< Числа 7 >

1 Когда Моисей поставил скинию, и помазал ее, и освятил ее и все принадлежности ее, и жертвенник и все принадлежности его, и помазал их и освятил их,
Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
2 тогда пришли двенадцать начальников Израилевых, главы се- мейств их, начальники колен, заведовавшие исчислением,
Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
3 и представили приношение свое пред Господа, шесть крытых повозок и двенадцать волов, по одной повозке от двух начальников и по одному волу от каждого, и представили сие пред скинию.
Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
4 И сказал Господь Моисею, говоря:
Yehova anawuza Mose kuti,
5 возьми от них; это будет для отправления работ при скинии собрания; и отдай это левитам, смотря по роду службы их.
“Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
6 И взял Моисей повозки и волов, и отдал их левитам:
Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
7 две повозки и четырех волов отдал сынам Гирсоновым, по роду служб их:
Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
8 и четыре повозки и восемь волов отдал сынам Мерариным, по роду служб их, под надзором Ифамара, сына Аарона, священника;
ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
9 а сынам Каафовым не дал, потому что служба их - носить святилище; на плечах они должны носить.
Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
10 И принесли начальники жертвы освящения жертвенника в день помазания его, и представили начальники приношение свое пред жертвенник.
Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
11 И сказал Господь Моисею: по одному начальнику в день пусть приносят приношение свое для освящения жертвенника.
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
12 В первый день принес приношение свое Наассон, сын Аминадавов, от колена Иудина;
Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
13 приношение его было: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
14 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
15 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
16 один козел в жертву за грех,
mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
17 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов, пять однолетних агнцев; вот приношение Наассона, сына Аминадавова.
ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
18 Во второй день принес Нафанаил, сын Цуара, начальник колена Иссахарова;
Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
19 он принес от себя приношение: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одну серебряную чашу в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
20 одну золотую кадильницу в десять сиклей, наполненную курением,
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
21 одного тельца, одного овна, одного однолетнего агнца, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
22 одного козла в жертву за грех,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
23 и в жертву мирную двух волов, пять овнов, пять козлов, пять однолетних агнцев; вот приношение Нафанаила, сына Цуарова.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
24 В третий день начальник сынов Завулоновых Елиав, сын Хелона;
Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
25 приношение его: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
26 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
27 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
28 один козел в жертву за грех,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
29 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов, пять однолетних агнцев; вот приношение Елиава, сына Хелонова.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
30 В четвертый день начальник сынов Рувимовых Елицур, сын Шедеуров;
Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
31 приношение его: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
32 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
33 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
34 один козел в жертву за грех,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
35 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов и пять однолетних агнцев; вот приношение Елицура, сына Шедеурова.
ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
36 В пятый день начальник сынов Симеоновых Шелумиил, сын Цуришаддая;
Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
37 приношение его: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
38 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
39 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
40 один козел в жертву за грех,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
41 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов и пять однолетних агнцев; вот приношение Шелумиила, сына Цуришаддаева.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
42 В шестой день начальник сынов Гадовых Елиасаф, сын Регуила;
Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
43 приношение его: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
44 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
45 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
46 один козел в жертву за грех,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
47 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов и пять однолетних агнцев; вот приношение Елиасафа, сына Регуилова.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
48 В седьмой день начальник сынов Ефремовых Елишама, сын Аммиуда.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
49 Приношение его: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
50 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
51 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
52 один козел в жертву за грех,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
53 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов, пять однолетних агнцев; вот приношение Елишамы, сына Аммиудова.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
54 В восьмой день начальник сынов Манассииных Гамалиил, сын Педацура.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
55 Приношение его: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
56 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
57 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
58 один козел в жертву за грех,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
59 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов, пять однолетних агнцев; вот приношение Гамалиила, сына Педацурова.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
60 В девятый день начальник сынов Вениаминовых Авидан, сын Гидеония;
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
61 приношение его: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
62 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
63 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
64 один козел в жертву за грех,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
65 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов, пять однолетних агнцев; вот приношение Авидана, сына Гидеониева.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
66 В десятый день начальник сынов Дановых Ахиезер, сын Аммишаддая;
Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
67 приношение его: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
68 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
69 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
70 один козел в жертву за грех,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
71 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов, пять однолетних агнцев; вот приношение Ахиезера, сына Аммишаддаева.
ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
72 В одиннадцатый день начальник сынов Асировых Пагиил, сын Охрана;
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
73 приношение его: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
74 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
75 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
76 один козел в жертву за грех,
mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
77 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов, пять однолетних агнцев; вот приношение Пагиила, сына Охранова.
ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
78 В двенадцатый день начальник сынов Неффалимовых Ахира, сын Енана;
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
79 приношение его: одно серебряное блюдо, весом в сто тридцать сиклей, одна серебряная чаша в семьдесят сиклей, по сиклю священному, наполненные пшеничною мукою, смешанною с елеем, в приношение хлебное,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
80 одна золотая кадильница в десять сиклей, наполненная курением,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
81 один телец, один овен, один однолетний агнец, во всесожжение,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
82 один козел в жертву за грех,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
83 и в жертву мирную два вола, пять овнов, пять козлов, пять однолетних агнцев; вот приношение Ахиры, сына Енанова.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
84 Вот приношения от начальников Израилевых при освящении жертвенника в день помазания его: двенадцать серебряных блюд, двенадцать серебряных чаш, двенадцать золотых кадильниц;
Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
85 по сто тридцати сиклей серебра в каждом блюде и по семидесяти в каждой чаше: итак всего серебра в сих сосудах две тысячи четыреста сиклей, по сиклю священному;
Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
86 золотых кадильниц, наполненных курением, двенадцать, в каждой кадильнице по десяти сиклей, по сиклю священному: всего золота в кадильницах сто двадцать сиклей;
Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
87 во всесожжение всего двенадцать тельцов из скота крупного, двенадцать овнов, двенадцать однолетних агнцев и при них хлебное приношение, и в жертву за грех двенадцать козлов,
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
88 и в жертву мирную всего из крупного скота двадцать четыре тельца, шестьдесят овнов, шестьдесят однолетних козлов, шестьдесят однолетних агнцев без порока; вот приношения при освящении жертвенника после помазания его.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
89 Когда Моисей входил в скинию собрания, чтобы говорить с Господом, слышал голос, говорящий ему с крышки, которая над ковчегом откровения между двух херувимов, и он говорил ему.
Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.

< Числа 7 >