< 1 Солуњанима 1 >

1 Од Павла и Силвана и Тимотија, цркви солунској у Богу Оцу и Господу Исусу Христу: благодат вам и мир од Бога Оца нашег и Господа Исуса Христа.
Paulo, Silivano ndi Timoteyo. Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu.
2 Захваљујемо Богу свагда за све вас спомињући вас у молитвама својим,
Ife timayamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu. Timakutchulani mʼmapemphero athu.
3 И спомињући без престанка ваше дело вере, и труд љубави, и трпљење наде Господа нашег Исуса Христа, пред Богом и Оцем нашим,
Nthawi zonse timakumbukira ntchito yanu yachikhulupiriro, yachikondi ndi kupirira kwanu kwa chiyembekezo mwa Ambuye athu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu wathu ndi Atate.
4 Знајући, браћо љубазна, од Бога избор ваш.
Abale okondedwa ndi Mulungu, tikudziwa kuti Mulungu anakusankhani,
5 Јер јеванђеље наше не би к вама само у речи него и у сили и у Духу Светом, и у великом признању, као што знате какви бисмо међу вама вас ради.
chifukwa uthenga wathu wabwino sunafike kwa inu ndi mawu okha, koma ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndi chitsimikizo chachikulu. Mukudziwa mmene tinkakhalira pakati panu kuti tikuthandizeni.
6 И ви се угледасте на нас и на Господа примивши реч у великој невољи с радошћу Духа Светог,
Inu mwakhala otitsatira athu ndi a Ambuye; ngakhale kuti panali masautso akulu, munalandira uthenga mwachimwemwe chochokera kwa Mzimu Woyera.
7 Тако да постадосте углед свима који верују у Македонији и у Ахаји.
Ndipo potero munakhala chitsanzo kwa abale onse a ku Makedoniya ndi Akaya.
8 Јер се од вас прочу реч Господња не само у Македонији и Ахаји, него и у свако место изиђе вера ваша у Бога тако да нам није потребно шта говорити.
Kuchokera kwa inu, uthenga wa Ambuye unamveka ku Makedoniya ndi ku Akaya ndipo mbiri ya chikhulupiriro chanu mwa Mulungu yamveka ponseponse. Choncho sikofunikanso kuti tinene kanthu,
9 Јер они обзнањују за вас какав улазак имасмо к вама, и како се обратисте Богу од идола, да служите Богу Живом и Истинитом,
pakuti iwo amafotokoza za momwe munatilandirira. Iwo amatiwuza za momwe munatembenukira kwa Mulungu kusiya mafano ndi kutumikira Mulungu wamoyo ndi woona.
10 И да чекате Сина Његовог с небеса ког васкрсе из мртвих, Исуса, који нас избавља од гнева који ће доћи.
Ndipo mukudikira Mwana wake kuchokera kumwamba, Yesu, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ukubwera.

< 1 Солуњанима 1 >