< Притчи 27 >

1 Не хвались завтрашним днем, потому что не знаешь, что родит тот день.
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 Пусть хвалит тебя другой, а не уста твои, - чужой, а не язык твой.
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 Тяжел камень, весок и песок; но гнев глупца тяжелее их обоих.
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 Жесток гнев, неукротима ярость; но кто устоит против ревности?
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
5 Лучше открытое обличение, нежели скрытая любовь.
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
6 Искренни укоризны от любящего, и лживы поцелуи ненавидящего.
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 Сытая душа попирает и сот, а голодной душе все горькое сладко.
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 Как птица, покинувшая гнездо свое, так человек, покинувший место свое.
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 Масть и курение радуют сердце; так сладок всякому друг сердечным советом своим.
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 Не покидай друга твоего и друга отца твоего, и в дом брата твоего не ходи в день несчастья твоего: лучше сосед вблизи, нежели брат вдали.
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 Будь мудр, сын мой, и радуй сердце мое; и я буду иметь, что отвечать злословящему меня.
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 Благоразумный видит беду и укрывается; а неопытные идут вперед и наказываются.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 Возьми у него платье его, потому что он поручился за чужого, и за стороннего возьми от него залог.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 Кто громко хвалит друга своего с раннего утра, того сочтут за злословящего.
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
15 Непрестанная капель в дождливый день и сварливая жена - равны:
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
16 кто хочет скрыть ее, тот хочет скрыть ветер и масть в правой руке своей, дающую знать о себе.
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
17 Железо железо острит, и человек изощряет взгляд друга своего.
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 Кто стережет смоковницу, тот будет есть плоды ее; и кто бережет господина своего, тот будет в чести.
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 Как в воде лицо - к лицу, так сердце человека - к человеку.
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 Преисподняя и Аваддон - ненасытимы; так ненасытимы и глаза человеческие. (Sheol h7585)
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
21 Что плавильня - для серебра, горнило - для золота, то для человека уста, которые хвалят его. Сердце беззаконника ищет зла, сердце же правое ищет знания.
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 Толки глупого в ступе пестом вместе с зерном, не отделится от него глупость его.
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 Хорошо наблюдай за скотом твоим, имей попечение о стадах;
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 потому что богатство не навек, да и власть разве из рода в род?
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 Прозябает трава, и является зелень, и собирают горные травы.
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 Овцы - на одежду тебе, и козлы - на покупку поля.
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 И довольно козьего молока в пищу тебе, в пищу домашним твоим и на продовольствие служанкам твоим.
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.

< Притчи 27 >