< Иисус Навин 19 >

1 Второй жребий вышел Симеону, колену сынов Симеоновых, по племенам их; и был удел их среди удела сынов Иудиных.
Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
2 В уделе их были: Вирсавия или Шева, Молада,
Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
3 Хацар-Шуал, Вала и Ацем,
Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
4 Елтолад, Вефул и Хорма,
Elitoladi, Betuli, Horima,
5 Циклаг, Беф-Маркавоф и Хацар-Суса,
Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
6 Беф-Леваоф и Шарухен: тринадцать городов с их селами.
Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
7 Аин, Риммон, Ефер и Ашан: четыре города с селами их,
Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
8 и все села, которые находились вокруг городов сих даже до Ваалаф-Беера, или южной Рамы. Вот удел колена сынов Симеоновых, по племенам их.
Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
9 От участка сынов Иудиных выделен удел колену сынов Симеоновых. Так как участок сынов Иудиных был слишком велик для них, то сыны Симеоновы и получили удел среди их удела.
Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
10 Третий жребий выпал сынам Завулоновым по племенам их, и простирался предел удела их до Сарида;
Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
11 предел их восходит к морю и Марале и примыкает к Дабешефу и примыкает к потоку, который пред Иокнеамом;
Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
12 от Сарида идет назад к восточной стороне, к востоку солнца, до предела Кислоф-Фавора; отсюда идет к Даврафу и восходит к Иафии;
Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
13 отсюда проходит к востоку в Геф-Хефер, в Итту-Кацин, и идет к Риммону, Мифоару и Нее;
Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
14 и поворачивает предел от севера к Ханнафону и оканчивается долиною Ифтах-Ел;
Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
15 далее: Каттаф, Нагалал, Шимрон, Идеала и Вифлеем: двенадцать городов с их селами.
Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
16 Вот удел сынов Завулоновых, по их племенам; вот города и села их.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
17 Четвертый жребий вышел Иссахару, сынам Иссахара, по племенам их;
Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
18 пределом их был: Изреель, Кесуллоф и Сунем,
Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
19 Хафараим, Шион и Анахараф,
Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
20 Раввиф, Кишион и Авец,
Rabiti, Kisoni, Ebezi,
21 Ремеф, Ен-Ганним, Ен-Хадда и Беф-Пацец;
Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
22 и примыкает предел к Фавору и Шагациме и Вефсамису, и оканчивается предел их у Иордана: шестнадцать городов с селами их.
Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
23 Вот удел колена сынов Иссахаровых по племенам их; вот города и села их.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
24 Пятый жребий вышел колену сынов Асировых, по племенам их;
Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
25 пределом их были: Хелкаф, Хали, Ветен и Ахсаф,
Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
26 Аламелех, Амад и Мишал; и примыкает предел к Кармилу с западной стороны и к Шихор-Ливнафу;
Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
27 потом идет назад к востоку солнца в Беф-Дагон, и примыкает к Завулону и к долине Ифтах-Ел с севера, и входит в пределы Асафы в Беф-Емек и Неиел, и идет у Кавула, с левой стороны;
Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
28 далее: Еврон, Рехов, Хаммон и Кана, до Сидона великого;
Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
29 потом предел возвращается к Раме до укрепленного города Тира, и поворачивает предел к Хоссе, и оканчивается у моря, в местечке Ахзиве;
Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
30 далее: Умма, Афек и Рехов: двадцать два города с селами их.
Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
31 Вот удел колена сынов Асировых, по племенам их; вот города и села их.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
32 Шестой жребий вышел сынам Неффалима, сынам Неффалима по племенам их;
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
33 предел их шел от Хелефа и от дубравы, что в Цананниме, к Адами-Некеву и Иавнеилу, до Лаккума, и оканчивался у Иордана;
Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
34 отсюда возвращается предел на запад к Азноф-Фавору и идет оттуда к Хуккоку, и примыкает к Завулону с юга, и к Асиру примыкает с запада, и к Иуде у Иордана, от востока солнца.
Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
35 Города укрепленные: Циддим, Цер, Хамаф, Раккаф и Хиннереф,
Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
36 Адама, Рама и Асор,
Adama, Rama, Hazori,
37 Кедес, Едрея и Ен-Гацор,
Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
38 Иреон, Мигдал-Ел, Хорем, Беф-Анаф и Вефсамис: девятнадцать городов с их селами.
Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
39 Вот удел колена сынов Неффалимовых по племенам их; вот города и села их.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
40 Колену сынов Дановых, по племенам их, вышел жребий седьмой;
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
41 пределом удела их были: Цора, Ештаол и Ир-Шемеш,
Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
42 Шаалаввин, Аиалон и Ифла,
Saalabini, Ayaloni, Itira,
43 Елон, Фимнафа и Екрон,
Eloni, Timna, Ekroni,
44 Елтеке, Гиввефон и Ваалаф,
Eliteke, Gibetoni, Baalati,
45 Игуд, Бене-Верак и Гаф-Риммон,
Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
46 Ме-Иаркон и Ракон с пределом близ Иоппии. И вышел предел сынов Дановых мал для них.
Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
47 И сыны Дановы пошли войною на Ласем и взяли его, и поразили его мечом, и получили его в наследие, и поселились в нем, и назвали Ласем Даном по имени Дана, отца своего. Аморреи оставались жить в Еломе и Саламине, но рука Ефремова одолела их, и сделались они данниками ему.
Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
48 Вот удел колена сынов Дановых, по племенам их; вот города и села их. Сыны Дановы не истребили Аморреев, которые стеснили их на горе, и не давали им Аморреи выходить на долину и отняли у них предел их участка.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
49 Когда окончили разделение земли, по пределам ее, тогда сыны Израилевы дали среди себя удел Иисусу, сыну Навину:
Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
50 по повелению Господню дали ему город Фамнаф-Сараи, которого он просил, на горе Ефремовой; и построил он город и жил в нем.
Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
51 Вот уделы, которые Елеазар священник, Иисус, сын Навин, и начальники поколений разделили коленам сынов Израилевых, по жребию, в Силоме, пред лицом Господним, у входа скинии собрания. И кончили разделение земли.
Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.

< Иисус Навин 19 >