеб овај живеће вавек. (aiōn )
Ichi ndiye chakudya chimene chinatsika kuchokera kumwamba. Makolo athu akale anadya mana ndi kufa, koma iye amene adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi yonse.” (aiōn )
Тада Му одговори Симон Петар: Господе! Коме ћемо ићи? Ти имаш речи вечног живота. (aiōnios )
Simoni Petro anamuyankha Iye kuti, “Ambuye, ife tidzapita kwa yani? Inu muli ndi mawu amoyo wosatha. (aiōnios )
А роб не остаје у кући вавек, син остаје вавек. (aiōn )
Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. (aiōn )
Заиста, заиста вам кажем: ко одржи реч моју неће видети смрт довека. (aiōn )
Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.” (aiōn )
Тада Му рекоше Јевреји: Сад видесмо да је ђаво у теби: Авраам умре и пророци, а ти говориш: Ко одржи реч моју неће окусити смрт довека. (aiōn )
Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ (aiōn )
Откако је света није чувено да ко отвори очи рођеном слепцу. (aiōn )
Palibe amene anamvapo za kutsekula maso a munthu wobadwa wosaona. (aiōn )
И ја ћу им дати живот вечни, и никад неће изгинути, и нико их неће отети из руке моје. (aiōn , aiōnios )
Ine ndimazipatsa moyo wosatha ndipo sizidzawonongeka. Palibe amene adzazikwatula mʼdzanja langa. (aiōn , aiōnios )
И ниједан који живи и верује мене неће умрети вавек. Верујеш ли ово? (aiōn )
Aliyense amene ali ndi moyo ndi kukhulupirira Ine sadzamwalira. Kodi iwe ukukhulupirira izi?” (aiōn )
Који љуби душу своју изгубиће је, а ко мрзи на душу своју на овом свету, сачуваће је за живот вечни. (aiōnios )
Munthu amene amakonda moyo wake adzawutaya, pamene munthu amene amadana ndi moyo wake mʼdziko lino lapansi adzawusungira ku moyo wosatha. (aiōnios )
Народ Му одговори: Ми чусмо из закона да ће Христос остати вавек; како ти говориш да се сину човечијем ваља подигнути? Ко је тај син човечији? (aiōn )
Gulu la anthu linayankha kuti, “Ife tinamva kuchokera mʼmalamulo kuti Khristu adzakhala kwamuyaya, nanga bwanji Inu mukunena kuti, ‘Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa?’ Kodi Mwana wa Munthuyu ndani?” (aiōn )
И знам да је заповест Његова живот вечни. Шта ја дакле говорим онако говорим као што ми рече Отац. (aiōnios )
Ine ndikudziwa kuti lamulo lake ndi moyo wosatha. Choncho chilichonse chimene Ine ndinena ndi chimene Atate andiwuza.” (aiōnios )
Рече Му Петар: Никад Ти нећеш опрати моје ноге. Исус му одговори: Ако те не оперем немаш део са мном. (aiōn )
Petro anati, “Ayi, Inu simudzandisambitsa konse mapazi anga.” Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine sindisambitsa mapazi ako, ulibe gawo mwa Ine.” (aiōn )
И ја ћу умолити Оца, и даће вам другог утешитеља да буде с вама вавек: (aiōn )
Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani Nkhoswe ina kuti izikhala nanu nthawi zonse. (aiōn )
Као што си Му дао власт над сваким телом да свему што си Му дао да живот вечни. (aiōnios )
Pakuti Inu munamupatsa Iye ulamuliro pa anthu onse kuti apereke moyo wosatha kwa onse amene mwamupatsa. (aiōnios )
А ово је живот вечни да познају Тебе јединог истинитог Бога, и кога си послао Исуса Христа. (aiōnios )
Tsono moyo wosathawo ndi uwu: Iwo akudziweni Inu, Mulungu yekhayo woona, ndi Yesu Khristu, amene Inu mwamutuma. (aiōnios )
Јер нећеш оставити душу моју у паклу, нити ћеш дати да Светац Твој види труљење. (Hadēs )
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs )
Предвидевши говори за васкрсење Христово да се не остави душа Његова у паклу, ни тело Његово виде труљење. (Hadēs )
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs )
Ког ваља дакле небо да прими до оног времена кад се све поправи, што Бог говори устима свих светих пророка својих од постања света. (aiōn )
Iye ayenera kukhalabe kumwamba mpaka nthawi ya kukonzanso zinthu zonse monga Mulungu analonjeza kale kudzera mwa aneneri ake oyera mtima. (aiōn )
А Павле и Варнава ослободивши се рекоше: Вама је најпре требало да се говори реч Божја; али кад је одбацујете, и сами се показујете да нисте достојни вечног живота, ево се обрћемо к незнабошцима. (aiōnios )
Ndipo Paulo ndi Barnaba anawayankha molimba mtima kuti, “Ife tinayenera kuyankhula Mawu a Mulungu kwa inu poyamba. Popeza inu mwawakana ndi kudziyesa nokha osayenera moyo wosatha, ife tsopano tikupita kwa anthu a mitundu ina. (aiōnios )
А кад чуше незнабошци, радоваху се и слављаху реч Божју, и вероваху колико их беше приправљено за живот вечни. (aiōnios )
Anthu a mitundu ina atamva izi, anakondwa ndipo analemekeza Mawu Ambuye; ndipo onse amene anawasankha kuti alandire moyo osatha anakhulupirira. (aiōnios )
