< Псалтирь 119 >

1 Аллилуия. Блаженны непорочные в пути, ходящие в законе Господнем.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Блаженны хранящие откровения Его, всем сердцем ищущие Его.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Они не делают беззакония, ходят путями Его.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Ты заповедал повеления Твои хранить твердо.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 О, если бы направлялись пути мои к соблюдению уставов Твоих!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Тогда я не постыдился бы, взирая на все заповеди Твои:
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 я славил бы Тебя в правоте сердца, поучаясь судам правды Твоей.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Буду хранить уставы Твои; не оставляй меня совсем.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Как юноше содержать в чистоте путь свой? - Хранением себя по слову Твоему.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Всем сердцем моим ищу Тебя; не дай мне уклониться от заповедей Твоих.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 В сердце моем сокрыл я слово Твое, чтобы не грешить пред Тобою.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Благословен Ты, Господи! научи меня уставам Твоим.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Устами моими возвещал я все суды уст Твоих.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 На пути откровений Твоих я радуюсь, как во всяком богатстве.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 О заповедях Твоих размышляю, и взираю на пути Твои.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Уставами Твоими утешаюсь, не забываю слова Твоего.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Яви милость рабу Твоему, и буду жить и хранить слово Твое.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Открой очи мои, и увижу чудеса закона Твоего.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Странник я на земле; не скрывай от меня заповедей Твоих.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Истомилась душа моя желанием судов Твоих во всякое время.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Ты укротил гордых, проклятых, уклоняющихся от заповедей Твоих.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Сними с меня поношение и посрамление, ибо я храню откровения Твои.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Князья сидят и сговариваются против меня, а раб Твой размышляет об уставах Твоих.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Откровения Твои - утешение мое, и уставы Твои - советники мои.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Душа моя повержена в прах; оживи меня по слову Твоему.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Объявил я пути мои, и Ты услышал меня; научи меня уставам Твоим.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Дай мне уразуметь путь повелений Твоих, и буду размышлять о чудесах Твоих.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Душа моя истаевает от скорби: укрепи меня по слову Твоему.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Удали от меня путь лжи, и закон Твой даруй мне.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Я избрал путь истины, поставил пред собою суды Твои.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Я прилепился к откровениям Твоим, Господи; не постыди меня.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Потеку путем заповедей Твоих, когда Ты расширишь сердце мое.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Укажи мне, Господи, путь уставов Твоих, и я буду держаться его до конца.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Вразуми меня, и буду соблюдать закон Твой и хранить его всем сердцем.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Поставь меня на стезю заповедей Твоих, ибо я возжелал ее.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Приклони сердце мое к откровениям Твоим, а не к корысти.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Отврати очи мои, чтобы не видеть суеты; животвори меня на пути Твоем.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Утверди слово Твое рабу Твоему, ради благоговения пред Тобою.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Отврати поношение мое, которого я страшусь, ибо суды Твои благи.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Вот, я возжелал повелений Твоих; животвори меня правдою Твоею.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Да придут ко мне милости Твои, Господи, спасение Твое по слову Твоему,
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 и я дам ответ поносящему меня, ибо уповаю на слово Твое.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Не отнимай совсем от уст моих слова истины, ибо я уповаю на суды Твои
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 и буду хранить закон Твой всегда, во веки и веки;
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 буду ходить свободно, ибо я взыскал повелений Твоих;
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 буду говорить об откровениях Твоих пред царями и не постыжусь;
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 буду утешаться заповедями Твоими, которые возлюбил;
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 руки мои буду простирать к заповедям Твоим, которые возлюбил, и размышлять об уставах Твоих.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Вспомни слово Твое к рабу Твоему, на которое Ты повелел мне уповать:
