< Псалтирь 121 >

1 Песнь восхождения. Возвожу очи мои к горам, откуда придет помощь моя.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Помощь моя от Господа, сотворившего небо и землю.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 Не даст Он поколебаться ноге твоей, не воздремлет хранящий тебя;
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 не дремлет и не спит хранящий Израиля.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 Господь - хранитель твой; Господь - сень твоя с правой руки твоей.
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 Днем солнце не поразит тебя, ни луна ночью.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 Господь сохранит тебя от всякого зла; сохранит душу твою Господь.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 Господь будет охранять выхождение твое и вхождение твое отныне и вовек.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

< Псалтирь 121 >