Богу су позната од постања света сва дела Његова; (aiōn )
zinaululidwa kuyambira kalekale.’ (aiōn )
Јер шта се на Њему не може видети, од постања света могло се познати и видети на створењима, и Његова вечна сила и божанство, да немају изговора. (aïdios )
Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios )
Који претворише истину Божију у лаж, и већма поштоваше и послужише твар него Творца, који је благословен ва век. Амин. (aiōn )
Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Онима, дакле, који су трпљењем дела доброг тражили славу и част и нераспадљивост, живот вечни; (aiōnios )
Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. (aiōnios )
Да као што царова грех за смрт, тако и благодат да царује правдом за живот вечни, кроз Исуса Христа Господа нашег. (aiōnios )
Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu. (aiōnios )
А сад опростивши се од греха, и поставши слуге Божје, имате плод свој на посвећење, а крај живот вечни. (aiōnios )
Koma tsopano pakuti inu mwamasulidwa ku tchimo ndipo mwasanduka akapolo a Mulungu, phindu lomwe mulipeza ndi kuyera mtima ndipo chotsatira chake ndi moyo wosatha. (aiōnios )
Јер је плата за грех смрт, а дар Божји је живот вечни у Христу Исусу Господу нашем. (aiōnios )
Pakuti malipiro a tchimo ndi imfa, koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōnios )
Којих су и оци, и од којих је Христос по телу, који је над свима, Бог благословен ва век. Амин. (aiōn )
Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni. (aiōn )
Или: Ко ће сићи у бездан? То јест да изведе Христа из мртвих. (Abyssos )
“kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). (Abyssos )
Јер Бог затвори све у неверство, да све помилује. (eleēsē )
Pakuti Mulungu anasandutsa anthu onse a mʼndende ya kusamvera kuti Iye akaonetse chifundo kwa onse. (eleēsē )
Јер је од Њега и кроз Њега и у Њему све. Њему слава вавек. Амин. (aiōn )
Pakuti zinthu zonse nʼzochokera kwa Iye, nʼzolengedwa ndi Iye ndipo zimabweretsa ulemerero kwa Iye. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya! Ameni. (aiōn )
И не владајте се према овоме веку, него се промените обновљењем ума свог, да бисте могли кушати које је добра и угодна и савршена воља Божија. (aiōn )
Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro. (aiōn )
А ономе који вас може утврдити по јеванђељу мом и проповедању Исуса Христа, по откривењу тајне која је била сакривена од постања света, (aiōnios )
Tsopano kwa Iye amene ali ndi mphamvu yokhazikitsa monga mwa uthenga wanga wabwino ndikulalikidwa kwa Yesu Khristu, monga mwa vumbulutso lachinsinsi chobisika kwa nthawi yayitali, (aiōnios )
А сад се јавила и обзнанила кроз писма пророчка, по заповести вечног Бога, за послушање вере међу свима незнабошцима, (aiōnios )
koma tsopano chavumbulutsidwa ndi kudziwika kudzera mʼMalemba a uneneri mwa lamulo la Mulungu wosatha, kuti mitundu yonse ikhulupirire ndi kumvera Iye, (aiōnios )
Једином премудром Богу, кроз Исуса Христа, слава вавек. Амин. (aiōn )
kwa Mulungu yekhayo wanzeru kukhale ulemerero kwamuyaya kudzera mwa Yesu Khristu! Ameni. (aiōn )
Где је премудри? Где је књижевник? Где је препирач овог века? Не претвори ли Бог мудрост овог света у лудост? (aiōn )
Munthu wanzeru ali kuti? Munthu wozama ndi maphunziro ali kuti? Munthu wodziwa zakuya zamakono ali kuti? Kodi Mulungu sanazipusitse nzeru za dziko lapansi? (aiōn )
Али премудрост говоримо која је у савршенима, а не премудрост века овог ни кнезова века овог који пролазе. (aiōn )
Komabe ife timayankhula uthenga wa nzeru kwa okhwima, koma osati ndi nzeru ya mʼbado uno kapena ya olamula a mʼbado uno, amene mphamvu yawo ikutha. (aiōn )
Него говоримо премудрост Божију у тајности сакривену, коју одреди Бог пре света за славу нашу; (aiōn )
Ayi, ife timayankhula za nzeru yobisika ya Mulungu, nzeru imene inabisidwa ndipo imene Mulungu anatikonzera mu ulemerero wathu isanayambe nthawi. (aiōn )
Које ниједан од кнезова века овог не позна; јер да су је познали, не би Господа славе разапели. (aiōn )
Palibe olamulira aliyense wa mʼbado uno amene anamumvetsetsa popeza anakamumvetsetsa sakanamupachika Ambuye wa ulemerero. (aiōn )
Нико нека се не вара: ако ко међу вама мисли да је мудар на овом свету, нека буде луд да буде мудар. (aiōn )
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn )
Зато, ако јело саблажњава брата мог, нећу јести меса довека, да не саблазним брата свог. (aiōn )
Nʼchifukwa chake ngati zimene ine ndimadya zichititsa mʼbale wanga kugwa mu tchimo, sindidzadyanso chakudyacho kuti mʼbaleyo ndisamuchimwitse. (aiōn )
