< Псалтирь 36 >

1 Начальнику хора. Раба Господня Давида. Нечестие беззаконного говорит в сердце моем: нет страха Божия пред глазами его,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova. Uthenga uli mu mtima mwanga wonena za kuchimwa kwa munthu woyipa: Mu mtima mwake mulibe kuopa Mulungu.
2 ибо он льстит себе в глазах своих, будто отыскивает беззаконие свое, чтобы возненавидеть его;
Pakuti iye mʼkuona kwake amadzinyenga yekha kwambiri, sazindikira kapena kudana ndi tchimo lake.
3 слова уст его - неправда и лукавство; не хочет он вразумиться, чтобы делать добро;
Mawu a pakamwa pake ndi oyipa ndi achinyengo; iyeyo waleka kukhala wanzeru ndi kuchita zabwino.
4 на ложе своем замышляет беззаконие, становится на путь недобрый, не гнушается злом.
Ngakhale ali pa bedi pake amakonzekera zoyipa; iye amadzipereka yekha ku njira ya uchimo ndipo sakana cholakwa chilichonse.
5 Господи! милость Твоя до небес, истина Твоя до облаков!
Chikondi chanu Yehova, chimafika ku mayiko a kumwamba, kukhulupirika kwanu mpaka ku mitambo.
6 Правда Твоя, как горы Божии, и судьбы Твои - бездна великая! Человеков и скотов хранишь Ты, Господи!
Chilungamo chanu Mulungu chili ngati mapiri aakulu, chiweruzo chanu chili ngati kuzama kwakukulu. Yehova mumasunga munthu pamodzi ndi chinyama.
7 Как драгоценна милость Твоя, Боже! Сыны человеческие в тени крыл Твоих покойны:
Chikondi chanu chosatha ndi chamtengowapatali! Otchuka pamodzi ndi anthu wamba pakati pa anthu amapeza pothawirapo mu mthunzi wa mapiko anu.
8 насыщаются от тука дома Твоего, и из потока сладостей Твоих Ты напояешь их,
Iwo amadyerera zinthu zambiri za mʼnyumba yanu; Inu mumawapatsa chakumwa kuchokera mu mtsinje wanu wachikondwerero.
9 ибо у Тебя источник жизни; во свете Твоем мы видим свет.
Pakuti kwa Inu kuli kasupe wamoyo; mʼkuwala kwanu ifenso timaona kuwala.
10 Продли милость Твою к знающим Тебя и правду Твою к правым сердцем,
Pitirizani chikondi chanu pa iwo amene amakudziwani, chilungamo chanu kwa olungama mtima.
11 да не наступит на меня нога гордыни, и рука грешника да не изгонит меня:
Musalole kuti phazi la wodzikuza libwere kulimbana nane, kapena dzanja la oyipa kundithamangitsa.
12 там пали делающие беззаконие, низринуты и не могут встать.
Onani momwe ochita zoyipa agonera atagwa, aponyeni pansi, kuti asathe kudzukanso!

< Псалтирь 36 >