< Књига Исуса Навина 17 >

1 И допаде део племену Манасијином, а он беше првенац Јосифов; Махиру првенцу Манасијином оцу Галадовом, јер беше човек јунак, зато му допаде Галад и Васан;
Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
2 Добише део и остали синови Манасијини по породицама својим, синови Авијезерови, и синови Хелекови, и синови Азрилови, и синови Сихемови, и синови Еферови, и синови Семидини. То су синови Манасије сина Јосифовог; људи по породицама својим.
Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
3 А Салпад син Ефера сина Галада сина Махира сина Манасијиног није имао синова него кћери; и ово су имена кћерима његовим: Мала и Нуја, Егла, Мелха и Терса.
Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
4 И оне дођоше пред Елеазара свештеника и пред Исуса сина Навиног и пред кнезове, и рекоше: Господ је заповедио Мојсију да нам се да наследство међу браћом нашом. И даде им Исус, по заповести Господњој, наследство међу браћом оца њиховог.
Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
5 И допаде Манасији десет делова, осим земље галадске и васанске, које су с оне стране Јордана.
Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
6 Јер кћери Манасијине добише наследство међу синовима његовим, а земља галадска допаде другим синовима Манасијиним.
chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
7 А међа Манасијина беше од Асира к Михмети, која је према Сихему, потом иде та међа надесно к становницима ен-тафујским.
Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
8 А Манасијина је земља тафујска, али Тафуја на међи Манасијиној припада синовима Јефремовим.
(Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
9 Одатле силази међа на поток Кану, с јужне стране тог потока; и градови су Јефремови међу градовима Манасијиним; а међа је Манасијина са северне стране потока и излази на море.
Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
10 С југа је Јефремово, а са севера Манасијино, а море им је међа; а с Асиром граниче на северу а с Исахаром на истоку.
Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
11 Јер је Манасијино у племену Исахаровом и Асировом: Вет-Сан са селима својим, и Ивлеам са селима својим, и Дорани са селима својим, и Ен-Дорани са селима својим, и Танашани са селима својим, и Мегиђани са селима својим; та три краја.
Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
12 Али синови Манасијини не могоше изагнати Хананеје из тих градова, него Хананеји стадоше живети у тој земљи.
Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
13 Али кад ојачаше синови Израиљеви, ударише данак на Хананеје, али их не изагнаше.
Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
14 А синови Јосифови рекоше Исусу говорећи: Зашто си нам дао у наследство један део и једно уже, кад је нас множина и Господ нас је благословио довде?
Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
15 А Исус им рече: Кад вас је множина, идите у шуму, и онде окрчите себи, у земљи ферезејској и рафајској, ако вам је тесна гора Јефремова.
Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
16 А синови Јосифови рекоше: Неће нам бити доста ова гора; а сви Хананеји који живе у долини имају гвоздена кола; и они који су у Вет-Сану и у селима његовим и они који су у долини језраелској.
Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
17 А Исус рече дому Јосифовом, Јефрему и Манасији, говорећи: Велик си народ и силан си, нећеш имати једног дела.
Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
18 Него гора нека буде твоја; ако је шума, исеци је, па ћеш имати међе њене; јер ћеш изагнати Хананеје, ако и имају гвоздена кола, ако и јесу јаки.
dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”

< Књига Исуса Навина 17 >