< Књига пророка Јеремије 10 >

1 Слушајте реч коју вам говори Господ, доме Израиљев.
Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena.
2 Овако вели Господ: Не учите се путу којим иду народи, и од знака небеских не плашите се, јер се од њих плаше народи.
Yehova akuti, “Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu ina kapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga, ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha.
3 Јер су уредбе у народа таштина, јер секу дрво у шуми, дело руку уметничких секиром;
Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe. Iwo amakadula mtengo ku nkhalango ndipo mmisiri amawusema ndi sompho.
4 Сребром и златом украшују га, клинима и чекићима утврђују га да се не помиче;
Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide; kenaka amachikhomerera ndi misomali kuti chisagwedezeke.
5 Стоје право као палме, не говоре; треба их носити, јер не могу ићи; не бој их се, јер не могу зла учинити, а не могу ни добра учинити.
Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka. Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwe ndipo ayenera kunyamulidwa popeza sangathe nʼkuyenda komwe. Musachite nawo mantha popeza sangathe kukuchitani choyipa ndiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.”
6 Нико није као Ти, Господе; велик си и велико је име Твоје у сили.
Palibe wofanana nanu, Inu Yehova; Inu ndinu wamkulu, ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu.
7 Ко се не би Тебе бојао, царе над народима! Јер Теби то припада; јер међу свим мудрацима у народа и у свим царствима њиховим нема таквог какав си Ти.
Ndani amene angaleke kukuopani, inu Mfumu ya mitundu ya anthu? Chimenechi ndicho chokuyenerani. Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onse a mitundu ya anthu, palibe wina wofanana nanu.
8 Него су сви луди и безумни, дрво је наука о таштини.
Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru; malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
9 Сребро ковано доноси се из Тарсиса и злато из Уфаза, дело уметничко и руку златарских, одело им је од порфире и скерлета, све је дело уметничко.
Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisi ndipo golide amachokera naye ku Ufazi. Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide. Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo. Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso.
10 А Господ је прави Бог, Бог живи и цар вечни, од Његове срдње тресе се земља, и гнев Његов не могу поднети народи.
Koma Yehova ndiye Mulungu woona; Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya. Akakwiya, dziko limagwedezeka; anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
11 Овако им реците: Богови, који нису начинили небо ни земљу, нестаће са земље и испод неба.
“Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’”
12 Он је начинио земљу силом својом, утврдио васиљену мудрошћу својом, и разумом својим разастро небеса;
Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
13 Он кад пусти глас свој, буче воде на небесима, подиже пару с крајева земаљских, пушта муње с даждем, и изводи ветар из стаја његових.
Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba; Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako.
14 Сваки човек поста безуман од знања, сваки се златар осрамоти ликом резаним, јер су лаж ливени ликови његови, и нема духа у њима.
Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
15 Таштина су, дело преварно; кад их походим, погинуће.
Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa.
16 Није такав део Јаковљев, јер је Творац свему, и Израиљ Му је наследство, име Му је Господ над војскама.
Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse kuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
17 Покупи из земље трг свој ти, која седиш у граду.
Sonkhanitsani katundu wanu, inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo.
18 Јер овако вели Господ: Гле, ја ћу избацити као праћом становнике ове земље, и притеснићу их да осете.
Pakuti Yehova akuti, “Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse amene akukhala mʼdziko lino; adzakhala pa mavuto mpaka adzamvetsa.”
19 Тешко мени од муке моје, рећи ће; љута је рана моја; а ја рекох: То је бол, треба да га подносим.
Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga! Chilonda changa nʼchachikulu!” Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi, choncho ndingolipirira.”
20 Мој је шатор опустошен и сва ужа моја покидана, синови моји отидоше од мене и нема их, нема више никога да разапне шатор мој и дигне завесе моје.
Tenti yanga yawonongeka, zingwe zake zonse zaduka. Ana anga andisiya ndipo kulibenso. Palibenso amene adzandimangire tenti, kapena kufunyulula nsalu yake.
21 Јер пастири посташе безумни и Господа не тражише; зато не бише срећни, и све се стадо њихово распрша.
Abusa ndi opusa ndipo sanapemphe nzeru kwa Yehova; choncho palibe chimene anapindula ndipo nkhosa zawo zonse zabalalika.
22 Гле, иде глас и врева велика из северне земље да обрати градове Јудине у пустош, у стан змајевски.
Tamvani! kukubwera mphekesera, phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto! Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda, malo okhala nkhandwe.
23 Знам, Господе, да пут човечји није у његовој власти нити је човеку који ходи у власти да управља корацима својим.
Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake; munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake.
24 Карај ме, Господе, али с мером, не у гневу свом, да ме не би затро.
Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo, osati ndi mkwiyo wanu, mungandiwononge kotheratu.
25 Излиј гнев свој на народе који Те не познају, и на племена која не призивају име Твоје, јер прождреше Јакова, прождреше га да га нема, и насеље његово опустеше.
Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani, ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba. Iwo aja anasakaza Yakobo; amusakaza kotheratu ndipo awononga dziko lake.

< Књига пророка Јеремије 10 >