< Псалтирь 112 >

1 Аллилуия. Блажен муж, боящийся Господа и крепко любящий заповеди Его.
Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 Сильно будет на земле семя его; род правых благословится.
Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3 Обилие и богатство в доме его, и правда его пребывает вовек.
Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Во тьме восходит свет правым; благ он и милосерд и праведен.
Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5 Добрый человек милует и взаймы дает; он даст твердость словам своим на суде.
Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6 Он вовек не поколеблется; в вечной памяти будет праведник.
Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7 Не убоится худой молвы: сердце его твердо, уповая на Господа.
Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8 Утверждено сердце его: он не убоится, когда посмотрит на врагов своих.
Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9 Он расточил, раздал нищим; правда его пребывает во веки; рог его вознесется во славе.
Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10 Нечестивый увидит это и будет досадовать, заскрежещет зубами своими и истает. Желание нечестивых погибнет.
Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.

< Псалтирь 112 >