< Псалтирь 127 >

1 Песнь восхождения. Соломона. Если Господь не созиждет дома, напрасно трудятся строящие его; если Господь не охранит города, напрасно бодрствует страж.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
2 Напрасно вы рано встаете, поздно просиживаете, едите хлеб печали, тогда как возлюбленному Своему Он дает сон.
Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
3 Вот наследие от Господа: дети; награда от Него - плод чрева.
Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
4 Что стрелы в руке сильного, то сыновья молодые.
Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
5 Блажен человек, который наполнил ими колчан свой! Не останутся они в стыде, когда будут говорить с врагами в воротах
Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

< Псалтирь 127 >