< Псалтирь 67 >

1 Начальнику хора. На струнных орудиях. Псалом. Песнь. Боже! будь милостив к нам и благослови нас, освети нас лицем Твоим,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2 дабы познали на земле путь Твой, во всех народах спасение Твое.
Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
3 Да восхвалят Тебя народы, Боже; да восхвалят Тебя народы все.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4 Да веселятся и радуются племена, ибо Ты судишь народы праведно и управляешь на земле племенами.
Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5 Да восхвалят Тебя народы, Боже, да восхвалят Тебя народы все.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
6 Земля дала плод свой; да благословит нас Бог, Бог наш.
Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
7 Да благословит нас Бог, и да убоятся Его все пределы земли.
Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.

< Псалтирь 67 >