< Иов 25 >

1 И отвечал Вилдад Савхеянин и сказал:
Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 держава и страх у Него; Он творит мир на высотах Своих!
“Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
3 Есть ли счет воинствам Его? и над кем не восходит свет Его?
Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
4 И как человеку быть правым пред Богом, и как быть чистым рожденному женщиною?
Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
5 Вот даже луна, и та несветла, и звезды нечисты пред очами Его.
Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
6 Тем менее человек, который есть червь, и сын человеческий, который есть моль.
nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”

< Иов 25 >