< Псалтирь 34 >

1 Псалом Давида, когда он притворился безумным пред Авимелехом и был изгнан от него и удалился. Благословлю Господа во всякое время; хвала Ему непрестанно в устах моих.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 Господом будет хвалиться душа моя; услышат кроткие и возвеселятся.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Величайте Господа со мною, и превознесем имя Его вместе.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 Я взыскал Господа, и Он услышал меня, и от всех опасностей моих избавил меня.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 Кто обращал взор к Нему, те просвещались, и лица их не постыдятся.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 Сей нищий воззвал, - и Господь услышал и спас его от всех бед его.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 Ангел Господень ополчается вокруг боящихся Его и избавляет их.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 Вкусите, и увидите, как благ Господь! Блажен человек, который уповает на Него!
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Бойтесь Господа, святые Его, ибо нет скудости у боящихся Его.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Скимны бедствуют и терпят голод, а ищущие Господа не терпят нужды ни в каком благе.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Придите, дети, послушайте меня: страху Господню научу вас.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Хочет ли человек жить и любит ли долгоденствие, чтобы видеть благо?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Удерживай язык свой от зла и уста свои от коварных слов.
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Уклоняйся от зла и делай добро; ищи мира и следуй за ним.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 Очи Господни обращены на праведников, и уши Его - к воплю их.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 Но лице Господне против делающих зло, чтобы истребить с земли память о них.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 Взывают праведные, и Господь слышит, и от всех скорбей их избавляет их.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Близок Господь к сокрушенным сердцем и смиренных духом спасет.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Много скорбей у праведного, и от всех их избавит его Господь.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Он хранит все кости его; ни одна из них не сокрушится.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 Убьет грешника зло, и ненавидящие праведного погибнут.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Избавит Господь душу рабов Своих, и никто из уповающих на Него не погибнет.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

< Псалтирь 34 >