< Числа 29 >

1 И в седьмой месяц, в первый день месяца, да будет у вас священное собрание; никакой работы не работайте; пусть будет это у вас день трубного звука;
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 и приносите всесожжение в приятное благоухание Господу: одного тельца, одного овна, семь однолетних агнцев, без порока,
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 и при них в приношение хлебное пшеничной муки, смешанной с елеем, три десятых части ефы на тельца, две десятых части ефы на овна,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 и одну десятую часть ефы на каждого из семи агнцев,
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 и одного козла в жертву за грех, для очищения вас,
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 сверх новомесячного всесожжения и хлебного приношения его, и сверх постоянного всесожжения и хлебного приношения его, и возлияний их, по уставу, в приятное благоухание Господу.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 И в десятый день сего седьмого месяца пусть будет у вас священное собрание: смиряйте тогда души ваши и никакого дела не делайте;
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 и приносите всесожжение Господу в приятное благоухание: одного тельца, одного овна, семь однолетних агнцев; без порока пусть будут они у вас;
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 и при них в приношение хлебное пшеничной муки, смешанной с елеем, три десятых части ефы на тельца, две десятых части ефы на овна,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 и по десятой части ефы на каждого из семи агнцев,
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 и одного козла в жертву за грех, для очищения вас, сверх жертвы за грех, приносимой в день очищения, и сверх всесожжения постоянного и хлебного приношения его, и возлияния их, по уставу приносимых в приятное благоухание, в жертву Господу.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 И в пятнадцатый день седьмого месяца пусть будет у вас священное собрание; никакой работы не работайте и празднуйте праздник Господень семь дней;
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 и приносите всесожжение, жертву, приятное благоухание Господу: тринадцать тельцов, двух овнов, четырнадцать однолетних агнцев; без порока пусть будут они;
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 и при них в приношение хлебное пшеничной муки, смешанной с елеем, три десятых части ефы на каждого из тринадцати тельцов, две десятых части ефы на каждого из двух овнов,
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 и по десятой части ефы на каждого из четырнадцати агнцев,
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 и одного козла в жертву за грех, сверх всесожжения постоянного и хлебного приношения его и возлияния его.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 И во второй день двенадцать тельцов, двух овнов, четырнадцать однолетних агнцев, без порока,
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 и при них приношение хлебное и возлияние для тельцов, овнов и агнцев, по числу их, по уставу,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 и одного козла в жертву за грех, сверх всесожжения постоянного и хлебного приношения и возлияния их.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 И в третий день одиннадцать тельцов, двух овнов, четырнадцать однолетних агнцев, без порока,
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 и при них приношение хлебное и возлияние для тельцов, овнов и агнцев, по числу их, по уставу,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 и одного козла в жертву за грех, сверх всесожжения постоянного и хлебного приношения и возлияния его.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 И в четвертый день десять тельцов, двух овнов, четырнадцать однолетних агнцев, без порока,
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 и при них приношение хлебное и возлияние для тельцов, овнов и агнцев, по числу их, по уставу,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 и одного козла в жертву за грех, сверх всесожжения постоянного и хлебного приношения и возлияния его.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 И в пятый день девять тельцов, двух овнов, четырнадцать однолетних агнцев, без порока,
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 и при них приношение хлебное и возлияние для тельцов, овнов и агнцев, по числу их, по уставу,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 и одного козла в жертву за грех, сверх всесожжения постоянного и хлебного приношения и возлияния его.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 И в шестой день восемь тельцов, двух овнов, четырнадцать однолетних агнцев, без порока,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 и при них приношение хлебное и возлияние для тельцов, овнов и агнцев, по числу их, по уставу,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 и одного козла в жертву за грех, сверх всесожжения постоянного и хлебного приношения и возлияния его.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 И в седьмой день семь тельцов, двух овнов, четырнадцать однолетних агнцев, без порока,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 и при них приношение хлебное и возлияние для тельцов, овнов и агнцев, по числу их, по уставу,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 и одного козла в жертву за грех, сверх всесожжения постоянного и хлебного приношения и возлияния его.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 В восьмой день пусть будет у вас отдание праздника; никакой работы не работайте;
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 и приносите всесожжение, жертву, приятное благоухание Господу: одного тельца, одного овна, семь однолетних агнцев, без порока,
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 и при них приношение хлебное и возлияние для тельца, овна и агнцев по числу их, по уставу,
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 и одного козла в жертву за грех, сверх всесожжения постоянного и приношения хлебного и возлияния его.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Приносите это Господу в праздники ваши, сверх приносимых вами, по обету или по усердию, всесожжений ваших и хлебных приношений ваших, и возлияний ваших и мирных жертв ваших.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 И пересказал Моисей сынам Израилевым все, что повелел Господь Моисею.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< Числа 29 >