< Псалтирь 109 >

1 Начальнику хора. Псалом Давида. Боже хвалы моей! не премолчи,
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 ибо отверзлись на меня уста нечестивые и уста коварные; говорят со мною языком лживым;
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 отовсюду окружают меня словами ненависти, вооружаются против меня без причины;
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 за любовь мою они враждуют на меня, а я молюсь;
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 воздают мне за добро злом, за любовь мою - ненавистью.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Поставь над ним нечестивого, и диавол да станет одесную его.
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 Когда будет судиться, да выйдет виновным, и молитва его да будет в грех;
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 да будут дни его кратки, и достоинство его да возьмет другой;
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 дети его да будут сиротами, и жена его - вдовою;
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 да скитаются дети его и нищенствуют, и просят хлеба из развалин своих;
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 да захватит заимодавец все, что есть у него, и чужие да расхитят труд его;
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 да не будет сострадающего ему, да не будет милующего сирот его;
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 да будет потомство его на погибель, и да изгладится имя их в следующем роде;
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 да будет воспомянуто пред Господом беззаконие отцов его, и грех матери его да не изгладится;
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 да будут они всегда в очах Господа, и да истребит Он память их на земле,
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 за то, что он не думал оказывать милость, но преследовал человека бедного и нищего и сокрушенного сердцем, чтобы умертвить его;
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 возлюбил проклятие, - оно и придет на него; не восхотел благословения, - оно и удалится от него;
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 да облечется проклятием, как ризою, и да войдет оно, как вода, во внутренность его и, как елей, в кости его;
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 да будет оно ему, как одежда, в которую он одевается, и как пояс, которым всегда опоясывается.
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Таково воздаяние от Господа врагам моим и говорящим злое на душу мою!
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 Со мною же, Господи, Господи, твори ради имени Твоего, ибо блага милость Твоя; спаси меня,
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 ибо я беден и нищ, и сердце мое уязвлено во мне.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Я исчезаю, как уклоняющаяся тень; гонят меня, как саранчу.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Колени мои изнемогли от поста, и тело мое лишилось тука.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Я стал для них посмешищем: увидев меня, кивают головами своими.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Помоги мне, Господи, Боже мой, спаси меня по милости Твоей,
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 да познают, что это - Твоя рука, и что Ты, Господи, соделал это.
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Они проклинают, а Ты благослови; они восстают, но да будут постыжены; раб же Твой да возрадуется.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Да облекутся противники мои бесчестьем и, как одеждою, покроются стыдом своим.
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 И я громко буду устами моими славить Господа и среди множества прославлять Его,
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 ибо Он стоит одесную бедного, чтобы спасти его от судящих душу его
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

< Псалтирь 109 >