< Иов 33 >

1 Итак слушай, Иов, речи мои и внимай всем словам моим.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Вот, я открываю уста мои, язык мой говорит в гортани моей.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 Слова мои от искренности моего сердца, и уста мои произнесут знание чистое.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 Дух Божий создал меня, и дыхание Вседержителя дало мне жизнь.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 Если можешь, отвечай мне и стань передо мною.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Вот я, по желанию твоему, вместо Бога. Я образован также из брения;
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 поэтому страх передо мною не может смутить тебя, и рука моя не будет тяжела для тебя.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Ты говорил в уши мои, и я слышал звук слов:
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 чист я, без порока, невинен я, и нет во мне неправды;
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 а Он нашел обвинение против меня и считает меня Своим противником;
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 поставил ноги мои в колоду, наблюдает за всеми путями моими.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Вот в этом ты не прав, отвечаю тебе, потому что Бог выше человека.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Для чего тебе состязаться с Ним? Он не дает отчета ни в каких делах Своих.
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Бог говорит однажды и, если того не заметят, в другой раз:
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 во сне, в ночном видении, когда сон находит на людей, во время дремоты на ложе.
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Тогда Он открывает у человека ухо и запечатлевает Свое наставление,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 чтобы отвести человека от какого-либо предприятия и удалить от него гордость,
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 чтобы отвести душу его от пропасти и жизнь его от поражения мечом.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Или он вразумляется болезнью на ложе своем и жестокою болью во всех костях своих, -
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 и жизнь его отвращается от хлеба и душа его от любимой пищи.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Плоть на нем пропадает, так что ее не видно, и показываются кости его, которых не было видно.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 И душа его приближается к могиле и жизнь его - к смерти.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 Если есть у него Ангел-наставник, один из тысячи, чтобы показать человеку прямой путь его, -
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Бог умилосердится над ним и скажет: освободи его от могилы; Я нашел умилостивление.
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 Тогда тело его сделается свежее, нежели в молодости; он возвратится к дням юности своей.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Будет молиться Богу, и Он - милостив к нему; с радостью взирает на лице его и возвращает человеку праведность его.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Он будет смотреть на людей и говорить: грешил я и превращал правду, и не воздано мне;
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Он освободил душу мою от могилы, и жизнь моя видит свет.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Вот, все это делает Бог два-три раза с человеком,
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 чтобы отвести душу его от могилы и просветить его светом живых.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Внимай, Иов, слушай меня, молчи, и я буду говорить.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Если имеешь, что сказать, отвечай; говори, потому что я желал бы твоего оправдания;
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 если же нет, то слушай меня: молчи, и я научу тебя мудрости.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Иов 33 >