< Псалтирь 47 >

1 Начальнику хора. Сынов Кореевых. Псалом. Восплещите руками все народы, воскликните Богу гласом радости;
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 ибо Господь Всевышний страшен, - великий Царь над всею землею;
Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 покорил нам народы и племена под ноги наши;
Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 избрал нам наследие наше, красу Иакова, которого возлюбил.
Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
5 Восшел Бог при восклицаниях, Господь при звуке трубном.
Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Пойте Богу нашему, пойте; пойте Царю нашему, пойте,
Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 ибо Бог - Царь всей земли; пойте все разумно.
Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
8 Бог воцарился над народами, Бог воссел на святом престоле Своем;
Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 князья народов собрались к народу Бога Авраамова, ибо щиты земли - Божии; Он превознесен над ними.
Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.

< Псалтирь 47 >