< Псалтирь 77 >

1 Начальнику хора Идифумова. Псалом Асафа. Глас мой к Богу, и я буду взывать; глас мой к Богу, и Он услышит меня.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
2 В день скорби моей ищу Господа; рука моя простерта ночью и не опускается; душа моя отказывается от утешения.
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
3 Вспоминаю о Боге и трепещу; помышляю, и изнемогает дух мой.
Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
4 Ты не даешь мне сомкнуть очей моих; я потрясен и не могу говорить.
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
5 Размышляю о днях древних, о летах веков минувших;
Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
6 припоминаю песни мои в ночи, беседую с сердцем моим, и дух мой испытывает:
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
7 неужели навсегда отринул Господь, и не будет более благоволить?
“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
8 неужели навсегда престала милость Его, и пресеклось слово Его в род и род?
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
9 неужели Бог забыл миловать? Неужели во гневе затворил щедроты Свои?
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
10 И сказал я: “вот мое горе - изменение десницы Всевышнего”.
Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 Буду вспоминать о делах Господа; буду вспоминать о чудесах Твоих древних;
Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 буду вникать во все дела Твои, размышлять о великих Твоих деяниях.
Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
13 Боже! свят путь Твой. Кто Бог так великий, как Бог наш!
Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 Ты - Бог, творящий чудеса; Ты явил могущество Свое среди народов;
Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 Ты избавил мышцею народ Твой, сынов Иакова и Иосифа.
Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
16 Видели Тебя, Боже, воды, видели Тебя воды и убоялись, и вострепетали бездны.
Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
17 Облака изливали воды, тучи издавали гром, и стрелы Твои летали.
Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 Глас грома Твоего в круге небесном; молнии освещали вселенную; земля содрогалась и тряслась.
Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Путь Твой в море, и стезя Твоя в водах великих, и следы Твои неведомы.
Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
20 Как стадо, вел Ты народ Твой рукою Моисея и Аарона.
Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

< Псалтирь 77 >