Ово се пак све догађаше угледи њима, а написа се за науку нама, на које последак света дође. (aiōn )
Zinthu izi zinawachitikira kuti zikhale chitsanzo ndipo zinalembedwa kuti zikhale chenjezo kwa ife, amene tiyandikira nthawi ya kutha kwa zonse. (aiōn )
Где ти је, смрти, жалац? Где ти је, пакле, победа? (Hadēs )
“Iwe imfa, kupambana kwako kuli kuti? Iwe imfa, ululu wako uli kuti?” (Hadēs )
У којима бог света овог ослепи разуме неверника, да им не засветли видело јеванђеља славе Христове, који је обличје Бога, који се не види. (aiōn )
Mulungu wa dziko lapansi anachititsa khungu anthu osakhulupirira, kuti asathe kuona kuwala kwa Uthenga Wabwino umene umaonetsa ulemerero wa Khristu, amene ndi chifaniziro cha Mulungu. (aiōn )
Јер наша лака садашња брига доноси нам вечну и од свега претежнију славу. (aiōnios )
Pakuti masautso athu ndi opepuka ndi a kanthawi, koma akutitengera ulemerero wamuyaya umene ndi wopambana kwambiri. (aiōnios )
Нама који не гледамо на ово што се види, него на оно што се не види; јер је ово што се види, за време, а оно што се не види, вечно. (aiōnios )
Motero sitiyangʼana zinthu zimene ndi zooneka ndi maso, koma zinthu zimene ndi zosaoneka. Pakuti zimene zimaoneka ndi zosakhalitsa, koma zimene sizioneka ndi zamuyaya. (aiōnios )
Јер знамо да кад се земаљска наша кућа тела раскопа, имамо зграду од Бога, кућу нерукотворену, вечну на небесима. (aiōnios )
Popeza tikudziwa kuti ngati msasa wa dziko lapansi umene tikukhalamo uwonongeka, tili ndi nyumba yochokera kwa Mulungu, nyumba yamuyaya yakumwamba, osati yomangidwa ndi manja a anthu. (aiōnios )
Као што је писано: Просу, даде сиромасима; правда његова остаје вавек. (aiōn )
Paja analemba kuti, “Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya.” (aiōn )
Бог и Отац Господа нашег Исуса Христа, који је благословен вавек, зна да не лажем. (aiōn )
Mulungu, Atate a Ambuye Yesu, amene tiyenera kumutamanda nthawi zonse, akudziwa kuti sindikunama. (aiōn )
Који даде себе за грехе наше да избави нас од садашњег света злог, по вољи Бога и Оца нашег, (aiōn )
Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn )
Коме слава ва век века. Амин. (aiōn )
Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Јер који сеје у тело своје, од тела ће пожњети погибао; а који сеје у дух, од духа ће пожњети живот вечни. (aiōnios )
Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. (aiōnios )
Над свим поглаварствима, и властима, и силама, и господствима, и над сваким именом што се може назвати, не само на овом свету него и на оном који иде. (aiōn )
Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. (aiōn )
У којима некад ходисте по веку овог света, по кнезу који влада у ветру, по духу који сад ради у синовима противљења; (aiōn )
mmene inu munkakhalamo pamene munkatsatira njira za dziko lapansi ndi za ulamuliro waufumu wa mlengalenga, mzimu umene ukugwira ntchito tsopano mwa amene samvera. (aiōn )
Да покаже у вековима који иду превелико богатство благодати своје добротом на нама у Христу Исусу. (aiōn )
ndi cholinga chakuti mʼnthawi imene ikubwera, Iyeyo adzaonetse chuma choposa cha chisomo chake, choonetsedwa mwa kukoma mtima kwake kwa ife mwa Khristu Yesu. (aiōn )
И да откријем свима шта је служба тајне од постања света сакривене у Богу, који је саздао све кроз Исуса Христа; (aiōn )
Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. (aiōn )
По наредби векова, коју учини у Христу Исусу, Господу нашем, (aiōn )
Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōn )
Ономе слава у цркви по Христу Исусу у све нараштаје ва век века. Амин. (aiōn )
Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Јер наш рат није с крвљу и с телом, него с поглаварима и властима, и с управитељима таме овог света, с духовима пакости испод неба. (aiōn )
Pakuti sitikulimbana ndi thupi ndi magazi, koma tikulimbana ndi maufumu, maulamuliro, mphamvu za dziko la mdima, ndi mphamvu zoyipa kwambiri zauzimu zamlengalenga. (aiōn )
А Богу и Оцу нашем слава ва век века. Амин. (aiōn )
Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Тајну која је била сакривена од постања света и нараштаја, а сад се јави светима Његовим, (aiōn )
chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn )
Који ће примити муку, погибао вечну од лица Господњег и од славе Његове, (aiōnios )
Adzalangidwa ndi chiwonongeko chamuyaya ndipo sadzaonanso nkhope ya Ambuye ndi ulemerero wamphamvu zake (aiōnios )
А сам Господ наш Исус Христос, и Бог и Отац наш, коме омилесмо и даде нам утеху вечну и наду добру у благодати, (aiōnios )
