< Псалтирь 108 >

1 Песнь. Псалом Давида. Готово сердце мое, Боже, готово сердце мое; буду петь и воспевать во славе моей.
Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
2 Воспрянь, псалтирь и гусли! Я встану рано.
Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
3 Буду славить Тебя, Господи, между народами; буду воспевать Тебя среди племен,
Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
4 ибо превыше небес милость Твоя и до облаков истина Твоя.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
5 Будь превознесен выше небес, Боже; над всею землею да будет слава Твоя,
Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
6 дабы избавились возлюбленные Твои: спаси десницею Твоею и услышь меня.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
7 Бог сказал во святилище Своем: “восторжествую, разделю Сихем и долину Сокхоф размерю;
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
8 Мой Галаад, Мой Манассия, Ефрем - крепость главы Моей, Иуда - скипетр Мой,
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
9 Моав - умывальная чаша Моя, на Едома простру сапог Мой, над землею Филистимскою восклицать буду”.
Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
10 Кто введет меня в укрепленный город? Кто доведет меня до Едома?
Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
11 Не Ты ли, Боже, Который отринул нас и не выходишь, Боже, с войсками нашими?
Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
12 Подай нам помощь в тесноте, ибо защита человеческая суетна.
Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
13 С Богом мы окажем силу: Он низложит врагов наших
Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.

< Псалтирь 108 >