< Иов 40 >

1 И продолжал Господь и сказал Иову:
Yehova anati kwa Yobu:
2 будет ли состязающийся со Вседержителем еще учить? Обличающий Бога пусть отвечает Ему.
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 И отвечал Иов Господу и сказал:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 вот, я ничтожен; что буду я отвечать Тебе? Руку мою полагаю на уста мои.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Однажды я говорил, - теперь отвечать не буду, даже дважды, но более не буду.
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 И отвечал Господь Иову из бури и сказал:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 препояшь, как муж, чресла твои: Я буду спрашивать тебя, а ты объясняй Мне.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Ты хочешь ниспровергнуть суд Мой, обвинить Меня, чтобы оправдать себя?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Такая ли у тебя мышца, как у Бога? И можешь ли возгреметь голосом, как Он?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Укрась же себя величием и славою, облекись в блеск и великолепие;
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 излей ярость гнева твоего, посмотри на все гордое и смири его;
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 взгляни на всех высокомерных и унизь их, и сокруши нечестивых на местах их;
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 зарой всех их в землю и лица их покрой тьмою.
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Тогда и Я признаю, что десница твоя может спасать тебя.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Вот бегемот, которого Я создал, как и тебя; он ест траву, как вол;
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 вот, его сила в чреслах его и крепость его в мускулах чрева его;
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 поворачивает хвостом своим, как кедром; жилы же на бедрах его переплетены;
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 ноги у него, как медные трубы; кости у него, как железные прутья;
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 это - верх путей Божиих; только Сотворивший его может приблизить к нему меч Свой;
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 горы приносят ему пищу, и там все звери полевые играют;
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 он ложится под тенистыми деревьями, под кровом тростника и в болотах;
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 тенистые дерева покрывают его своею тенью; ивы при ручьях окружают его;
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 вот, он пьет из реки и не торопится; остается спокоен, хотя бы Иордан устремился ко рту его.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Возьмет ли кто его в глазах его и проколет ли ему нос багром?
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?

< Иов 40 >