Ambuye athu Yesu Khristu mwini ndi Mulungu Atate wathu, amene anatikonda ife ndipo mwachisomo chake anatipatsa kulimba mtima kwamuyaya ndi chiyembekezo chabwino, (aiōnios )
Али тога ради ја бих помилован да на мени првом покаже све трпљење Исус Христос за углед онима који Му хоће веровати за живот вечни. (aiōnios )
Ndipo pa chifukwa chimenechi, Mulungu anandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwitsitsa, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse kuti ndikhale chitsanzo cha omwe angathe kumukhulupirira ndi kulandira moyo wosatha. (aiōnios )
А Цару вечном, Нераспадљивом, који се не види, једином премудром Богу част и слава ва век века. Амин. (aiōn )
Tsopano kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Бори се у доброј борби вере, мучи се за вечни живот на који си и позван, и признао си добро признање пред многим сведоцима. (aiōnios )
Menya nkhondo yabwino yachikhulupiriro. Gwiritsitsa moyo wosatha umene anakuyitanira pamene unavomereza bwino lomwe pamaso pa mboni zambiri. (aiōnios )
Који сам има бесмртност, и живи у светлости којој се не може приступити, ког нико од људи није видео, нити може видети, коме част и држава вечна. Амин. (aiōnios )
Ndiye yekha wosafa ndipo amakhala mʼkuwala koopsa. Mulungu amene munthu aliyense sanamuone. Kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu mpaka muyaya. Ameni. (aiōnios )
Богатима на овом свету заповедај да се не поносе нити уздају у богатство пропадљиво, него у Бога Живога, који нам све даје изобилно за ужитак; (aiōn )
Anthu onse amene ali ndi chuma uwalamule kuti asanyade kapena kuyika mitima yawo pa chuma chimene nʼchosadalirika. Koma chiyembekezo chawo chikhale mwa Mulungu amene amatipatsa mowolowamanja zonse zotisangalatsa. (aiōn )
Који нас спасе и призва звањем светим, не по делима нашим, него по својој наредби и благодати, која нам је дана у Христу Исусу пре времена вечних; (aiōnios )
Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. (aiōnios )
Зато трпим све избраних ради да и они добију спасење у Христу Исусу са славом вечном. (aiōnios )
Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha. (aiōnios )
Јер ме Димас остави, омилевши му садашњи свет, и отиде у Солун; Крискент у Галатију, Тит у Далмацију; Лука је сам код мене. (aiōn )
Paja Dema anandisiya chifukwa chokonda dziko lapansi lino, ndipo anapita ku Tesalonika. Kresike anapita ku Galatiya ndipo Tito anapita ku Dalimatiya. (aiōn )
И Господ ће ме избавити од сваког злог дела, и сачуваће ме за царство своје небеско; коме слава ва век века. Амин. (aiōn )
Ambuye adzandilanditsa ku chilichonse chofuna kundichita choyipa ndipo adzandisamalira bwino mpaka kundilowetsa chonse mu ufumu wake wakumwamba. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya. (aiōn )
За наду вечног живота, који обећа нелажни Бог пре времена вечних, (aiōnios )
ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. (aiōnios )
Учећи нас да се одрекнемо безбожности и жеља овог света, и да поштено и праведно и побожно поживимо на овом свету, (aiōn )
Chisomo chimatiphunzitsa kukana moyo osalemekeza Mulungu komanso zilakolako za dziko lapansi. Ndipo chimatiphunzitsa kukhala moyo odziletsa, olungama ndi opembedza Mulungu nthawi ino, (aiōn )
Да се оправдамо благодаћу Његовом, и да будемо наследници живота вечног по нади. (aiōnios )
kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. (aiōnios )
Јер може бити да се за то растаде с тобом на неко време да га добијеш вечно, (aiōnios )
Mwina chifukwa chimene unasiyana naye kwa kanthawi ndi chakuti ukhale nayenso nthawi zonse. (aiōnios )
говори и нама у последак дана ових преко сина, Ког постави наследника свему, кроз ког и свет створи. (aiōn )
Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. (aiōn )
А сину: Престо је Твој, Боже, ва век века; палица је правде палица царства Твог. (aiōn )
Koma za Mwana wake akuti, “Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya, ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu. (aiōn )
Као што и на другом месту говори: Ти си свештеник вавек по реду Мелхиседековом. (aiōn )
Ndipo penanso anati, “Iwe ndiwe wansembe mpaka muyaya, monga mwa unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn )
И свршивши све, постаде свима који Га послушаше узрок спасења вечног. (aiōnios )
Atasanduka wangwiro kotheratu, anakhala gwero la chipulumutso chosatha kwa onse omvera Iye. (aiōnios )
Науке крштења, и стављања руку, и васкрсења мртвих, и суда вечног. (aiōnios )
za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. (aiōnios )
