< Псалтирь 29 >

1 Псалом Давида. Воздайте Господу, сыны Божии, воздайте Господу славу и честь,
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 воздайте Господу славу имени Его; поклонитесь Господу в благолепном святилище Его.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 Глас Господень над водами; Бог славы возгремел, Господь над водами многими.
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 Глас Господа силен, глас Господа величествен.
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 Глас Господа сокрушает кедры; Господь сокрушает кедры Ливанские
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 и заставляет их скакать подобно тельцу, Ливан и Сирион, подобно молодому единорогу.
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 Глас Господа высекает пламень огня.
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 Глас Господа потрясает пустыню; потрясает Господь пустыню Кадес.
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 Глас Господа разрешает от бремени ланей и обнажает леса; и во храме Его все возвещает о Его славе.
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 Господь восседал над потопом, и будет восседать Господь царем вовек.
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 Господь даст силу народу Своему, Господь благословит народ Свой миром.
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

< Псалтирь 29 >