< Псалтирь 111 >

1 Аллилуия. Славлю Тебя, Господи, всем сердцем моим в совете праведных и в собрании.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 Велики дела Господни, вожделенны для всех, любящих оные.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 Дело Его - слава и красота, и правда Его пребывает вовек.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Памятными соделал Он чудеса Свои; милостив и щедр Господь.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 Пищу дает боящимся Его; вечно помнит завет Свой.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 Силу дел Своих явил Он народу Своему, чтобы дать ему наследие язычников.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 Дела рук Его - истина и суд; все заповеди Его верны,
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 тверды на веки и веки, основаны на истине и правоте.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 Избавление послал Он народу Своему; заповедал на веки завет Свой. Свято и страшно имя Его!
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 Начало мудрости - страх Господень; разум верный у всех, исполняющих заповеди Его. Хвала Ему пребудет вовек
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< Псалтирь 111 >