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 это - утешение в бедствии моем, что слово Твое оживляет меня.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Гордые крайне ругались надо мною, но я не уклонился от закона Твоего.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Вспоминал суды Твои, Господи, от века, и утешался.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Ужас овладевает мною при виде нечестивых, оставляющих закон Твой.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Уставы Твои были песнями моими на месте странствований моих.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Ночью вспоминал я имя Твое, Господи, и хранил закон Твой.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Он стал моим, ибо повеления Твои храню.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Удел мой, Господи, сказал я, соблюдать слова Твои.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Молился я Тебе всем сердцем: помилуй меня по слову Твоему.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Размышлял о путях моих и обращал стопы мои к откровениям Твоим.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Спешил и не медлил соблюдать заповеди Твои.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Сети нечестивых окружили меня, но я не забывал закона Твоего.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 В полночь вставал славословить Тебя за праведные суды Твои.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Общник я всем боящимся Тебя и хранящим повеления Твои.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Милости Твоей, Господи, полна земля; научи меня уставам Твоим.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Благо сотворил Ты рабу Твоему, Господи, по слову Твоему.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Доброму разумению и ведению научи меня, ибо заповедям Твоим я верую.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Прежде страдания моего я заблуждался; а ныне слово Твое храню.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Благ и благодетелен Ты, Господи; научи меня уставам Твоим.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Гордые сплетают на меня ложь; я же всем сердцем буду хранить повеления Твои.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Ожирело сердце их, как тук; я же законом Твоим утешаюсь.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Благо мне, что я пострадал, дабы научиться уставам Твоим.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Закон уст Твоих для меня лучше тысяч золота и серебра.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Руки Твои сотворили меня и устроили меня; вразуми меня, и научусь заповедям Твоим.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Боящиеся Тебя увидят меня - и возрадуются, что я уповаю на слово Твое.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Знаю, Господи, что суды Твои праведны и по справедливости Ты наказал меня.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Да будет же милость Твоя утешением моим, по слову Твоему к рабу Твоему.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Да придет ко мне милосердие Твое, и я буду жить; ибо закон Твой - утешение мое.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Да будут постыжены гордые, ибо безвинно угнетают меня; я размышляю о повелениях Твоих.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Да обратятся ко мне боящиеся Тебя и знающие откровения Твои.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Да будет сердце мое непорочно в уставах Твоих, чтобы я не посрамился.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Истаевает душа моя о спасении Твоем; уповаю на слово Твое.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Истаевают очи мои о слове Твоем; я говорю: когда Ты утешишь меня?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Я стал, как мех в дыму, но уставов Твоих не забыл.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Сколько дней раба Твоего? Когда произведешь суд над гонителями моими?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Яму вырыли мне гордые, вопреки закону Твоему.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Все заповеди Твои - истина; несправедливо преследуют меня: помоги мне;
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 едва не погубили меня на земле, но я не оставил повелений Твоих.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 По милости Твоей оживляй меня, и буду хранить откровения уст Твоих.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 На веки, Господи, слово Твое утверждено на небесах;
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 истина Твоя в род и род. Ты поставил землю, и она стоит.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 По определениям Твоим все стоит доныне, ибо все служит Тебе.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Если бы не закон Твой был утешением моим, погиб бы я в бедствии моем.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Вовек не забуду повелений Твоих, ибо ими Ты оживляешь меня.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Твой я, спаси меня; ибо я взыскал повелений Твоих.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Нечестивые подстерегают меня, чтобы погубить; а я углубляюсь в откровения Твои.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Я видел предел всякого совершенства, но Твоя заповедь безмерно обширна.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Как люблю я закон Твой! весь день размышляю о нем.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Заповедью Твоею Ты соделал меня мудрее врагов моих, ибо она всегда со мною.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Я стал разумнее всех учителей моих, ибо размышляю об откровениях Твоих.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Я сведущ более старцев, ибо повеления Твои храню.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 От всякого злого пути удерживаю ноги мои, чтобы хранить слово Твое;
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 от судов Твоих не уклоняюсь, ибо Ты научаешь меня.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Как сладки гортани моей слова Твои! лучше меда устам моим.
