< Иисус Навин 21 >

1 Начальники поколений левитских пришли к Елеазару священнику и к Иисусу, сыну Навину, и к начальникам поколений сынов Израилевых,
Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
2 и говорили им в Силоме, в земле Ханаанской, и сказали: Господь повелел чрез Моисея дать нам города для жительства и предместья их для скота нашего.
ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
3 И дали сыны Израилевы левитам из уделов своих, по повелению Господню, сии города с предместьями их.
Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
4 Вышел жребий племенам Каафовым; и досталось по жребию сынам Аарона священника, левитам, от колена Иудина, и от колена Симеонова, и от колена Вениаминова, тринадцать городов;
Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
5 а прочим сынам Каафа от племен колен Ефремова, и от колена Данова, и от половины колена Манассиина, по жребию, досталось десять городов;
Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
6 сынам Гирсоновым - от племен колена Иссахарова, и от колена Асирова, и от колена Неффалимова, и от половины колена Манассиина в Васане, по жребию, досталось тринадцать городов;
Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
7 сынам Мерариным, по их племенам, от колена Рувимова, от колена Гадова и от колена Завулонова - двенадцать городов.
Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
8 И отдали сыны Израилевы левитам сии города с предместьями их, как повелел Господь чрез Моисея, по жребию.
Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
9 От колена сынов Иудиных, и от колена сынов Симеоновых, и от колена сынов Вениаминовых дали города, которые здесь названы по имени:
Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
10 сынам Аарона, из племен Каафовых, из сынов Левия так как жребий их был первый,
ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
11 дали Кириаф-Арбы, отца Енакова, иначе Хеврон, на горе Иудиной, и предместья его вокруг его;
Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
12 а поле сего города и села его отдали в собственность Халеву, сыну Иефонниину.
Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
13 Итак сынам Аарона священника дали город убежища для убийцы - Хеврон и предместья его, Ливну и предместья ее,
Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
14 Иаттир и предместья его, Ештемо и предместья его,
Yatiri, Esitemowa,
15 Холон и предместья его, Давир и предместья его,
Holoni, Debri,
16 Аин и предместья его, Ютту и предместья ее, Беф-Шемеш и предместья его: девять городов от двух колен сих;
Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
17 а от колена Вениаминова: Гаваон и предместья его, Геву и предместья ее,
Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
18 Анафоф и предместья его, Алмон и предместья его: четыре города.
Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
19 Всех городов сынам Аароновым, священникам, досталось тринадцать городов с предместьями их.
Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
20 И племенам сынов Каафовых, левитов, прочим из сынов Каафовых, по жребию их, достались города от колена Ефремова;
Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
21 дали им город убежища для убийцы - Сихем и предместья его, на горе Ефремовой, Гезер и предместья его,
Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
22 Кивцаим и предместья его, Беф-Орон и предместья его: четыре города;
Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
23 от колена Данова: Елфеке и предместья его, Гиввефон и предместья его,
Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
24 Аиалон и предместья его, Гаф-Риммон и предместья его: четыре города;
Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
25 от половины колена Манассиина: Фаанах и предместья его, Гаф-Риммон и предместья его: два города.
Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
26 Всех городов с предместьями их прочим племенам сынов Каафовых досталось десять.
Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
27 А сынам Гирсоновым, из племен левитских дали: от половины колена Манассиина город убежища для убийцы - Голан в Васане и предместья его, и Беештеру и предместья ее: два города;
Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
28 от колена Иссахарова: Кишион и предместья его, Давраф и предместья его,
Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
29 Иармуф и предместья его, Ен-Ганним и предместья его: четыре города;
Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
30 от колена Асирова: Мишал и предместья его, Авдон и предместья его,
Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
31 Хелкаф и предместья его, Рехов и предместья его: четыре города;
Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
32 от колена Неффалимова город убежища для убийцы - Кедес в Галилее и предместья его, Хамоф-Дор и предместья его, Карфан и предместья его: три города.
Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
33 Всех городов сынам Гирсоновым, по племенам их, досталось тринадцать городов с предместьями их.
Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
34 Племенам сынов Мерариных, остальным левитам, дали: от колена Завулонова Иокнеам и предместья его, Карфу и предместья ее,
Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
35 Димну и предместья ее, Нагалал и предместья его: четыре города;
Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
36 по ту сторону Иордана против Иерихона от колена Рувимова дан город убежища для убийцы Бецер в пустыне Мисор и предместья его, Иааца и предместья ее,
Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
37 Кедемоф и предместья его, Мефааф и предместья его: четыре города;
Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
38 от колена Гадова: города убежища для убийцы - Рамоф в Галааде и предместья его, Маханаим и предместья его,
Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
39 Есевон и предместья его, Иазер и предместья его: всех городов четыре.
Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
40 Всех городов сынам Мерариным по племенам их, остальным племенам левитским, по жребию досталось двенадцать городов.
Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
41 Всех городов левитских среди владения сынов Израилевых было сорок восемь городов с предместьями их.
Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
42 При городах сих были при каждом городе предместья вокруг него: так было при всех городах сих.
Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
43 Таким образом отдал Господь Израилю всю землю, которую дать клялся отцам их, и они получили ее в наследие и поселились на ней.
Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
44 И дал им Господь покой со всех сторон, как клялся отцам их, и никто из всех врагов их не устоял против них; всех врагов их предал Господь в руки их.
Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
45 Не осталось неисполнившимся ни одно слово из всех добрых слов, которые Господь говорил дому Израилеву; все сбылось.
Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.

< Иисус Навин 21 >