< 5 Мојсијева 19 >

1 Кад Господ Бог твој потре народе којих земљу даје теби Господ Бог твој, и кад их наследиш и настаниш се по градовима њиховим и по кућама њиховим,
Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo,
2 Одвој три града усред земље своје коју ти даје Господ Бог твој да је наследиш,
mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu.
3 Начини пут, и раздели на троје крајеве земље своје коју ти да Господ Бог твој у наследство, па нека бежи онамо сваки крвник.
Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.
4 А овако нека буде с крвником који утече онамо, да би остао жив: ко убије ближњег свог нехотице, не мрзевши пре на њ,
Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa.
5 Као кад би ко отишао с ближњим својим у шуму да сече дрва, па би замахнуо секиром у руци својој да посече дрво, а она би спала с држалице и погодила би ближњег његова тако да умре он нека утече у који од тих градова да остане жив,
Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake.
6 Да не би осветник потерао крвника док му је срце распаљено и да га не би стигао на далеком путу и убио га, премда није заслужио смрт, јер није пре мрзео на њ.
Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala.
7 Зато ти заповедам и велим: три града одвој.
Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.
8 А кад рашири Господ Бог твој међе твоје као што се заклео оцима твојим, и да ти сву земљу коју је рекао дати оцима твојим,
Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera,
9 Ако уздржиш и уствориш све ове заповести, које ти ја данас заповедам, да љубиш Господа Бога свог и ходиш путевима Његовим свагда, онда додај још три града осим она три,
chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera.
10 Да се не пролива крв права у земљи твојој, коју ти Господ Бог твој даје у наследство, и да не буде на теби крв.
Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.
11 Али ако ко мрзи на ближњег свог и вреба га, и скочи на њ, и удари га тако да умре, а он утече у који од тих градова,
Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi,
12 Онда старешине места његова нека пошаљу и узму га оданде, и предаду га у руке осветнику да се погуби.
akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe.
13 Нека га не жали око твоје него скини крв праву с Израиља, да би ти добро било.
Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.
14 Не помичи међе ближњег свог коју поставе стари у наследству твом које добијеш у земљи коју ти Господ Бог твој даје да је наследиш.
Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
15 Нека не устаје један сведок на човека ни за како зло и ни за какав грех између свих греха који се чине, него на речима два или три сведока да остаје ствар.
Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.
16 Ако би устао лажан сведок на кога да сведочи на њега да се одмеће Бога,
Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu,
17 Онда нека стану та два човека, који имају ту распру, пред Господа, пред свештенике и пред судије које буду у то време;
anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo.
18 И нека добро испитају судије, ако сведок онај буде лажан сведок и лажно сведочи на брата свог,
Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake,
19 Учините му онако како је он мислио учинити брату свом и извади зло из себе,
ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
20 Да се остали чувши то боје, и унапред више не чине тако зло усред тебе.
Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu.
21 Нека не жали око твоје: живот за живот, око за око, зуб за зуб, руку за руку, ногу за ногу.
Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.

< 5 Мојсијева 19 >