< Псалтирь 105 >

1 Славьте Господа; призывайте имя Его; возвещайте в народах дела Его;
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 воспойте Ему и пойте Ему; поведайте о всех чудесах Его.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Хвалитесь именем Его святым; да веселится сердце ищущих Господа.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Ищите Господа и силы Его, ищите лица Его всегда.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Воспоминайте чудеса Его, которые сотворил, знамения Его и суды уст Его,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 вы, семя Авраамово, рабы Его, сыны Иакова, избранные Его.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Он Господь Бог наш: по всей земле суды Его.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Вечно помнит завет Свой, слово, которое заповедал в тысячу родов,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 которое завещал Аврааму, и клятву Свою Исааку,
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 и поставил то Иакову в закон и Израилю в завет вечный,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 говоря: “тебе дам землю Ханаанскую в удел наследия вашего”.
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 Когда их было еще мало числом, очень мало, и они были пришельцами в ней
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 и переходили от народа к народу, из царства к иному племени,
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 никому не позволял обижать их и возбранял о них царям:
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 “не прикасайтесь к помазанным Моим, и пророкам Моим не делайте зла”.
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 И призвал голод на землю; всякий стебель хлебный истребил.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Послал пред ними человека: в рабы продан был Иосиф.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Стеснили оковами ноги его; в железо вошла душа его,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 доколе исполнилось слово Его: слово Господне испытало его.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Послал царь, и разрешил его владетель народов и освободил его;
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 поставил его господином над домом своим и правителем над всем владением своим,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 чтобы он наставлял вельмож его по своей душе и старейшин его учил мудрости.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Тогда пришел Израиль в Египет, и переселился Иаков в землю Хамову.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 И весьма размножил Бог народ Свой и сделал его сильнее врагов его.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Возбудил в сердце их ненависть против народа Его и ухищрение против рабов Его.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Послал Моисея, раба Своего, Аарона, которого избрал.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Они показали между ними слова знамений Его и чудеса Его в земле Хамовой.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Послал тьму и сделал мрак, и не воспротивились слову Его.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Преложил воду их в кровь, и уморил рыбу их.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Земля их произвела множество жаб даже в спальне царей их.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Он сказал, и пришли разные насекомые, скнипы во все пределы их.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Вместо дождя послал на них град, палящий огонь на землю их,
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 и побил виноград их и смоковницы их, и сокрушил дерева в пределах их.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Сказал, и пришла саранча и гусеницы без числа;
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 и съели всю траву на земле их, и съели плоды на полях их.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 И поразил всякого первенца в земле их, начатки всей силы их.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 И вывел Израильтян с серебром и золотом, и не было в коленах их болящего.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Обрадовался Египет исшествию их; ибо страх от них напал на него.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Простер облако в покров им и огонь, чтобы светить им ночью.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Просили, и Он послал перепелов, и хлебом небесным насыщал их.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Разверз камень, и потекли воды, потекли рекою по местам сухим,
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 ибо вспомнил Он святое слово Свое к Аврааму, рабу Своему,
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 и вывел народ Свой в радости, избранных Своих в веселии,
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 и дал им земли народов, и они наследовали труд иноплеменных,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 чтобы соблюдали уставы Его и хранили законы Его. Аллилуия!
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Псалтирь 105 >