И окусили добру реч Божју, и силу оног света, и отпали, (aiōn )
Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. (aiōn )
Где Исус уђе напред за нас, поставши поглавар свештенички довека по реду Мелхиседековом. (aiōn )
Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki. (aiōn )
Јер сведочи: Ти си свештеник вавек по реду Мелхиседековом. (aiōn )
Pakuti Mulungu anamuchitira umboni kuti, “Iwe ndi wansembe wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn )
Јер они без заклетве посташе свештеници; а Овај са заклетвом кроз Оног који Му говори: Закле се Господ и неће се раскајати: Ти си свештеник вавек по реду Мелхиседековом. (aiōn )
Koma Yesu ankakhala wansembe ndi lumbiro pamene Mulungu anati, “Ambuye analumbira ndipo sangasinthe maganizo ake, ‘Iwe ndi wansembe wamuyaya.’” (aiōn )
А Овај, будући да остаје вавек, има вечно свештенство. (aiōn )
Koma Yesu popeza ndi wamuyaya, unsembe wake ndi wosatha. (aiōn )
Јер закон поставља људе за свештенике који имају слабост; а реч заклетве које је речена по закону, постави сина вавек савршена. (aiōn )
Pakuti lamulo limasankha anthu amene ndi ofowoka kukhala akulu a ansembe; koma lumbiro, lomwe linabwera pambuyo pa lamulo, linasankha Mwana, amene anapangidwa kukhala wangwiro kwamuyaya. (aiōn )
Ни с крвљу јарчијом, нити телећом, него кроз своју крв уђе једном у светињу, и нађе вечни откуп. (aiōnios )
Iye sanalowemo ndi magazi ambuzi yayimuna, ana angʼombe amphongo, koma analowa Malo Opatulika kamodzi kokha ndi magazi ake, atatikonzera chipulumutso chosatha. (aiōnios )
А камоли неће крв Христа, који Духом Светим себе принесе без кривице Богу, очистити савест нашу од мртвих дела, да служимо Богу Живом и Истинитом? (aiōnios )
nʼkoposa kotani magazi a Khristu, amene mwa Mzimu wamuyaya anadzipereka yekha kwa Mulungu kukhala nsembe yopanda chilema. Iye adzayeretsa chikumbumtima chathu pochotsa ntchito za imfa, kuti ife titumikire Mulungu wamoyo. (aiōnios )
И зато је новом завету посредник, да кроз смрт, која би за откуп од преступака у првом завету, обећање вечног наследства приме звани. (aiōnios )
Pa chifukwa chimenechi Khristu ndi mʼkhalapakati wa pangano latsopano, kuti iwo amene anayitanidwa alandire chuma chamuyaya, pakuti Iye tsopano anafa ngati dipo lomasula iwo ku machimo amene anachita ali pansi pa pangano loyamba lija. (aiōnios )
Иначе би Он морао много пута страдати од постања света; а сад једном на свршетку века јави се да својом жртвом сатре грех. (aiōn )
Zikanatero bwenzi Khristu atamva zowawa kambirimbiri chilengedwere cha dziko lapansi. Koma tsopano anaoneka kamodzi kokha chifukwa cha onse pa nthawi yotsiriza kuti achotse tchimo podzipereka yekha nsembe. (aiōn )
Вером познајемо да је свет речју Божјом свршен, да је све што видимо из ништа постало. (aiōn )
Ndi chikhulupiriro timazindikira kuti dziko lapansi ndi la mmwamba zinapangidwa ndi Mawu a Mulungu, ndikuti zinthu zoonekazi zinachokera ku zinthu zosaoneka. (aiōn )
Исус Христос јуче је и данас онај исти и вавек. (aiōn )
Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi kunthawi zonse. (aiōn )
А Бог мира, који изведе из мртвих великог Пастира овцама, крвљу завета вечног, Господа нашег Исуса Христа, (aiōnios )
Mulungu wamtendere, amene kudzera mʼmagazi a pangano lamuyaya anaukitsa Ambuye athu Yesu kwa akufa, amene ndi Mʼbusa wamkulu, (aiōnios )
Да вас саврши у сваком делу добром, да учините вољу Његову, чинећи у вама шта је угодно пред Њиме, кроз Исуса Христа, коме слава ва век века. Амин. (aiōn )
akupatseni chilichonse chabwino kuti muchite chifuniro chake ndipo Mulungu achite mwa ife, chimene chingamukomere kudzera mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ku nthawi zanthawi, Ameni. (aiōn )
И језик је ватра, свет пут неправде. Тако и језик живи међу нашим удима, поганећи све тело, и палећи време живота нашег, и запаљујући се од пакла. (Geenna )
Lilime nalonso ndi moto, dziko la zoyipa pakati pa ziwalo za thupi. Limawononga munthu yense wathunthu. Limayika zonse za moyo wake pa moto, ndipo moto wake ndi wochokera ku gehena. (Geenna )
Као прерођени не од семена које труне, него од оног које не труне, речју Живог Бога, која остаје довека. (aiōn )
Popeza mwabadwanso, osati ndi mbewu imene imawonongeka, koma imene siwonongeka, ndiye kuti ndi Mawu a Mulungu amoyo ndi okhalitsa. (aiōn )
Али реч Господња осаје довека. А ово је реч што је објављена међу вама. (aiōn )
koma mawu a Ambuye adzakhala mpaka muyaya.” Ndipo awa ndi mawu amene tinalalikira kwa inu. (aiōn )
