< Иов 8 >

1 И отвечал Вилдад Савхеянин и сказал:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 долго ли ты будешь говорить так? - слова уст твоих бурный ветер!
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Неужели Бог извращает суд, и Вседержитель превращает правду?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Если сыновья твои согрешили пред Ним, то Он и предал их в руку беззакония их.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Если же ты взыщешь Бога и помолишься Вседержителю,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 и если ты чист и прав, то Он ныне же встанет над тобою и умиротворит жилище правды твоей.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 И если вначале у тебя было мало, то впоследствии будет весьма много.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Ибо спроси у прежних родов и вникни в наблюдения отцов их;
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 а мы - вчерашние и ничего не знаем, потому что наши дни на земле тень.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Вот, они научат тебя, скажут тебе и от сердца своего произнесут слова:
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 поднимается ли тростник без влаги? растет ли камыш без воды?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Еще он в свежести своей и не срезан, а прежде всякой травы засыхает.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Таковы пути всех забывающих Бога, и надежда лицемера погибнет;
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 упование его подсечено, и уверенность его - дом паука.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Обопрется о дом свой и не устоит; ухватится за него и не удержится.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Зеленеет он пред солнцем, за сад простираются ветви его;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 в кучу камней вплетаются корни его, между камнями врезываются.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Но когда вырвут его с места его, оно откажется от него: “я не видало тебя!”
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Вот радость пути его! а из земли вырастают другие.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Видишь, Бог не отвергает непорочного и не поддерживает руки злодеев.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Он еще наполнит смехом уста твои и губы твои радостным восклицанием.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Ненавидящие тебя облекутся в стыд, и шатра нечестивых не станет.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Иов 8 >