< Псалтирь 133 >

1 Песнь восхождения. Давида. Как хорошо и как приятно жить братьям вместе!
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Onani, nʼkokoma ndi kokondweretsa ndithu pamene abale akhala pamodzi mwachiyanjano!
2 Это - как драгоценный елей на голове, стекающий на бороду, бороду Ааронову, стекающий на края одежды его;
Zili ngati mafuta amtengowapatali othiridwa pa mutu, otsikira ku ndevu, ku ndevu za Aaroni, oyenderera mpaka mʼkhosi mwa mkanjo wake.
3 как роса Ермонская, сходящая на горы Сионские, ибо там заповедал Господь благословение и жизнь на веки.
Zili ngati mame a ku Heremoni otsikira pa Phiri la Ziyoni. Pakuti pamenepo Yehova amaperekapo dalitso, ndiwo moyo wamuyaya.

< Псалтирь 133 >