< 3 Мојсијева 20 >

1 И рече Господ Мојсију говорећи:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Још реци синовима Израиљевим: Ко год између синова Израиљевих или између дошљака који се баве у Израиљу, да од семена свог Молоху, нека се погуби, народ у земљи нека га заспе камењем.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala.
3 И ја ћу окренути лице своје насупрот таквом човеку, и истребићу га из народа његовог, што од семена свог даде Молоху, и запрзни светињу моју и оскврни свето име моје.
Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera.
4 Ако ли народ како год затвори очи да не види тог човека кад да од семена свог Молоху, и не убију га,
Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha,
5 Ја ћу окренути лице своје насупрот оном човеку и насупрот дому његовом, и истребићу га, и све који за њим чине прељубу чинећи прељубу за Молохом, из народа њиховог.
Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”
6 А ко се обрати к врачарима и к гатарима да чини прељубу за њима, окренућу лице своје на супрот њему, и истребићу га из народа његовог.
“‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.
7 Зато посвећујте се, и будите свети, јер сам ја Господ Бог ваш.
“‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
8 И чувајте уредбе моје и вршите их. Ја сам Господ који вас посвећујем.
Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.
9 Ко опсује оца свог или матер своју, да се погуби; опсовао је оца свог или матер своју; крв његова на њ.
“‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.
10 А човек који учини прељубу с туђом женом, што је учинио прељубу са женом ближњег свог, да се погуби и прељубочинац и прељубочиница.
“‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.
11 Ко би спавао са женом оца свог, открио је голотињу оца свог; обоје да се погубе; крв њихова на њих.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.
12 Ко би спавао са женом сина свог, обоје да се погубе; учинише срамоту; крв њихова на њих.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
13 Ко би мушкарца облежао као жену, учинише гадну ствар обојица; да се погубе; крв њихова на њих.
“‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
14 И ко би узео жену и матер њену, зло је, огњем да се спали и он и она, да не буде зла међу вама.
“‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.
15 Ко би облежао живинче, да се погуби; убијте и живинче.
“‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.
16 И ако би жена легла под живинче, убиј и жену и живинче, нека погину, крв њихова на њих.
“‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
17 Ко би узео сестру своју, кћер оца свог или кћер матере своје, видео би голотињу њену и она би видела голотињу његову, срамота је; зато да се истребе испред синова народа свог; открио је голотињу сестре своје, нека носи безакоње своје.
“‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.
18 И ко би спавао са женом кад има време и открио голотињу њену откривши течење њено, и она би открила течење крви своје, да се истребе обоје из народа свог.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.
19 Голотиње сестре матере своје и сестре оца свог не откриј, јер би открио своју крв; нека носе безакоње своје.
“‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.
20 А ко би спавао са женом стрица свог, открио би голотињу стрица свог, нека носе обоје грех свој, нека помру без деце.
“‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.
21 Ко би узео жену брата свог, ружно је, открио је голотињу брата свог; без деце да буду.
“‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.
22 Чувајте све уредбе моје и све законе моје, и вршите их, да вас земља не изметне, у коју вас водим да живите у њој.
“‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni.
23 Немојте живети по уредбама народа које ћу отерати испред вас, јер су чинили све то, зато ми омрзоше.
Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo.
24 И рекох вам: Ви ћете наследити земљу њихову и ја ћу вам је дати у државу, земљу у којој тече млеко и мед. Ја сам Господ Бог ваш који вас одвојих од других народа.
Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.
25 Зато разликујте стоку чисту од нечисте, и птицу чисту од нечисте, и немојте скврнити душа својих стоком или птицом или чим год што пуже по земљи, што сам вам одвојио да је нечисто.
“‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu.
26 И бићете ми свети, јер сам свет ја, Господ, и одвојих вас од других народа да будете моји.
Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.
27 А човек или жена, у којима би био дух врачарски или гатарски, да се погубе, камењем да се заспу, крв њихова на њих.
“‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’”

< 3 Мојсијева 20 >