< Иисус Навин 17 >

1 И выпал жребий колену Манассии, так как он был первенец Иосифа. Махиру, первенцу Манассии, отцу Галаада, который был храбр на войне, достался Галаад и Васан.
Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
2 Достались уделы и прочим сынам Манассии, по племенам их, и сынам Авиезера, и сынам Хелека, и сынам Асриила, и сынам Шехема, и сынам Хефера, и сынам Шемиды. Вот дети Манассии, сына Иосифова, мужеского пола, по племенам их.
Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
3 У Салпаада же, сына Хеферова, сына Галаадова, сына Махирова, сына Манассиина, не было сыновей, а только дочери. Вот имена дочерей его: Махла, Ноа, Хогла, Милка и Фирца.
Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
4 Они пришли к священнику Елеазару и к Иисусу, сыну Навину, и к начальникам, и сказали: Господь повелел Моисею дать нам удел между братьями нашими. И дан им удел, по повелению Господню, между братьями отца их.
Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
5 И выпало Манассии десять участков, кроме земли Галаадской и Васанской, которая за Иорданом;
Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
6 ибо дочери сынов Манассии получили удел среди сыновей его, а земля Галаадская досталась прочим сыновьям Манассии.
chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
7 Предел сынов Манассии идет от Асира к Михмефафу, который против Сихема; отсюда предел идет направо к жителям Ен-Таппуаха.
Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
8 Земля Таппуах досталась Манассии, а город Таппуах у предела Манассиина - сынам Ефремовым.
(Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
9 Отсюда предел нисходит к потоку Кане, с южной стороны потока. Города сии принадлежат Ефрему, хотя находятся среди городов Манассии. Предел Манассии - на северной стороне потока и оканчивается морем.
Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
10 Что к югу, то Ефремово, а что к северу, то Манассиино; море же было пределом их; к Асиру примыкали они с северной стороны и к Иссахару с восточной.
Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
11 У Иссахара и Асира принадлежат Манассии Беф-Сан и зависящие от него места, Ивлеам и зависящие от него места, жители Дора и зависящие от него места, жители Ен-Дора и зависящие от него места, жители Фаанаха и зависящие от него места, жители Мегиддона и зависящие от него места, и третья часть Нафефа с селами его.
Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
12 Сыны Манассиины не могли выгнать жителей городов сих, и Хананеи остались жить в земле сей.
Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
13 Когда же сыны Израилевы пришли в силу, тогда Хананеев сделали они данниками, но изгнать не изгнали их.
Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
14 Сыны Иосифа говорили Иисусу и сказали: почему ты дал мне в удел один жребий и один участок, тогда как я многолюден, потому что так благословил меня Господь?
Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
15 Иисус сказал им: если ты многолюден, то пойди в леса и там, в земле Ферезеев и Рефаимов, расчисти себе место, если гора Ефремова для тебя тесна.
Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
16 Сыны Иосифа сказали: не останется за нами гора, потому что железные колесницы у всех Хананеев, живущих на долине, как у тех, которые в Беф-Сане и в зависящих от него местах, так и у тех, которые на долине Изреельской.
Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
17 Но Иисус сказал дому Иосифову, Ефрему и Манассии: ты многолюден и сила у тебя велика; не один жребий будет у тебя:
Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
18 и гора будет твоею, и лес сей; ты расчистишь его, и он будет твой до самого конца его; ибо ты изгонишь Хананеев, хотя у них колесницы железные, и хотя они сильны, ты одолеешь их.
dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”

< Иисус Навин 17 >