Ако ко говори, нека говори као речи Божије; ако ко служи нека служи као по моћи коју Бог даје: да се у свачему слави Бог кроз Исуса Христа, коме је слава и држава ва век века. Амин. (aiōn )
Ngati wina ayankhula, ayankhuledi mawu enieni a Mulungu. Ngati wina atumikira, atumikire ndi mphamvu imene Mulungu amapereka, kuti pa zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn )
А Бог сваке благодати, који вас позва на вечну своју славу у Христу Исусу, он да вас, пошто мало пострадате, саврши, да утврди, да укрепи, да утемељи. (aiōnios )
Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. (aiōnios )
Њему слава и држава ва век века. Амин. (aiōn )
Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn )
Јер вам се тако обилно допусти улазак у вечно царство Господа нашег и спаса Исуса Христа. (aiōnios )
Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. (aiōnios )
Јер кад Бог не поштеде анђела који сагрешише, него их метну у окове мрака пакленог, и предаде да се чувају за суд; (Tartaroō )
Pakuti Mulungu sanalekerere angelo atachimwa paja, koma anawaponya mʼndende, nawayika mʼmaenje amdima, kuwasunga kuti adzaweruzidwe. (Tartaroō )
Него напредујте у благодати и у познању Господа нашег и спаса Исуса Христа. Њему слава и сад и у вечна времена. Амин. (aiōn )
Koma kulani mu chisomo ndi mʼchidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
И живот се јави, и видесмо, и сведочимо, и јављамо вам живот вечни, који беше у Оца, и јави се нама; (aiōnios )
Moyowo unaoneka, tinawuona ndipo tikuchitira umboni. Tikukulalikirani za moyo wosatha umene unali ndi Atate ndipo unaonekera kwa ife. (aiōnios )
И свет пролази и жеља његова; а који твори вољу Божију остаје довека. (aiōn )
Dziko lapansi likupita pamodzi ndi zilakolako zake, koma amene amachita chifuniro cha Mulungu amakhalapo mpaka muyaya. (aiōn )
И ово је обећање које нам Он обећа, живот вечни. (aiōnios )
Ndipo chimene anatilonjeza nʼchimenechi: moyo wosatha. (aiōnios )
Сваки који мрзи на брата свог крвник је људски; и знате да ниједан крвник људски нема у себи вечни живот. (aiōnios )
Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha. (aiōnios )
И ово је сведочанство да нам је Бог дао живот вечни; и овај живот вечни у Сину је Његовом. (aiōnios )
Ndipo umboniwo ndi uwu: Mulungu anatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowu uli mwa Mwana wake. (aiōnios )
Ово писах вама који верујете у име Сина Божијег, да знате да имате живот вечни и да верујете у име Сина Божијег. (aiōnios )
Ine ndikulemba zimenezi kwa inu, amene mwakhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha. (aiōnios )
А знамо да Син Божји дође, и дао нам је разум да познамо Бога Истинитог, и да будемо у истинитом Сину Његовом Исусу Христу. Ово је Истинити Бог и Живот вечни. (aiōnios )
Tikudziwa kuti Mwana wa Mulungu anafika ndipo anatipatsa nzeru, kuti timudziwe Iye amene ali woona. Ndipo ife tili mwa Iye amene ndi woona, Mwana wake, Yesu Khristu. Iye ndi Mulungu woona ndi moyo wosatha. (aiōnios )
За истину која у нама стоји и биће с нама довека: (aiōn )
Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya. (aiōn )
И анђеле који не држаше своје старешинство него оставише свој стан чува у вечним оковима под мраком за суд великог дана. (aïdios )
Ndipo mukumbukire angelo amene sanakhutire ndi maudindo awo, koma anasiya malo awo. Angelo amenewa Mulungu anawamanga ndi maunyolo osatha, ndipo akuwasunga mʼmalo a mdima mpaka tsiku lalikulu lachiweruzo. (aïdios )
Као што Содом и Гомор, и околни њихови градови, који су се прокурвали онако као и они, и ходили за другим месом, поставише се углед и муче се у вечном огњу: (aiōnios )
Musayiwale mizinda ya Sodomu ndi Gomora ija, ndi mizinda yoyandikana nayo. Anthu mʼmenemo anadziperekanso kuchita zadama ndi kuchita zonyansa zachilendo. Mizinda imeneyi yakhala ngati chitsanzo cha amene adzalangidwa ndi moto wosatha. (aiōnios )
Бесни валови морски, који се пене својим срамотама, звезде лажне, којима се чува мрак вечне таме. (aiōn )
Iwowa ali ngati mafunde awukali apanyanja, amene amatulutsa thovu la zonyansa zawo. Amenewa ali ngati nyenyezi zosochera, ndipo Mulungu akuwasungira mdima wandiweyani mpaka muyaya. (aiōn )
И сами себе држите у љубави Божијој, чекајући милост Господа нашег Исуса Христа за живот вечни. (aiōnios )
Khalani mʼchikondi cha Mulungu pamene mukudikira chifundo cha Ambuye athu Yesu Khristu kuti akubweretsereni moyo wosatha. (aiōnios )
Једином премудром Богу и Спасу нашем, кроз Исуса Христа Господа нашег, слава и величанство, држава и власт пре свију векова и сад и у све векове. Амин. (aiōn )
