< Псалтирь 73 >

1 Как благ Бог к Израилю, к чистым сердцем!
Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 А я - едва не пошатнулись ноги мои, едва не поскользнулись стопы мои, -
Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
3 я позавидовал безумным, видя благоденствие нечестивых,
Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 ибо им нет страданий до смерти их, и крепки силы их;
Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 на работе человеческой нет их, и с прочими людьми не подвергаются ударам.
Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
6 Оттого гордость, как ожерелье, обложила их, и дерзость, как наряд, одевает их;
Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
7 выкатились от жира глаза их, бродят помыслы в сердце;
Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 над всем издеваются, злобно разглашают клевету, говорят свысока;
Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 поднимают к небесам уста свои, и язык их расхаживает по земле.
Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 Потому туда же обращается народ Его, и пьют воду полною чашею,
Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
11 и говорят: “как узнает Бог? и есть ли ведение у Вышнего?”
Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 И вот, эти нечестивые благоденствуют в веке сем, умножают богатство.
Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 Так не напрасно ли я очищал сердце мое и омывал в невинности руки мои,
Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 и подвергал себя ранам всякий день и обличениям всякое утро?
Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 Но если бы я сказал: “буду рассуждать так”, - то я виновен был бы пред родом сынов Твоих.
Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 И думал я, как бы уразуметь это, но это трудно было в глазах моих,
Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
17 доколе не вошел я во святилище Божие и не уразумел конца их.
kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 Так! на скользких путях поставил Ты их и низвергаешь их в пропасти.
Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 Как нечаянно пришли они в разорение, исчезли, погибли от ужасов!
Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 Как сновидение по пробуждении, так Ты, Господи, пробудив их, уничтожишь мечты их.
Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
21 Когда кипело сердце мое, и терзалась внутренность моя,
Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 тогда я был невежда и не разумел; как скот был я пред Тобою.
ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
23 Но я всегда с Тобою: Ты держишь меня за правую руку;
Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 Ты руководишь меня советом Твоим и потом примешь меня в славу.
Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 Кто мне на небе? и с Тобою ничего не хочу на земле.
Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 Изнемогает плоть моя и сердце мое: Бог твердыня сердца моего и часть моя вовек.
Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
27 Ибо вот, удаляющие себя от Тебя гибнут; Ты истребляешь всякого отступающего от Тебя.
Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 А мне благо приближаться к Богу! На Господа Бога я возложил упование мое, чтобы возвещать все дела Твои.
Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

< Псалтирь 73 >