< Псалтирь 61 >

1 Начальнику хора. На струнном орудии. Псалом Давида. Услышь, Боже, вопль мой, внемли молитве моей!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
2 От конца земли взываю к Тебе в унынии сердца моего; возведи меня на скалу, для меня недосягаемую,
Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
3 ибо Ты прибежище мое, Ты крепкая защита от врага.
Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
4 Да живу я вечно в жилище Твоем и покоюсь под кровом крыл Твоих,
Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
5 ибо Ты, Боже, услышал обеты мои и дал мне наследие боящихся имени Твоего.
Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
6 Приложи дни ко дням царя, лета его продли в род и род,
Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
7 да пребудет он вечно пред Богом; заповедуй милости и истине охранять его.
Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
8 И я буду петь имени Твоему вовек, исполняя обеты мои всякий день.
Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

< Псалтирь 61 >