< Псалтирь 30 >

1 Псалом Давида; песнь при обновлении дома. Превознесу Тебя, Господи, что Ты поднял меня и не дал моим врагам восторжествовать надо мною.
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
2 Господи, Боже мой! я воззвал к Тебе, и Ты исцелил меня.
Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
3 Господи! Ты вывел из ада душу мою и оживил меня, чтобы я не сошел в могилу. (Sheol h7585)
Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
4 Пойте Господу, святые Его, славьте память святыни Его,
Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
5 ибо на мгновение гнев Его, на всю жизнь благоволение Его: вечером водворяется плач, а на утро радость.
Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
6 И я говорил в благоденствии моем: “не поколеблюсь вовек”.
Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
7 По благоволению Твоему, Господи, Ты укрепил гору мою; но Ты сокрыл лице Твое, и я смутился.
Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
8 Тогда к Тебе, Господи, взывал я, и Господа умолял:
Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
9 “что пользы в крови моей, когда я сойду в могилу? будет ли прах славить Тебя? будет ли возвещать истину Твою?
“Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
10 услышь, Господи, и помилуй меня; Господи! будь мне помощником”.
Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
11 И Ты обратил сетование мое в ликование, снял с меня вретище и препоясал меня веселием,
Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
12 да славит Тебя душа моя и да не умолкает. Господи, Боже мой! буду славить Тебя вечно.
kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.

< Псалтирь 30 >