< Псалтирь 98 >

1 Псалом Давида. Воспойте Господу новую песнь, ибо Он сотворил чудеса. Его десница и святая мышца Его доставили Ему победу.
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 Явил Господь спасение Свое, открыл пред очами народов правду Свою.
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 Вспомнил Он милость Свою к Иакову и верность Свою к дому Израилеву. Все концы земли увидели спасение Бога нашего.
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 Восклицайте Господу, вся земля; торжествуйте, веселитесь и пойте;
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 пойте Господу с гуслями, с гуслями и с гласом псалмопения;
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 при звуке труб и рога торжествуйте пред Царем Господом.
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 Да шумит море и что наполняет его, вселенная и живущие в ней;
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 да рукоплещут реки, да ликуют вместе горы
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 пред лицем Господа, ибо Он идет судить землю. Он будет судить вселенную праведно и народы - верно
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.

< Псалтирь 98 >