< Псалтирь 5 >

1 Начальнику хора. На духовых орудиях. Псалом Давида. Услышь, Господи, слова мои, уразумей помышления мои.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide. Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova, ganizirani za kusisima kwanga
2 Внемли гласу вопля моего, Царь мой и Бог мой! ибо я к Тебе молюсь.
Mverani kulira kwanga kofuna thandizo, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga, pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
3 Господи! рано услышь голос мой, рано предстану пред Тобою, и буду ожидать,
Mmawa, Yehova mumamva mawu anga; Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu ndi kudikira mwachiyembekezo.
4 ибо Ты Бог, не любящий беззакония; у Тебя не водворится злой;
Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa; choyipa sichikhala pamaso panu.
5 нечестивые не пребудут пред очами Твоими: Ты ненавидишь всех, делающих беззаконие.
Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
6 Ты погубишь говорящих ложь; кровожадного и коварного гнушается Господь.
Mumawononga iwo amene amanena mabodza; anthu akupha ndi achinyengo, Yehova amanyansidwa nawo.
7 А я, по множеству милости Твоей, войду в дом Твой, поклонюсь святому храму Твоему в страхе Твоем.
Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu, ndidzalowa mʼNyumba yanu; mwa ulemu ndidzaweramira pansi kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
8 Господи! путеводи меня в правде Твоей, ради врагов моих; уровняй предо мною путь Твой.
Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu chifukwa cha adani anga ndipo wongolani njira yanu pamaso panga.
9 Ибо нет в устах их истины: сердце их - пагуба, гортань их - открытый гроб, языком своим льстят.
Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike; mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko. Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
10 Осуди их, Боже, да падут они от замыслов своих; по множеству нечестия их, отвергни их, ибо они возмутились против Тебя.
Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu! Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo. Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri, pakuti awukira Inu.
11 И возрадуются все уповающие на Тебя, вечно будут ликовать, и Ты будешь покровительствовать им; и будут хвалиться Тобою любящие имя Твое.
Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere; lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe. Aphimbeni ndi chitetezo chanu, iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
12 Ибо Ты благословляешь праведника, Господи; благоволением, как щитом, венчаешь его.
Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama; mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.

< Псалтирь 5 >