< От Луки 1 >

1 Как уже многие начали составлять повествования о совершенно известных между нами событиях,
Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
2 как передали нам то бывшие с самого начала очевидцами и служителями Слова,
monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
3 то рассудилось и мне, по тщательном исследовании всего сначала, по порядку описать тебе, достопочтенный Феофил,
Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
4 чтобы ты узнал твердое основание того учения, в котором был наставлен.
kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
5 Во дни Ирода, царя Иудейского, был священник из Авиевой чреды, именем Захария, и жена его из рода Ааронова, имя ей Елисавета.
Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
6 Оба они были праведны пред Богом, поступая по всем заповедям и уставам Господним беспорочно.
Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
7 У них не было детей, ибо Елисавета была неплодна, и оба были уже в летах преклонных.
Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
8 Однажды, когда он в порядке своей чреды служил пред Богом,
Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
9 по жребию, как обыкновенно было у священников, досталось ему войти в храм Господень для каждения,
Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
10 а все множество народа молилось вне во время каждения, -
Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
11 тогда явился ему Ангел Господень, стоя по правую сторону жертвенника кадильного.
Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
12 Захария, увидев его, смутился, и страх напал на него.
Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
13 Ангел же сказал ему: не бойся, Захария, ибо услышана молитва твоя, и жена твоя Елисавета родит тебе сына, и наречешь ему имя: Иоанн;
Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
14 и будет тебе радость и веселие, и многие о рождении его возрадуются,
Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
15 ибо он будет велик пред Господом; не будет пить вина и сикера, и Духа Святаго исполнится еще от чрева матери своей;
chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
16 и многих из сынов Израилевых обратит к Господу Богу их;
Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
17 и предъидет пред Ним в духе и силе Илии, чтобы возвратить сердца отцов детям, и непокоривым образ мыслей праведников, дабы представить Господу народ приготовленный.
Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
18 И сказал Захария Ангелу: по чему я узнаю это? ибо я стар, и жена моя в летах преклонных.
Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
19 Ангел сказал ему в ответ: я Гавриил, предстоящий пред Богом, и послан говорить с тобою и благовестить тебе сие;
Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
20 и вот, ты будешь молчать и не будешь иметь возможности говорить до того дня, как это сбудется, за то, что ты не поверил словам моим, которые сбудутся в свое время.
Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
21 Между тем народ ожидал Захарию и дивился, что он медлит в храме.
Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
22 Он же, выйдя, не мог говорить к ним; и они поняли, что он видел видение в храме; и он объяснялся с ними знаками, и оставался нем.
Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
23 А когда окончились дни службы его, возвратился в дом свой.
Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
24 После сих дней зачала Елисавета, жена его, и таилась пять месяцев и говорила:
Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
25 так сотворил мне Господь во дни сии, в которые призрел на меня, чтобы снять с меня поношение между людьми.
Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
26 В шестой же месяц послан был Ангел Гавриил от Бога в город Галилейский, называемый Назарет,
Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
27 к Деве, обрученной мужу, именем Иосифу, из дома Давидова; имя же Деве: Мария.
kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
28 Ангел, войдя к Ней, сказал: радуйся, Благодатная! Господь с Тобою; благословенна Ты между женами.
Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
29 Она же, увидев его, смутилась от слов его и размышляла, что бы это было за приветствие.
Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
30 И сказал Ей Ангел: не бойся, Мария, ибо Ты обрела благодать у Бога;
Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
31 и вот, зачнешь во чреве, и родишь Сына, и наречешь Ему имя: Иисус.
Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
32 Он будет велик и наречется Сыном Всевышнего, и даст Ему Господь Бог престол Давида, отца Его;
Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
33 и будет царствовать над домом Иакова во веки, и Царству Его не будет конца. (aiōn g165)
ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
34 Мария же сказала Ангелу: как будет это, когда я мужа не знаю?
Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
35 Ангел сказал Ей в ответ: Дух Святый найдет на Тебя, и сила Всевышнего осенит Тебя; посему и рождаемое Святое наречется Сыном Божиим.
Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
36 Вот и Елисавета, родственница Твоя, называемая неплодною, и она зачала сына в старости своей, и ей уже шестой месяц,
Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
37 ибо у Бога не останется бессильным никакое слово.
Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
38 Тогда Мария сказала: се, Раба Господня; да будет Мне по слову твоему. И отошел от Нее Ангел.
Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
39 Встав же Мария во дни сии, с поспешностью пошла в нагорную страну, в город Иудин,
Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
40 и вошла в дом Захарии, и приветствовала Елисавету.
kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
41 Когда Елисавета услышала приветствие Марии, взыграл младенец во чреве ее; и Елисавета исполнилась Святаго Духа,
Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
42 и воскликнула громким голосом, и сказала: благословенна Ты между женами, и благословен плод чрева Твоего!
Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
43 И откуда это мне, что пришла Матерь Господа моего ко мне?
Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
44 Ибо когда голос приветствия Твоего дошел до слуха моего, взыграл младенец радостно во чреве моем.
Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
45 И блаженна Уверовавшая, потому что совершится сказанное ей от Господа.
Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
46 И сказала Мария: величает душа моя Господа,
Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 и возрадовался дух мой о Боге, Спасителе моем,
Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 что призрел Он на смирение рабы своей, ибо отныне будут ублажать меня все роды;
pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 что сотворил мне величие Сильный, и свято имя Его;
pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
50 и милость Его в роды родов к боящимся Его;
Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
51 явил силу мышцы Своей; рассеял надменных помышлениями сердца их;
Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 низложил сильных с престолов, и вознес смиренных;
Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
53 алчущих исполнил благ, и богатящихся отпустил ни с чем;
Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 воспринял Израиля, отрока Своего, воспомянув милость,
Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
55 как говорил отцам нашим, к Аврааму и семени его до века. (aiōn g165)
Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
56 Пребыла же Мария с нею около трех месяцев, и возвратилась в дом свой.
Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
57 Елисавете же настало время родить, и она родила сына.
Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
58 И услышали соседи и родственники ее, что возвеличил Господь милость Свою над нею, и радовались с нею.
Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
59 В восьмой день пришли обрезать младенца и хотели назвать его, по имени отца его, Захариею.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
60 На это мать его сказала: нет, а назвать его Иоанном.
koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
61 И сказали ей: никого нет в родстве твоем, кто назывался бы сим именем.
Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
62 И спрашивали знаками у отца его, как бы он хотел назвать его.
Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
63 Он потребовал дощечку и написал: Иоанн имя ему. И все удивились.
Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
64 И тотчас разрешились уста его и язык его, и он стал говорить, благословляя Бога.
Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
65 И был страх на всех живущих вокруг них; и рассказывали обо всем этом по всей нагорной стране Иудейской.
Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
66 Все слышавшие положили это на сердце своем и говорили: что будет младенец сей? И рука Господня была с ним.
Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
67 И Захария, отец его, исполнился Святаго Духа и пророчествовал, говоря:
Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
68 благословен Господь Бог Израилев, что посетил народ Свой и сотворил избавление ему,
“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
69 и воздвиг рог спасения нам в дому Давида, отрока Своего,
Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
70 как возвестил устами бывших от века святых пророков Своих, (aiōn g165)
(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
71 что спасет нас от врагов наших и от руки всех ненавидящих нас;
chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
72 сотворит милость с отцами нашими и помянет святой завет Свой,
kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
73 клятву, которою клялся Он Аврааму, отцу нашему, дать нам,
lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
74 небоязненно, по избавлении от руки врагов наших,
kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
75 служить Ему в святости и правде пред Ним, во все дни жизни нашей.
mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
76 И ты, младенец, наречешься пророком Всевышнего, ибо предъидешь пред лицем Господа приготовить пути Ему,
“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
77 дать уразуметь народу Его спасение в прощении грехов их,
kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
78 по благоутробному милосердию Бога нашего, которым посетил нас Восток свыше,
chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
79 просветить сидящих во тьме и тени смертной, направить ноги наши на путь мира.
kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
80 Младенец же возрастал и укреплялся духом, и был в пустынях до дня явления своего Израилю.
Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.

< От Луки 1 >