< Псалтирь 4 >

1 Начальнику хора. На струнных орудиях. Псалом Давида. Когда я взываю, услышь меня, Боже правды моей! В тесноте Ты давал мне простор. Помилуй меня и услышь молитву мою.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
2 Сыны мужей! доколе слава моя будет в поругании? доколе будете любить суету и искать лжи?
Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
3 Знайте, что Господь отделил для Себя святаго Своего; Господь слышит, когда я призываю Его.
Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
4 Гневаясь, не согрешайте: размыслите в сердцах ваших на ложах ваших, и утишитесь;
Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
5 приносите жертвы правды и уповайте на Господа.
Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
6 Многие говорят: “кто покажет нам благо?” Яви нам свет лица Твоего, Господи!
Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
7 Ты исполнил сердце мое веселием с того времени, как у них хлеб и вино умножились.
Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
8 Спокойно ложусь я и сплю, ибо Ты, Господи, един даешь мне жить в безопасности.
Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.

< Псалтирь 4 >