< Књига пророка Осије 2 >

1 Реците браћи својој: Народе мој; и сестрама својим: Помилована.
“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
2 Прите се с матером својом, прите се, јер ми није жена, нити сам јој ја муж; нека одбаци курварства своја од лица свог, и прељубе своје од дојака својих,
“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
3 Да је не бих свукао голу и учинио је каква је била онај дан кад се родила, и да је не бих поставио да буде као пустиња и обратио је да буде као земља сасушена, и уморио је жеђу.
Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
4 И нећу се смиловати на децу њену, јер су копилад.
Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
5 Јер се мати њихова курва, срамоти се родитељка њихова; јер говори: Ићи ћу за милосницима својим који ми дају хлеб мој и воду моју, вуну моју и лан мој, уље моје и пиће моје.
Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
6 Зато ево ја ћу јој заградити пут трњем и зазидаћу зидом да не нађе стаза својих.
Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
7 И трчаће за својим милосницима, али их неће стигнути; и тражиће их, али их неће наћи; па ће рећи: Идем да се вратим к првом мужу свом, јер ми беше боље онда него сада.
Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
8 Јер она не зна да сам јој ја давао жито и вино и уље, и умножавао јој сребро и злато, од ког начинише Вала.
Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
9 Зато ћу узети натраг жито своје, кад буде време, и вино своје, кад буде време, и узећу вуну своју и лан свој, којим би покривала голотињу своју.
“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
10 И открићу ругобу њену пред милосницима њеним, и нико је неће избавити из моје руке.
Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
11 И укинућу сваку радост њену, светковине њене, младине њене и суботе њене и све празнике њене.
Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
12 И потрћу чокоте њене и смокве, за које говори: Плата су ми, што ми дадоше милосници моји; и обратићу их у шуму да их једе зверје пољско.
Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
13 И походићу на њој дане валимске, у које им је кадила и китила се обоцима и гривнама, и ишла за својим милосницима, и мене заборавила, говори Господ.
Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
14 Али ево, ја ћу је примамити и одвешћу је у пустињу, и говорићу с њом лепо.
“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 И даћу јој винограде њене од тог места, и долину Ахор за врата надању, и онде ће певати као за младости своје и као кад је ишла из Мисира.
Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
16 И тада ћеш ме, говори Господ, звати: Мужу мој; а нећеш ме више звати: Вале мој.
“Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 Јер ћу уклонити из уста њених имена Валова; и неће им се више помињати имена.
Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 И тада ћу им учинити завет са зверјем пољским и са птицама небеским и с бубинама земаљским; и поломићу лук и мач и рат да их нестане у земљи, и учинићу да леже без страха.
Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
19 И заручићу те себи довека, заручићу те себи правдом и судом и милошћу и милосрђем.
Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
20 И заручићу те себи вером, и познаћеш Господа.
Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
21 И тада ћу се одазвати, говори Господ, одазваћу се небесима, а она ће се одазвати земљи.
“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 А земља ће се одазвати житу и вину и уљу, а то ће се одазвати Језраелу.
ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 И посејаћу је себи на земљи, и смиловаћу се на Лорухаму, и рећи ћу Лоамији: Ти си мој народ, и он ће рећи: Боже мој!
Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”

< Књига пророка Осије 2 >