< К Римлянам 12 >

1 Итак умоляю вас, братия, милосердием Божиим, представьте тела ваши в жертву живую, святую, благоугодную Богу, для разумного служения вашего,
Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu.
2 и не сообразуйтесь с веком сим, но преобразуйтесь обновлением ума вашего, чтобы вам познавать, что есть воля Божия, благая, угодная и совершенная. (aiōn g165)
Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro. (aiōn g165)
3 По данной мне благодати, всякому из вас говорю: не думайте о себе более, нежели должно думать; но думайте скромно, по мере веры, какую каждому Бог уделил.
Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani.
4 Ибо как в одном теле у нас много членов, но не у всех членов одно и то же дело,
Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana.
5 так мы, многие, составляем одно тело во Христе, а порознь один для другого члены.
Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake.
6 И как, по данной нам благодати, имеем различные дарования, то имеешь ли пророчество, пророчествуй по мере веры;
Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake.
7 имеешь ли служение, пребывай в служении; учитель ли, - в учении;
Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse.
8 увещатель ли, увещевай; раздаватель ли, раздавай в простоте; начальник ли, начальствуй с усердием; благотворитель ли, благотвори с радушием.
Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.
9 Любовь да будет непритворна; отвращайтесь зла, прилепляйтесь к добру;
Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino.
10 будьте братолюбивы друг к другу с нежностью; в почтительности друг друга предупреждайте;
Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni.
11 в усердии не ослабевайте; духом пламенейте; Господу служите;
Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye.
12 утешайтесь надеждою; в скорби будьте терпеливы, в молитве постоянны;
Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero.
13 в нуждах святых принимайте участие; ревнуйте о странноприимстве.
Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.
14 Благословляйте гонителей ваших; благословляйте, а не проклинайте.
Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere.
15 Радуйтесь с радующимися и плачьте с плачущими.
Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira.
16 Будьте единомысленны между собою; не высокомудрствуйте, но последуйте смиренным; не мечтайте о себе;
Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.
17 никому не воздавайте злом за зло, но пекитесь о добром перед всеми человеками.
Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense.
18 Если возможно с вашей стороны, будьте в мире со всеми людьми.
Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere.
19 Не мстите за себя, возлюбленные, но дайте место гневу Божию. Ибо написано: Мне отмщение, Я воздам, говорит Господь.
Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye.
20 Итак, если враг твой голоден, накорми его; если жаждет, напой его: ибо, делая сие, ты соберешь ему на голову горящие уголья.
Koma, “Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya. Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa. Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”
21 Не будь побежден злом, но побеждай зло добром.
Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.

< К Римлянам 12 >