< Псалтирь 102 >

1 Молитва страждущего, когда он унывает и изливает пред Господом печаль свою. Господи! услышь молитву мою, и вопль мой да придет к Тебе.
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Не скрывай лица Твоего от меня; в день скорби моей приклони ко мне ухо Твое; в день, когда воззову к Тебе, скоро услышь меня;
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 ибо исчезли, как дым, дни мои, и кости мои обожжены, как головня;
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 сердце мое поражено, и иссохло, как трава, так что я забываю есть хлеб мой;
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 от голоса стенания моего кости мои прильпнули к плоти моей.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 Я уподобился пеликану в пустыне; я стал как филин на развалинах;
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 не сплю и сижу, как одинокая птица на кровле.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 Всякий день поносят меня враги мои, и злобствующие на меня клянут мною.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 Я ем пепел, как хлеб, и питье мое растворяю слезами,
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 от гнева Твоего и негодования Твоего, ибо Ты вознес меня и низверг меня.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 Дни мои - как уклоняющаяся тень, и я иссох, как трава.
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 Ты же, Господи, вовек пребываешь, и память о Тебе в род и род.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Ты восстанешь, умилосердишься над Сионом, ибо время помиловать его, - ибо пришло время;
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 ибо рабы Твои возлюбили и камни его, и о прахе его жалеют.
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 И убоятся народы имени Господня, и все цари земные - славы Твоей.
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Ибо созиждет Господь Сион и явится во славе Своей;
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 призрит на молитву беспомощных и не презрит моления их.
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 Напишется о сем для рода последующего, и поколение грядущее восхвалит Господа,
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 ибо Он приникнул со святой высоты Своей, с небес призрел Господь на землю,
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 чтобы услышать стон узников, разрешить сынов смерти,
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 дабы возвещали на Сионе имя Господне и хвалу Его - в Иерусалиме,
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 когда соберутся народы вместе и царства для служения Господу.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 Изнурил Он на пути силы мои, сократил дни мои.
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Я сказал: Боже мой! не восхити меня в половине дней моих. Твои лета в роды родов.
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 В начале Ты, Господи, основал землю, и небеса - дело Твоих рук;
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 они погибнут, а Ты пребудешь; и все они, как риза, обветшают, и, как одежду, Ты переменишь их, и изменятся;
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 но Ты - тот же, и лета Твои не кончатся.
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Сыны рабов Твоих будут жить, и семя их утвердится пред лицем Твоим.
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

< Псалтирь 102 >