< 2 Књига Самуилова 8 >

1 После тога разби Давид Филистеје, и покори их, и узе Давид Метег-Аму из руку филистејских.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 Разби и Моавце, и измери их ужем поваљавши их по земљи, и измери их два ужа да се погубе а једно уже да се оставе у животу. И Моавци посташе слуге Давидове, и плаћаху му данак.
Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
3 Давид разби и Адад-Езера сина Реововог цара совског, изашав да рашири власт своју до реке Ефрата.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 И зароби их Давид хиљаду и седам стотина коњаника и двадесет хиљада пешака, и подреза Давид жиле свим коњима колским, само остави за сто кола.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 И беху дошли Сирци из Дамаска у помоћ Адад-Езеру цару совском, и Давид поби двадесет и две хиљаде Сираца.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 И намести Давид војску у Сирији што је под Дамаском, и Сирци посташе слуге Давидове плаћајући му данак. И Господ чуваше Давида куда год иђаше.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 И Давид узе златне штитове које имаху слуге Адад-Езерове, и донесе их у Јерусалим.
Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 И из Ветаха и из Виротаја, градова Адад-Езерових, однесе цар Давид силну бронзу.
Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
9 А кад чу Тоја, цар ематски, да је Давид побио сву војску Адад-Езерову,
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
10 Посла Тоја Јорама сина свог к цару Давиду да га поздрави и да му честита што је војевао на Адад-Езера и убио га, јер Тоја имаше рат с Адад-Езером; и донесе Јорам закладе златне и сребрне и бронзане.
anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
11 Па и то цар Давид посвети Господу са сребром и златом што беше посветио од свих народа које покори,
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
12 Од Сираца и од Моаваца и од синова Амонових и од Филистеја и од Амалика, и од плена Адад-Езера сина Реововог, цара совског.
Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
13 И Давид стече име кад се врати побивши Сирце, осамнаест хиљада у сланој долини.
Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
14 И намести војску по Идумеји, по свој Идумеји намести војску, и сви Едомци посташе слуге Давидове. И Господ чуваше Давида куда год иђаше.
Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
15 Тако царова Давид над свим Израиљем, судећи и дајући правду свему народу свом.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
16 И Јоав син Серујин беше над војском; а Јосафат син Ахилудов паметар;
Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
17 А Садок син Ихитовов и Ахимелех син Авијатаров свештеници; а Сераја писар;
Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
18 А Венаја син Јодајев беше над Херетејима и Фелетејима; а синови Давидови кнезови.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.

< 2 Књига Самуилова 8 >