< Псалтирь 72 >

1 О Соломоне. Боже! даруй царю Твой суд и сыну царя Твою правду,
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 да судит праведно людей Твоих и нищих Твоих на суде;
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
3 да принесут горы мир людям и холмы правду;
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 да судит нищих народа, да спасет сынов убогого и смирит притеснителя, -
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
5 и будут бояться Тебя, доколе пребудут солнце и луна, в роды родов.
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 Он сойдет, как дождь на скошенный луг, как капли, орошающие землю;
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 во дни его процветет праведник, и будет обилие мира, доколе не престанет луна;
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 он будет обладать от моря до моря и от реки до концов земли;
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 падут пред ним жители пустынь, и враги его будут лизать прах;
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 цари Фарсиса и островов поднесут ему дань; цари Аравии и Савы принесут дары;
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 и поклонятся ему все цари; все народы будут служить ему;
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 ибо он избавит нищего, вопиющего и угнетенного, у которого нет помощника.
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 Будет милосерд к нищему и убогому, и души убогих спасет;
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 от коварства и насилия избавит души их, и драгоценна будет кровь их пред очами его;
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 и будет жить, и будут давать ему от золота Аравии, и будут молиться о нем непрестанно, всякий день благословлять его;
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 будет обилие хлеба на земле, наверху гор; плоды его будут волноваться, как лес на Ливане, и в городах размножатся люди, как трава на земле;
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 будет имя его вовек; доколе пребывает солнце, будет передаваться имя его; и благословятся в нем племена, все народы ублажат его.
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Благословен Господь Бог, Бог Израилев, един творящий чудеса,
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 и благословенно имя славы Его вовек, и наполнится славою Его вся земля. Аминь и аминь.
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
20 Кончились молитвы Давида, сына Иесеева.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.

< Псалтирь 72 >