kwa Mulungu yekhayo, Mpulumutsi wathu, kwa Iye kukhale ulemerero, ukulu, mphamvu ndi ulamuliro, mwa Yesu Khristu Ambuye athu, kuyambira isanayambe nthawi, tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
И учини нас цареве и свештенике Богу и Оцу свом; томе слава и држава ва век века. Амин. (aiōn )
ndipo watisandutsa mafumu ndi ansembe kuti tizitumikira Mulungu ndi Atate ake. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu ku nthawi zosatha, Ameni. (aiōn )
И Живи: и бејах мртав и ево сам жив ва век века, амин. И имам кључеве од пакла и од смрти. (aiōn , Hadēs )
Ine ndine Wamoyo; ndinali wakufa ndipo taona ndine wamoyo mpaka muyaya! Ndipo ndili ndi makiyi a imfa ndi Hade. (aiōn , Hadēs )
И кад даше животиње славу и част и хвалу Ономе што сеђаше на престолу, што живи ва век века, (aiōn )
Nthawi zonse zamoyozo zimapereka ulemerero, ulemu ndi mayamiko kwa uja wokhala pa mpando waufumu, amene ali ndi moyo wamuyaya. (aiōn )
Падоше двадесет и четири старешине пред Оним што сеђаше на престолу, и поклонише се Ономе што живи ва век века, и метнуше круне своје пред престолом говорећи: (aiōn )
Izi zikamachitika akuluakulu 24 aja amadzigwetsa pansi pamaso pa wokhala pa mpando waufumuyo, namupembedza wokhala ndi moyo wamuyayayo. Iwo amaponya pansi zipewa zawo zaufumu patsogolo pa mpando waufumu nati: (aiōn )
И свако створење, што је на небу, и на земљи, и под земљом, и што је на мору, и што је у њима, све чух где говоре: Ономе што седи на престолу, и Јагњету благослов и част и слава и држава ва век века. (aiōn )
Kenaka ndinamva mawu a cholengedwa chilichonse kumwamba, pa dziko lapansi, kunsi kwa dziko lapansi, pa nyanja ndi zonse zili mʼmenemo zikuyimba kuti, “Kwa wokhala pa mpando waufumu ndi kwa Mwana Wankhosa, kukhale mayamiko, ulemu, ulemerero ndi mphamvu (aiōn )
И видех, и гле, коњ блед, и ономе што сеђаше на њему беше име смрт, и пакао иђаше за њим; и њему се даде област на четвртом делу земље да убије мачем и глађу и смрћу и зверињем земаљским. (Hadēs )
Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wotuwa! Wokwerapo wake dzina lake linali Imfa ndipo Hade inali kumutsatira pambuyo pake. Anapatsidwa ulamuliro pa gawo limodzi la magawo anayi a dziko lapansi kuti aphe ndi lupanga, njala, mliri, ndi zirombo zakuthengo za mʼdziko lapansi. (Hadēs )
Говорећи: Амин; благослов и слава и премудрост и хвала и част и сила и јачина Богу нашем ва век века. Амин. (aiōn )
Iwo anati, “Ameni! Matamando ndi ulemerero, nzeru, mayamiko, ulemu, ulamuliro ndi mphamvu zikhale kwa Mulungu wathu kunthawi zanthawi, Ameni!” (aiōn )
И пети анђео затруби, и видех звезду где паде с неба на земљу, и даде јој се кључ од студенца бездана; (Abyssos )
Mngelo wachisanu anayimba lipenga lake, ndipo ndinaona nyenyezi ikugwa pa dziko lapansi kuchokera ku thambo. Nyenyeziyo inapatsidwa kiyi ya ku chidzenje chakuya. (Abyssos )
И отвори студенац бездана, и изиђе дим из студенца као дим велике пећи, и поцрне сунце и небо од дима студенчевог. (Abyssos )
Nyenyeziyo itatsekula pa chidzenje chakuyacho panatuluka utsi ngati wochokera mʼngʼanjo yayikulu. Dzuwa ndi thambo zinada chifukwa cha utsi ochokera mʼdzenjemo. (Abyssos )
И имаху над собом цара анђела бездана коме је име јеврејски Авадон, а грчки Аполион. (Abyssos )
Mfumu yawo inali mngelo wolamulira Chidzenje chakuya chija. Mʼchihebri dzina lake ndi Abadoni ndipo mʼChigriki ndi Apoliyoni (tanthauzo lake ndiye kuti, Wowononga). (Abyssos )
И закле се Оним који живи ва век века, који сазда небо и шта је на њему, и земљу и шта је на њој, и море и шта је у њему, да времена већ неће бити; (aiōn )
Mngeloyo analumbira mʼdzina la Iye wokhala ndi moyo mpaka muyaya, amene analenga kumwamba ndi zonse zili kumeneko, dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo, nati, “Pasakhalenso zochedwa tsopano! (aiōn )
И кад сврше сведочанство своје, онда ће звер што излази из бездана учинити с њима рат, и победиће их и убиће их. (Abyssos )
Tsono zikadzatsiriza umboni wawowo, chirombo chotuluka mʼChidzenje chakuya chija chidzachita nawo nkhondo nʼkuzigonjetsa mpaka kuzipha. (Abyssos )
И седми анђео затруби и посташе велики гласови на небесима говорећи: Поста царство света Господа нашег и Христа Његовог, и цароваће ва век века. (aiōn )
Mngelo wachisanu ndi chiwiri anawomba lipenga lake, ndipo kumwamba kunamveka mawu ofuwula amene anati, “Ufumu wa dziko lapansi uli mʼmanja mwa Ambuye athu ndi Khristu wake uja, ndipo adzalamulira mpaka muyaya.” (aiōn )
И видех другог анђела где лети посред неба, који имаше вечно јеванђеље да објави онима који живе на земљи, и сваком племену, и језику и колену и народу. (aiōnios )
