< Књига пророка Исаије 25 >

1 Господе, Ти си Бог мој, узвишаваћу Те, славићу име Твоје, јер си учинио чудеса; намере Твоје од старине вера су и истина.
Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
2 Јер си од града начинио гомилу, и од тврдог града зидине; од града двор за странце, довека се неће саградити.
Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
3 Зато ће Те славити народ силан, град страшних народа бојаће Те се.
Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
4 Јер си био крепост убогом, крепост сиромаху у невољи његовој, уточиште од поплаве, заклон од жеге, јер је гнев насилнички као поплава која обаљује зид.
Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
5 Вреву иностранаца прекинуо си као припеку на сувом месту; као припека сеном од облака, тако се певање насилника прекиде.
ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
6 И Господ ће над војскама учинити свим народима на овој гори гозбу од претила меса, гозбу од чистог вина, од претилог меса с можданима, од вина без талога.
Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
7 И поквариће на овој гори застирач којим су застрти сви народи, и покривач којим су покривени сви народи.
Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
8 Уништиће смрт заувек, и утрће Господ Господ сузе са сваког лица, и срамоту народа свог укинуће са све земље; јер Господ рече.
Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
9 И рећи ће се у оно време: Гле, ово је Бог наш, Њега чекасмо, и спашће нас; ово је Господ, Њега чекасмо; радоваћемо се и веселићемо се за спасење Његово.
Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
10 Јер ће рука Господња починути на овој гори, а Моав ће се изгазити на свом месту као што се гази слама за гној.
Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
11 И размахнуће рукама својим сред њега, као што размахује пливач да плива, и обориће охолост његову мишицама руку својих.
Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
12 И град и високе зидове твоје снизиће, обориће, бациће на земљу у прах.
Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.

< Књига пророка Исаије 25 >