< Иов 28 >

1 Так! у серебра есть источная жила, и у золота место, где его плавят.
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Железо получается из земли; из камня выплавляется медь.
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 Человек полагает предел тьме и тщательно разыскивает камень во мраке и тени смертной.
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 Вырывают рудокопный колодезь в местах, забытых ногою, спускаются вглубь, висят и зыблются вдали от людей.
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 Земля, на которой вырастает хлеб, внутри изрыта как бы огнем.
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 Камни ее - место сапфира, и в ней песчинки золота.
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 Стези туда не знает хищная птица, и не видал ее глаз коршуна;
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
8 не попирали ее скимны, и не ходил по ней шакал.
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 На гранит налагает он руку свою, с корнем опрокидывает горы;
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 в скалах просекает каналы, и все драгоценное видит глаз его;
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 останавливает течение потоков и сокровенное выносит на свет.
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 Но где премудрость обретается? и где место разума?
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 Не знает человек цены ее, и она не обретается на земле живых.
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 Бездна говорит: не во мне она; и море говорит: не у меня.
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 Не дается она за золото и не приобретается она за вес серебра;
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 не оценивается она золотом Офирским, ни драгоценным ониксом, ни сапфиром;
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 не равняется с нею золото и кристалл, и не выменяешь ее на сосуды из чистого золота.
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 А о кораллах и жемчуге и упоминать нечего, и приобретение премудрости выше рубинов.
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 Не равняется с нею топаз Ефиопский; чистым золотом не оценивается она.
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 Откуда же исходит премудрость? и где место разума?
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 Сокрыта она от очей всего живущего и от птиц небесных утаена.
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 Аваддон и смерть говорят: ушами нашими слышали мы слух о ней.
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 Бог знает путь ее, и Он ведает место ее.
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 Ибо Он прозирает до концов земли и видит под всем небом.
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 Когда Он ветру полагал вес и располагал воду по мере,
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
26 когда назначал устав дождю и путь для молнии громоносной,
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 тогда Он видел ее и явил ее, приготовил ее и еще испытал ее.
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 и сказал человеку: вот, страх Господень есть истинная премудрость, и удаление от зла - разум.
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”

< Иов 28 >