< Псалтирь 6 >

1 Начальнику хора. На восьмиструнном. Псалом Давида. Господи! не в ярости Твоей обличай меня и не во гневе Твоем наказывай меня.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Помилуй меня, Господи, ибо я немощен; исцели меня, Господи, ибо кости мои потрясены;
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 и душа моя сильно потрясена; Ты же, Господи, доколе?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Обратись, Господи, избавь душу мою, спаси меня ради милости Твоей,
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 ибо в смерти нет памятования о Тебе: во гробе кто будет славить Тебя? (Sheol h7585)
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
6 Утомлен я воздыханиями моими: каждую ночь омываю ложе мое, слезами моими омочаю постель мою.
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 Иссохло от печали око мое, обветшало от всех врагов моих.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Удалитесь от меня все, делающие беззаконие, ибо услышал Господь голос плача моего,
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 услышал Господь моление мое; Господь примет молитву мою.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 Да будут постыжены и жестоко поражены все враги мои; да возвратятся и постыдятся мгновенно.
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

< Псалтирь 6 >