Kenaka ndinaona mngelo wina akuwuluka mu mlengalenga ndipo anali ndi Uthenga Wabwino wamuyaya woti akalalikire kwa anthu okhala pa dziko lapansi, kwa a mtundu uliwonse, a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse ndi kwa anthu onse. (aiōnios )
И дим мучења њиховог излазиће ва век века; и неће имати мира дан и ноћ који се поклањају звери и икони њеној, и који примају жиг имена њеног. (aiōn )
Ndipo utsi wa moto wowazunzawo udzakwera kumwamba mpaka muyaya. Sikudzakhala kupumula usana ndi usiku kwa amene anapembedza chirombo chija ndi fano lake kapena kwa aliyense amene analembedwa chizindikiro cha dzina lake lija.” (aiōn )
И једна од четири животиње даде седморици анђела седам чаша златних напуњених гнева Бога, који живи ва век века. (aiōn )
Ndipo kenaka chimodzi cha zamoyo zinayi zija chinapereka kwa angelo asanu ndi awiri mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi ukali wa Mulungu amene ali ndi moyo mpaka muyaya. (aiōn )
Звер коју си видео беше и није, и изићи ће из бездана и отићи ће у пропаст; и удивиће се који живе на земљи, којима имена написана нису у књигу живота од постања света, кад виде звер која беше, и није, и доћи ће опет. (Abyssos )
Chirombo chimene wachionachi chinalipo kale koma tsopano kulibe ndipo chidzatuluka ku chidzenje chakuya ndi kupita kukawonongedwa. Anthu okhala pa dziko lapansi amene mayina awo sanalembedwe mʼbuku lamoyo kuyambira pa kulengedwa kwa dziko lapansi adzadabwa pamene adzaona chirombocho, chifukwa chinalipo kale, tsopano kulibe, komabe chidzabwera. (Abyssos )
И другом рекоше: Алилуја! И дим њен излажаше ва век века. (aiōn )
Ndipo anafuwulanso kuti, “Haleluya! Utsi wochokera kwa mkazi wadamayo udzakwera kumwamba mpaka muyaya.” (aiōn )
И би ухваћена звер, и с њом лажни пророк који учини пред њом знаке којима превари оне који примише жиг зверин и који се поклањају икони њеној: живи бише бачени обоје у језеро огњено, које гори сумпором. (Limnē Pyr )
Koma chirombocho chinagwidwa pamodzi ndi mneneri wonyenga uja amene anachita zizindikiro zodabwitsa pamaso pake. Ndi zizindikirozi anasocheretsa amene analembedwa chizindikiro cha chirombocho napembedza fano lake. Onse awiri anaponyedwa amoyo mʼnyanja yamoto yasulufule wotentha. (Limnē Pyr )
И видех анђела где силази с неба, који имаше кључ од бездана и вериге велике у руци својој. (Abyssos )
Ndipo ndinaona mngelo akutsika kuchokera kumwamba ali ndi kiyi ya ku chidzenje chakuya chija atanyamula mʼdzanja lake unyolo waukulu. (Abyssos )
И у бездан баци је, и затвори је, и запечати над њом, да више не прелашћује народе, док се не наврши хиљаду година; и потом ваља да буде одрешена на мало времена. (Abyssos )
Anamuponya ku chidzenje chakuya chija namutsekera ndi kiyi ndi kumatirira pa khomopo kuti asatulukenso kukanyenga mitundu ya anthu mpaka patapita zaka 1,000. Zikadzatha zakazo, adzamumasula kwa kanthawi pangʼono chabe. (Abyssos )
И ђаво који их вараше би бачен у језеро огњено и сумпорито, где је звер и лажни пророк; и биће мучени дан и ноћ ва век века. (aiōn , Limnē Pyr )
Ndipo Mdierekezi amene anawanyenga, anaponyedwa mʼnyanja ya sulufule wotentha, kumene kunaponyedwa chirombo chija ndi mneneri wonama uja. Iwo adzazunzika usiku ndi usana kwamuyaya. (aiōn , Limnē Pyr )
И море даде своје мртваце, и смрт и пакао дадоше своје мртваце; и суд примише по делима својим. (Hadēs )
Nyanja inapereka amene anaferamo ndipo imfa ndi Hade zinapereka akufa ake ndipo munthu aliyense anaweruzidwa monga mwa ntchito zake. (Hadēs )
И смрт и пакао бачени бише у језеро огњено. И ово је друга смрт. (Hadēs , Limnē Pyr )
Kenaka imfa ndi Hade zinaponyedwa mʼnyanja ya moto. Nyanja yamoto ndiyo imfa yachiwiri. (Hadēs , Limnē Pyr )
И ко се не нађе написан у књизи живота, бачен би у језеро огњено. (Limnē Pyr )
Ngati dzina la wina aliyense silinapezeke mʼBuku Lamoyo, anaponyedwa mʼnyanja yamoto. (Limnē Pyr )
А страшљивима и невернима и поганима и крвницима, и курварима, и врачарима, и идолопоклоницима, и свима лажама, њима је део у језеру што гори огњем и сумпором; које је смрт друга. (Limnē Pyr )
Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.” (Limnē Pyr )
И ноћи тамо неће бити, и неће потребовати видела од жишка, ни видела сунчаног, јер ће их обасјавати Господ Бог, и цароваће ва век века. (aiōn )
Sipadzakhalanso usiku. Sadzafuna kuwala kwa nyale kapena kwa dzuwa pakuti Ambuye Mulungu adzakhala kuwala kwawo. Ndipo adzalamulira kwamuyaya. (aiōn )
Ово су безводни извори, и облаци и магле које прогоне ветрови, за које се чува мрак тамни вавек. ()