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Повелениями Твоими я вразумлен; потому ненавижу всякий путь лжи.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Слово Твое - светильник ноге моей и свет стезе моей.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Я клялся хранить праведные суды Твои, и исполню.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Сильно угнетен я, Господи; оживи меня по слову Твоему.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Благоволи же, Господи, принять добровольную жертву уст моих, и судам Твоим научи меня.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Душа моя непрестанно в руке моей, но закона Твоего не забываю.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Нечестивые поставили для меня сеть, но я не уклонился от повелений Твоих.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Откровения Твои я принял, как наследие на веки, ибо они веселие сердца моего.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Я приклонил сердце мое к исполнению уставов Твоих навек, до конца.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Вымыслы человеческие ненавижу, а закон Твой люблю.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Ты покров мой и щит мой; на слово Твое уповаю.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Удалитесь от меня, беззаконные, и буду хранить заповеди Бога моего.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Укрепи меня по слову Твоему, и буду жить; не посрами меня в надежде моей;
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 поддержи меня, и спасусь; и в уставы Твои буду вникать непрестанно.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Всех, отступающих от уставов Твоих, Ты низлагаешь, ибо ухищрения их - ложь.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Как изгарь, отметаешь Ты всех нечестивых земли; потому я возлюбил откровения Твои.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Трепещет от страха Твоего плоть моя, и судов Твоих я боюсь.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Я совершал суд и правду; не предай меня гонителям моим.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Заступи раба Твоего ко благу его, чтобы не угнетали меня гордые.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Истаевают очи мои, ожидая спасения Твоего и слова правды Твоей.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Сотвори с рабом Твоим по милости Твоей, и уставам Твоим научи меня.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Я раб Твой: вразуми меня, и познаю откровения Твои.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Время Господу действовать: закон Твой разорили.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 А я люблю заповеди Твои более золота, и золота чистого.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Все повеления Твои - все признаю справедливыми; всякий путь лжи ненавижу.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Дивны откровения Твои; потому хранит их душа моя.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Откровение слов Твоих просвещает, вразумляет простых.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Открываю уста мои и вздыхаю, ибо заповедей Твоих жажду.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Призри на меня и помилуй меня, как поступаешь с любящими имя Твое.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Утверди стопы мои в слове Твоем и не дай овладеть мною никакому беззаконию;
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 избавь меня от угнетения человеческого, и буду хранить повеления Твои;
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 осияй раба Твоего светом лица Твоего и научи меня уставам Твоим.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Из глаз моих текут потоки вод оттого, что не хранят закона Твоего.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Праведен Ты, Господи, и справедливы суды Твои.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Откровения Твои, которые Ты заповедал, - правда и совершенная истина.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Ревность моя снедает меня, потому что мои враги забыли слова Твои.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Слово Твое весьма чисто, и раб Твой возлюбил его.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Мал я и презрен, но повелений Твоих не забываю.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Правда Твоя - правда вечная, и закон Твой - истина.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Скорбь и горесть постигли меня; заповеди Твои - утешение мое.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Правда откровений Твоих вечна: вразуми меня, и буду жить.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Взываю всем сердцем моим: услышь меня, Господи, - и сохраню уставы Твои.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Призываю Тебя: спаси меня, и буду хранить откровения Твои.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Предваряю рассвет и взываю; на слово Твое уповаю.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Очи мои предваряют утреннюю стражу, чтобы мне углубляться в слово Твое.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Услышь голос мой по милости Твоей, Господи; по суду Твоему оживи меня.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Приблизились замышляющие лукавство; далеки они от закона Твоего.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Близок Ты, Господи, и все заповеди Твои - истина.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Издавна узнал я об откровениях Твоих, что Ты утвердил их на веки.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Воззри на бедствие мое и избавь меня, ибо я не забываю закона Твоего.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Вступись в дело мое и защити меня; по слову Твоему оживи меня.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Далеко от нечестивых спасение, ибо они уставов Твоих не ищут.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Много щедрот Твоих, Господи; по суду Твоему оживи меня.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Много у меня гонителей и врагов, но от откровений Твоих я не удаляюсь.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Вижу отступников, и сокрушаюсь, ибо они не хранят слова Твоего.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Зри, как я люблю повеления Твои; по милости Твоей, Господи, оживи меня.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Основание слова Твоего истинно, и вечен всякий суд правды Твоей.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Князья гонят меня безвинно, но сердце мое боится слова Твоего.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Радуюсь я слову Твоему, как получивший великую прибыль.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Ненавижу ложь и гнушаюсь ею; закон же Твой люблю.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Семикратно в день прославляю Тебя за суды правды Твоей.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Велик мир у любящих закон Твой, и нет им преткновения.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Уповаю на спасение Твое, Господи, и заповеди Твои исполняю.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Душа моя хранит откровения Твои, и я люблю их крепко.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Храню повеления Твои и откровения Твои, ибо все пути мои пред Тобою.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Да приблизится вопль мой пред лице Твое, Господи; по слову Твоему вразуми меня.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Да придет моление мое пред лице Твое; по слову Твоему избавь меня.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Уста мои произнесут хвалу, когда Ты научишь меня уставам Твоим.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Язык мой возгласит слово Твое, ибо все заповеди Твои праведны.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Да будет рука Твоя в помощь мне, ибо я повеления Твои избрал.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Жажду спасения Твоего, Господи, и закон Твой - утешение мое.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Да живет душа моя и славит Тебя, и суды Твои да помогут мне.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Я заблудился, как овца потерянная: взыщи раба Твоего, ибо я заповедей Твоих не забыл.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Псалтирь 119 >